< Salme 112 >
1 Halleluja! Salig er den, der frygter HERREN og ret har Lyst til hans Bud!
Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2 Hans Æt bliver mægtig paa Jord, den Oprigtiges Slægt velsignes;
Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3 Velstand og Rigdom er i hans Hus, hans Retfærdighed varer evindelig.
Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 For den oprigtige oprinder Lys i Mørke; han er mild, barmhjertig, retfærdig.
Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5 Salig den, der ynkes og laaner ud og styrer sine Sager med Ret;
Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6 thi han rokkes aldrig i Evighed, den retfærdige ihukommes for evigt;
Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7 han frygter ikke for onde Tidender, hans Hjerte er trøstigt i Tillid til HERREN;
Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8 fast er hans Hjerte og uden Frygt, indtil han skuer sine Fjender med Fryd;
Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9 til fattige deler han rundhaandet ud, hans Retfærdighed varer evindelig; med Ære løfter hans Horn sig.
Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10 Den gudløse ser det og græmmer sig, skærer Tænder og gaar til Grunde; de gudløses Attraa bliver til intet.
Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.