< Salme 116 >
1 Halleluja! Jeg elsker HERREN, thi han hører min Røst, min tryglende Bøn,
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 ja, han bøjed sit Øre til mig, jeg paakaldte HERRENS Navn.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Dødens Baand omspændte mig, Dødsrigets Angster greb mig, i Trængsel og Nød var jeg stedt. (Sheol )
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
4 Jeg paakaldte HERRENS Navn: »Ak, HERRE, frels min Sjæl!«
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Naadig er HERREN og retfærdig, barmhjertig, det er vor Gud;
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 HERREN vogter enfoldige, jeg var ringe, dog frelste han mig.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Vend tilbage, min Sjæl, til din Ro, thi HERREN har gjort vel imod dig!
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Ja, han fried min Sjæl fra Døden, mit Øje fra Graad, min Fod fra Fald.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 Jeg vandrer for HERRENS Aasyn udi de levendes Land;
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 jeg troede, derfor talte jeg, saare elendig var jeg,
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 sagde saa i min Angst: »Alle Mennesker lyver!«
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 Hvorledes skal jeg gengælde HERREN alle hans Velgerninger mod mig?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Jeg vil løfte Frelsens Bæger og paakalde HERRENS Navn.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Jeg vil indfri HERREN mine Løfter i Paasyn af alt hans Folk.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Kostbar i HERRENS Øjne er hans frommes Død.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Ak, HERRE, jeg er jo din Tjener, din Tjener, din Tjenerindes Søn, mine Lænker har du løst.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 Jeg vil ofre dig Lovprisningsoffer og paakalde HERRENS Navn;
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 mine Løfter vil jeg indfri HERREN i Paasyn af alt hans Folk
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 i HERRENS Hus's Forgaarde og i din Midte, Jerusalem!
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.