< Salme 19 >
1 Til Sangmesteren. En Salme af David.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
2 Himlen forkynder Guds Ære, Hvælvingen kundgør hans Hænders værk.
Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
3 Dag bærer Bud til Dag, Nat lader Nat det vide.
Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
4 Uden Ord og uden Tale, uden at Lyden høres,
Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
5 naar Himlens Røst over Jorden vide, dens Tale til Jorderigs Ende. Paa Himlen rejste han Solen et Telt;
Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
6 som en Brudgom gaar den ud af sit Kammer, er glad som en Helt ved at løbe sin Bane,
Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
7 rinder op ved Himlens ene Rand, og dens Omløb naar til den anden. Intet er skjult for dens Glød.
Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
8 HERRENS Lov er fuldkommen, kvæger Sjælen, HERRENS Vidnesbyrd holder, gør enfoldig viis,
Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
9 HERRENS Forskrifter er rette, glæder Hjertet, HERRENS Bud er purt, giver Øjet Glans,
Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
10 HERRENS Frygt er ren, varer evigt, HERRENS Lovbud er Sandhed, rette til Hobe,
ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
11 kostelige fremfor Guld, ja fint Guld i Mængde, søde fremfor Honning og Kubens Saft.
Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
12 Din Tjener tager og Vare paa dem; at holde dem lønner sig rigt.
Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
13 Hvo mærker selv, at han fejler? Tilgiv mig lønlige Brøst!
Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
14 Værn ogsaa din Tjener mod frække, ej raade de over mig! Saa bliver jeg uden Lyde og fri for svare Synder. Lad min Munds Ord være dig til Behag, lad mit Hjertes Tanker naa frem for dit Aasyn, HERRE, min Klippe og min Genløser!
Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.