< Salme 135 >
1 Halleluja! Pris HERRENS Navn, pris det, I HERRENS Tjenere,
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 som staar i HERRENS Hus, i vor Guds Huses Forgaarde!
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Pris HERREN, thi god er HERREN, lovsyng hans Navn, thi lifligt er det.
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 Thi HERREN udvalgte Jakob, Israel til sin Ejendom.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 Ja, jeg ved, at HERREN er stor, vor Herre er større end alle Guder.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 HERREN gør alt, hvad han vil, i Himlene og paa Jorden, i Have og alle Verdensdyb.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 Han lader Skyer stige op fra Jordens Ende, faar Lynene til at give Regn, sender Stormen ud fra sine Forraadskamre;
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 han, som slog Ægyptens førstefødte, baade Mennesker og Kvæg,
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 og sendte Tegn og Undere i din Midte, Ægypten, mod Farao og alle hans Folk;
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 han, som fældede store Folk og vog saa mægtige Konger,
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Amoriternes Konge Sihon og Basans Konge Og og alle Kana'ans Riger
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 og gav deres Land i Eje, i Eje til Israel, hans Folk.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 HERRE, dit Navn er evigt, din Ihukommelse, HERRE, fra Slægt til Slægt,
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 thi Ret skaffer HERREN sit Folk og ynkes over sine Tjenere.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 Folkenes Billeder er Sølv og Guld, Værk af Menneskehænder;
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 de har Mund, men taler ikke, Øjne, men ser dog ej;
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 de har Ører, men hører ikke, ej heller er der Aande i deres Mund.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Som dem skal de, der laved dem, blive enhver, som stoler paa dem.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Lov HERREN, Israels Hus, lov HERREN, Arons Hus,
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 lov HERREN, Levis Hus, lov HERREN, I, som frygter HERREN!
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Fra Zion være HERREN lovet, han, som bor i Jerusalem!
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.