< Salme 143 >
1 En Salme af David. HERRE, hør min Bøn og lyt til min Tryglen, bønhør mig i din Trofasthed, i din Retfærd,
Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
2 gaa ikke i Rette med din Tjener, thi for dig er ingen, som lever, retfærdig!
Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
3 Thi Fjender forfølger min Sjæl, de træder mit Liv i Støvet, lader mig bo i Mørke som de, der for længst er døde.
Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
4 Aanden hensygner i mig, mit Hjerte stivner i Brystet.
Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
5 Jeg kommer fordums Dage i Hu, tænker paa alle dine Gerninger, grunder paa dine Hænders Værk.
Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
6 Jeg udbreder Hænderne mod dig, som et tørstigt Land saa længes min Sjæl efter dig. (Sela)
Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
7 Skynd dig at svare mig, HERRE, min Aand svinder hen; skjul ikke dit Aasyn for mig, saa jeg bliver som de, der synker i Graven.
Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
8 Lad mig aarle høre din Miskundhed, thi jeg stoler paa dig. Lær mig den Vej, jeg skal gaa, thi jeg løfter min Sjæl til dig.
Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
9 Fri mig fra mine Fjender, HERRE, til dig flyr jeg hen;
Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
10 lær mig at gøre din Vilje, thi du er min Gud, mig føre din gode Aand ad den jævne Vej!
Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
11 For dit Navns Skyld, HERRE, holde du mig i Live, udfri i din Retfærd min Sjæl af Trængsel,
Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
12 udslet i din Miskundhed mine Fjender, tilintetgør alle, som trænger min Sjæl! Thi jeg er din Tjener.
Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.