< Ordsprogene 19 >

1 Bedre Fattigmand med lydefri Færd end en, som gaar Krogveje, er han end rig.
Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
2 At mangle Kundskab er ikke godt, men den træder fejl, som har Hastværk.
Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
3 Et Menneskes Daarskab øder hans Vej, men paa HERREN vredes hans Hjerte.
Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
4 Gods skaffer mange Venner, den ringe skiller hans Ven sig fra.
Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
5 Det falske Vidne undgaar ej Straf; den slipper ikke, som farer med Løgn.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
6 Mange bejler til Stormands Yndest, og alle er Venner med gavmild Mand.
Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
7 Fattigmands Frænder hader ham alle, end mere skyr hans Venner ham da. Ej frelses den, som jager efter Ord.
Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
8 Den, der vinder Vid, han elsker sin Sjæl, og den, der vogter paa Indsigt, faar Lykke.
Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
9 Det falske Vidne undgaar ej Straf, og den, der farer med Løgn, gaar under.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
10 Vellevned sømmer sig ikke for Taabe, end mindre for Træl at herske over Fyrster.
Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
11 Klogskab gør Mennesket sindigt, hans Ære er at overse Brøde.
Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
12 Som Brøl af en Løve er Kongens Vrede, som Dug paa Græs er hans Gunst.
Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
13 Taabelig Søn er sin Faders Ulykke, Kvindekiv er som ustandseligt Tagdryp.
Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
14 Hus og Gods er Arv efter Fædre, en forstandig Hustru er fra HERREN.
Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
15 Dovenskab sænker i Dvale, den lade Sjæl maa sulte.
Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
16 Den vogter sin Sjæl, som vogter paa Budet, men skødesløs Vandel fører til Død.
Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
17 Er man god mod den ringe, laaner man HERREN, han gengælder en, hvad godt man har gjort.
Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
18 Tugt din Søn, imens der er Haab, ellers stiler du efter at slaa ham ihjel.
Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
19 Den, som er hidsig, maa bøde, ved Skaansel gør man det værre.
Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
20 Hør paa Raad og tag ved Lære, saa du til sidst bliver viis.
Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
21 I Mands Hjerte er mange Tanker, men HERRENS Raad er det, der staar fast.
Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
22 Vinding har man af Godhed, hellere fattig end Løgner.
Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
23 HERRENS Frygt er Vej til Liv, man hviler mæt og frygter ej ondt.
Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
24 Den lade rækker til Fadet, men fører ej Haanden til Munden.
Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
25 Faar Spottere Hug, bliver tankeløs klog, ved Revselse faar den forstandige Kundskab.
Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
26 Mishandle Fader og bortjage Moder gør kun en daarlig, vanartet Søn.
Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
27 Hør op, min Søn, med at høre paa Tugt og saa fare vild fra Kundskabsord.
Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
28 Niddingevidne spotter Retten, gudløses Mund er glubsk efter Uret.
Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
29 Slag er rede til Spottere, Hug til Taabers Ryg.
Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.

< Ordsprogene 19 >