< Salme 28 >
1 Af David. Jeg raaber til dig, o HERRE, min Klippe, vær ikke tavs imod mig, at jeg ej, naar du tier, skal blive som de, der synker i Graven.
Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
2 Hør min tryglende Røst, naar jeg raaber til dig, løfter Hænderne op mod dit hellige Tempel.
Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
3 Riv mig ej bort med gudløse, Udaadsmænd, som har ondt i Sinde mod Næsten trods venlige Ord.
Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
4 Løn dem for deres Idræt og onde Gerninger; løn dem for deres Hænders Værk, gengæld dem efter Fortjeneste!
Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
5 Thi HERRENS Gerning ænser de ikke, ej heller hans Hænders Værk. Han nedbryde dem og opbygge dem ej!
Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
6 Lovet være HERREN, thi han har hørt min tryglende Røst;
Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
7 min Styrke, mit Skjold er HERREN, mit Hjerte stoler paa ham. Jeg fik Hjælp, mit Hjerte jubler, jeg takker ham med min Sang.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
8 HERREN er Værn for sit Folk, sin Salvedes Tilflugt og Frelse.
Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
9 Frels dit Folk og velsign din Arv, røgt dem og bær dem til evig Tid!
Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.