< Salme 96 >

1 Syng HERREN en ny Sang, syng for HERREN, al Jorden,
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 syng for HERREN og lov hans Navn, fortæl om hans Frelse Dag efter Dag,
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 kundgør hans Ære blandt Folkene, hans Undere blandt alle Folkeslag!
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 Thi stor og højlovet er HERREN, forfærdelig over alle Guder;
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 thi alle Folkeslagenes Guder er Afguder, HERREN er Himlens Skaber.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 For hans Aasyn er Højhed og Hæder, Lov og Pris i hans Helligdom.
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 Giv HERREN, I Folkeslags Slægter, giv HERREN Ære og Pris,
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 giv HERREN hans Navns Ære, bring Gaver og kom til hans Forgaarde,
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 tilbed HERREN i helligt Skrud, bæv for hans Aasyn, al Jorden!
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Sig blandt Folkeslag: »HERREN har vist, han er Konge, han grundfæsted Jorden, den rokkes ikke, med Retfærd dømmer han Folkene.«
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Himlen glæde sig, Jorden juble, Havet med dets Fylde bruse,
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 Marken juble og alt, hvad den bærer! Da fryder sig alle Skovens Træer
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 for HERRENS Aasyn, thi han kommer, han kommer at dømme Jorden; han dømmer Jorden med Retfærd og Folkene i sin Trofasthed.
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

< Salme 96 >