< Ordsprogene 5 >
1 Mærk dig, min Søn, min Visdom, bøj til min Indsigt dit Øre,
Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
2 at Kløgt maa vaage øver dig, Læbernes Kundskab vare paa dig.
kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
3 Thi af Honning drypper den fremmedes Læber, glattere end Olie er hendes Gane;
Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
4 men til sidst er hun besk som Malurt, hvas som tveægget Sværd;
koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
5 hendes Fødder styrer nedad mod Døden, til Dødsriget stunder hendes Fjed; (Sheol )
Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol )
6 hun følger ej Livets Vej, hendes Spor er bugtet, hun ved det ikke.
Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
7 Hør mig da nu, min Søn, vig ikke fra min Munds Ord!
Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
8 Lad din Vej være langt fra hende, kom ej hendes Husdør nær,
Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
9 at du ikke maa give andre din Ære, en grusom Mand dine Aar.
kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
10 at ikke dit Gods skal mætte fremmede, din Vinding ende i Andenmands Hus,
kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
11 saa du gribes af Anger til sidst, naar dit Kød og Huld svinder hen,
Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
12 og du siger: »Ak, at jeg hadede Tugt, at mit Hjerte lod haant om Revselse,
Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
13 saa jeg ikke lød mine Læreres Røst, ej bøjed mit Øre til dem, som lærte mig!
Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
14 Nær var jeg kommet i alskens Ulykke midt i Forsamling og Menighed!«
Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
15 Drik Vand af din egen Cisterne og rindende Vand af din Brønd;
Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
16 lad ej dine Kilder flyde paa Gaden, ej dine Bække paa Torvene!
Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
17 Dig skal de tilhøre, dig alene, ingen fremmed ved Siden af dig!
Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
18 Velsignet være dit Væld, og glæd dig ved din Ungdoms Hustru,
Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
19 den elskelige Hind, den yndige Gazel; hendes Elskov fryde dig stedse, berus dig altid i hendes Kærlighed!
Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
20 Hvi beruser du dig, min Søn, i en fremmed og tager en andens Hustru i Favn?
Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
21 Thi for HERRENS Øjne er Menneskets Veje, grant følger han alle dets Spor;
Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
22 den gudløse fanges af egen Brøde og holdes fast i Syndens Reb;
Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
23 han dør af Mangel paa Tugt, gaar til ved sin store Daarskab.
Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.