< Ordsprogene 9 >
1 Visdommen bygged sig Hus, rejste sig støtter syv,
Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
2 slagted sit Kvæg og blanded sin Vin, hun har ogsaa dækket sit Bord;
Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
3 hun har sendt sine Terner ud, byder ind paa Byens højeste Steder:
Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
4 Hvo som er tankeløs, han komme hid, jeg taler til dem, som er uden Vid:
“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
5 Kom og smag mit Brød og drik den Vin, jeg har blandet!
“Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
6 Lad Tankeløshed fare, saa skal I leve, skrid frem ad Forstandens Vej! —
Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
7 Tugter man en Spotter, henter man sig Haan; revser man en gudløs, høster man Skam;
Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
8 revs ikke en Spotter, at han ikke skal hade dig, revs den vise, saa elsker han dig;
Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
9 giv til den vise, saa bliver han visere, lær den retfærdige, saa øges hans Viden.
Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
10 HERRENS Frygt er Visdoms Grundlag, at kende den HELLIGE, det er Forstand. —
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
11 Thi mange bliver ved mig dine Dage, dine Livsaars Tal skal øges.
Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
12 Er du viis, er det til Gavn for dig selv; spotter du, bærer du ene Følgen!
Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
13 Daarskaben, hun slaar sig løs og lokker og kender ikke til Skam;
Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
14 hun sidder ved sit Huses Indgang, troner paa Byens Høje
Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
15 og byder dem ind, der kommer forbi, vandrende ad deres slagne Vej:
kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
16 Hvo som er tankeløs, han komme hid, jeg taler til dem, som er uden Vid:
Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
17 Stjaalen Drik er sød, lønligt Brød er lækkert!
“Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
18 Han ved ej, at Skyggerne dvæler der, hendes Gæster er i Dødsrigets Dyb. (Sheol )
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol )