< Salme 55 >
1 Til Sangmesteren. Med Strengespil. En Maskil af David. Lyt, o Gud, til min Bøn, skjul dig ej for min Tryglen,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
2 laan mig Øre og svar mig, jeg vaander mig i Klage,
mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
3 jeg stønner ved Fjendernes Raab og de gudløses Skrig; thi Ulykke vælter de over mig, forfølger mig grumt;
chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
4 Hjertet er angst i mit Bryst, Dødens Rædsler er faldet over mig.
Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
5 Frygt og Angst falder paa mig, Gru er over mig.
Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
6 Jeg siger: Ak, havde jeg Vinger som Duen, da fløj jeg i Ly,
Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
7 ja, langt bort vilde jeg fly og blive i Ørkenen. (Sela)
Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
8 Da søgte jeg skyndsomt Tilflugt for rivende Storm og Uvejr.
Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
9 Herre, forvir og split deres Tungemaal! Thi Vold og Ufred ser jeg i Byen;
Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10 de gaar Rundgang Dag og Nat paa dens Mure;
Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11 Ulykke, Kvide og Vanheld raader derinde, Voldsfærd og Svig viger aldrig bort fra dens Torve.
Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
12 Det var ikke en Fjende, som haaned mig — det kunde bæres; min Uven ydmyged mig ej — ham kunde jeg undgaa;
Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
13 men du, en Mand af min Stand, en Ven og fortrolig,
Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14 og det skønt vi delte Samværets Sødme, vandred endrægtelig i Guds Hus.
Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
15 Over dem komme Død, lad dem levende synke i Dødsriget! Thi der er Ondskab i deres Bolig, i deres Indre! (Sheol )
Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol )
16 Jeg, jeg raaber til Gud, og HERREN vil frelse mig.
Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
17 Jeg klager og stønner ved Kvæld, ved Gry og ved Middag; min Røst vil han høre
Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
18 og udfri min Sjæl i Fred, saa de ikke kan komme mig nær; thi mange er de imod mig.
Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
19 Gud, som troner fra Fortids Dage, vil høre og ydmyge dem. (Sela) Thi der er ingen Forandring hos dem, og de frygter ikke for Gud.
Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
20 Paa Venner lagde han Haand og brød sin Pagt.
Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
21 Glattere end Smør er hans Mund, men Hjertet vil Krig, blødere end Olie hans Ord, skønt dragne Sværd.
Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
22 Kast din Byrde paa HERREN, saa sørger han for dig, den retfærdige lader han ikke i Evighed rokkes.
Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
23 Og du, o Gud, nedstyrt dem i Gravens Dyb! Ej skal blodstænkte, svigefulde Mænd naa Hælvten af deres Dage. Men jeg, jeg stoler paa dig!
Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.