< Salme 72 >
1 Af Salomo. Gud, giv Kongen din ret, Kongesønnen din retfærd,
Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 saa han dømmer dit Folk med Retfærdighed og dine arme med Ret!
Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
3 Da bærer Bjerge og Høje Fred for Folket i Retfærd.
Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 De arme blandt Folket skaffer han Ret, han bringer de fattige Frelse, og han slaar Voldsmanden ned.
Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
5 Han skal leve, saa længe Solen lyser og Maanen skinner, fra Slægt til Slægt.
Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 Han kommer som Regn paa slagne Enge, som Regnskyl, der væder Jorden;
Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 i hans Dage blomstrer Retfærd, og dyb Fred raader, til Maanen forgaar.
Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8 Fra Hav til Hav skal han herske, fra Floden til Jordens Ender;
Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9 hans Avindsmænd bøjer Knæ for ham, og hans Fjender slikker Støvet;
Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 Konger fra Tarsis og fjerne Strande frembærer Gaver, Sabas og Sebas Konger kommer med Skat;
Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11 alle Konger skal bøje sig for ham, alle Folkene være hans Tjenere.
Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
12 Thi han skal redde den fattige, der skriger om Hjælp, den arme, der savner en Hjælper,
Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 ynkes over ringe og fattig og frelse fattiges Sjæle;
Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 han skal fri deres Sjæle fra Uret og Vold, deres Blod er dyrt i hans Øjne.
Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15 Maatte han leve og Guld fra Saba gives ham! De skal bede for ham bestandig, velsigne ham Dagen igennem.
Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 Korn skal der være i Overflod i Landet, paa Bjergenes Top; som Libanon skal dets Afgrøde bølge og Folk spire frem af Byen som Jordens Urter.
Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 Velsignet være hans Navn evindelig, hans Navn skal leve, mens Solen skinner. Ved ham skal man velsigne sig, alle Folk skal prise ham lykkelig!
Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18 Lovet være Gud HERREN, Israels Gud, som ene gør Undergerninger,
Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 og lovet være hans herlige Navn evindelig; al Jorden skal fyldes af hans Herlighed. Amen, Amen!
Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
20 Her ender Davids, Isajs Søns, Bønner.
Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.