< Salme 88 >

1 En Sang. En Salme af Koras Sønner. Til Sangmesteren. Al-mahalat-leannot. En Maskil af Ezraiten Heman. HERRE min Gud, jeg raaber om Dagen, om Natten naar mit Skrig til dig;
Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
2 lad min Bøn komme frem for dit Aasyn, til mit Klageraab laane du Øre!
Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
3 Thi min Sjæl er mæt af Lidelser, mit Liv er Dødsriget nær, (Sheol h7585)
Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
4 jeg regnes blandt dem, der sank i Graven, er blevet som den, det er ude med,
Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
5 kastet hen imellem de døde, blandt faldne, der hviler i Graven, hvem du ej mindes mere, thi fra din Haand er de revet.
Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
6 Du har lagt mig i den underste Grube, paa det mørke, det dybe Sted;
Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
7 tungt hviler din Vrede paa mig, alle dine Brændinger lod du gaa over mig. (Sela)
Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
8 Du har fjernet mine Frænder fra mig, gjort mig vederstyggelig for dem; jeg er fængslet, kan ikke gaa ud,
Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
9 mit Øje er sløvt af Vaande. Hver Dag, HERRE, raaber jeg til dig og rækker mine Hænder imod dig.
maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
10 Gør du Undere for de døde, staar Skyggerne op og takker dig? (Sela)
Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
11 Tales der om din Naade i Graven, i Afgrunden om din Trofasthed?
Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
12 Er dit Under kendt i Mørket, din Retfærd i Glemselens Land?
Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
13 Men jeg, o HERRE, jeg raaber til dig, om Morgenen kommer min Bøn dig i Møde.
Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
14 Hvorfor forstøder du, HERRE, min Sjæl og skjuler dit Aasyn for mig?
Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
15 Elendig er jeg og Døden nær, dine Rædsler har omgivet mig fra min Ungdom;
Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
16 din Vredes Luer gaar over mig, dine Rædsler har lagt mig øde,
Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
17 som Vand er de om mig Dagen lang, til Hobe slutter de Kreds om mig;
Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
18 Ven og Frænde fjerned du fra mig, holdt mine Kendinge borte.
Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.

< Salme 88 >