< Salme 120 >
1 Sang til Festrejserne. Jeg raabte til HERREN i Nød, og han svarede mig.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
2 HERRE, udfri min Sjæl fra Løgnelæber, fra den falske Tunge!
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
3 Der ramme dig dette og hint, du falske Tunge!
Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
4 Den stærkes Pile er hvæsset ved glødende Gyvel.
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
5 Ve mig, at jeg maa leve som fremmed i Mesjek, bo iblandt Kedars Telte!
Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
6 Min Sjæl har længe nok boet blandt Folk, som hader Fred.
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
7 Jeg vil Fred; men taler jeg, vil de Krig!
Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.