< Salme 66 >

1 Til Sangmesteren. En Sang. En Salme. Bryd ud i Jubel for Gud, al Jorden,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 lovsyng hans Navns Ære, syng ham en herlig Lovsang,
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 sig til Gud: »Hvor forfærdelige er dine Gerninger! For din vældige Styrkes Skyld logrer Fjenderne for dig,
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 al Jorden tilbeder dig, de lovsynger dig, lovsynger dit Navn.« (Sela)
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 Kom hid og se, hvad Gud har gjort, i sit Virke en Rædsel for Menneskenes Børn.
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 Han forvandlede Hav til Land, de vandred til Fods over Strømmen; lad os fryde os højlig i ham.
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 Han hersker med Vælde for evigt, paa Folkene vogter hans Øjne, ej kan genstridige gøre sig store. (Sela)
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 I Folkeslag, lov vor Gud, lad lyde hans Lovsangs Toner,
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 han, som har holdt vor Sjæl i Live og ej lod vor Fod glide ud!
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 Thi du ransaged os, o Gud, rensede os, som man renser Sølv;
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 i Fængsel bragte du os, lagde Tynge paa vore Lænder,
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 lod Mennesker skride hen over vort Hoved, vi kom gennem Ild og Vand; men du førte os ud og bragte os Lindring!
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 Med Brændofre vil jeg gaa ind i dit Hus og indfri dig mine Løfter,
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 dem, mine Læber fremførte, min Mund udtalte i Nøden.
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 Jeg bringer dig Ofre af Fedekvæg sammen med Vædres Offerduft, jeg ofrer Okser tillige med Bukke. (Sela)
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 Kom og hør og lad mig fortælle jer alle, som frygter Gud, hvad han har gjort for min Sjæl!
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 Jeg raabte til ham med min Mund og priste ham med min Tunge.
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 Havde jeg tænkt paa ondt i mit Hjerte, da havde Herren ej hørt;
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 visselig, Gud har hørt, han lytted til min bedende Røst.
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 Lovet være Gud, som ikke har afvist min Bøn eller taget sin Miskundhed fra mig!
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

< Salme 66 >