< 4 Mosebog 21 >
1 Men da Kana'anæeren, Kongen af Arad, der boede i Sydlandet, hørte, at Israel rykkede frem ad Atarimvejen, angreb han Israel og tog nogle af dem til Fange.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi, imene inkakhala ku Negevi, itamva kuti Aisraeli akubwera kudzera msewu wopita ku Atarimu, inachita nkhondo ndi Aisraeli nigwira ena mwa iwo.
2 Da aflagde Israel et Løfte til HERREN og sagde: »Hvis du giver dette Folk i min Haand, vil jeg lægge Band paa deres Byer!«
Ndipo Israeli anachita lonjezo ili kwa Yehova: “Mukapereka anthu awa mʼdzanja lathu ife tidzawonongeratu mizinda yawo.”
3 Og HERREN hørte Israels Røst og gav Kana'anæerne i deres Haand, hvorefter de lagde Band paa dem og deres Byer. Derfor gav man Stedet Navnet Horma.
Yehova anamva pempho la Aisraeli ndipo anapereka Akanaaniwo kwa iwo. Anawawononga pamodzi ndi mizinda yawo. Kotero malowo anatchedwa Horima.
4 Saa brød de op fra Bjerget Hor i Retning af det røde Hav for at komme uden om Edoms Land. Undervejs blev Folket utaalmodigt
Aisraeli anayenda kuchokera ku phiri la Hori kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira kuzungulira dziko la Edomu. Koma anthu anataya mtima mʼnjiramo
5 og talte mod Gud og Moses og sagde: »Hvorfor førte I os ud af Ægypten, naar vi skal dø i Ørkenen? Her er jo hverken Brød eller Vand, og vi er lede ved denne usle Føde.«
ndipo anayankhula motsutsana ndi Mulungu ndi Mose, nati, “Chifukwa chiyani munatitulutsa kuchoka mʼdziko la Igupto kuti tidzafere mʼchipululu muno? Kuno kulibe chakudya, kulibe madzi ndipo chakudya cha chabechabechi tatopa nacho.”
6 Da sendte HERREN Giftslanger blandt Folket, og de bed Folket saa en Mængde af Israel døde.
Choncho Yehova anatumiza njoka zaululu pakati pawo. Zinaluma anthu ndipo Aisraeli ambiri anafa.
7 Saa kom Folket til Moses og sagde: »Vi har syndet ved at tale imod HERREN og dig; gaa i Forbøn hos HERREN, at han tager Slangerne fra os!« Og Moses gik i Forbøn for Folket.
Anthuwo anabwera kwa Mose ndi kunena kuti, “Tachimwa chifukwa tayankhula motsutsana ndi Yehova komanso inu. Pempherani kwa Yehova kuti atichotsere njokazi.” Tsono Mose anapempherera anthuwo.
8 Da sagde HERREN til Moses: »Lav dig en Slange og sæt den paa en Stang, saa skal enhver slangebidt, der ser hen paa den, leve!«
Yehova anati kwa Mose, “Upange njoka yaululu ndipo uyipachike pa mtengo. Aliyense amene walumidwa akangoyangʼana njokayo adzakhala ndi moyo.”
9 Da lavede Moses en Kobberslange og satte den paa en Stang; og enhver, der saa hen paa Kobberslangen, naar en Slange havde bidt ham, beholdt Livet.
Pamenepo Mose anapanga njoka yamkuwa ndi kuyipachika pa mtengo. Ndipo aliyense wolumidwa akayangʼana njoka yamkuwayo ankakhala ndi moyo.
10 Saa brød Israeliterne op og slog Lejr i Obot;
Aisraeli anayendabe nakamanga misasa yawo ku Oboti.
11 og de brød op fra Obot og slog Lejr i Ijje-Ha'abarim i Ørkenen østen for Moab.
Kenaka anasamuka ku Oboti nakamanga misasa yawo ku Iye-Abarimu, mʼchipululu chimene chili kummawa kwa Mowabu, kotulukira dzuwa.
12 Derfra brød de op og slog Lejr i Zereddalen.
Kuchoka kumeneko anayendabe nakamanga misasa yawo mʼchigwa cha Zeredi.
13 Derfra brød de op og slog Lejr i Ørkenen hinsides Arnon, som udspringer paa Amoriternes Omraade, thi Arnon var Moabs Grænse mod Amoriterne.
Anasamukanso kumeneko nakamanga moyandikana ndi Arinoni mʼdera limene lili mʼchipululu chimene chimafika mʼdziko la Aamori. Arinoni ndiwo malire a Mowabu ndi Aamori.
14 Derfor hedder det i Bogen om HERRENS Krige: .... Vaheb i Sufa og Dalene, Arnon og Dalenes Skrænt,
Nʼchifukwa chake Buku la Nkhondo za Yehova limati, “Mzinda wa Wahebu uli mu Sufa, mu zigwa za Arinoni,
15 som strækker sig til Ars Sæde og læner sig til Moabs Grænse.
ku matsitso a zigwa amene afika mpaka ku Ari nakhudza malire a dziko la Mowabu.”
16 Derfra brød de op til Be'er; det er det Be'er, HERREN havde for Øje, da han sagde til Moses: »Kald Folket sammen, saa vil jeg give dem Vand!«
Kuchokera kumeneko anapitirira mpaka ku Beeri, pa chitsime chomwe Yehova anawuza Mose kuti, “Sonkhanitsa anthu pamodzi ndipo ndidzawapatsa madzi.”
17 Da sang Israeliterne denne Sang: Brønd, væld frem! Syng til dens Pris!
Pamenepo Aisraeli anayimba nyimbo iyi: “Tulutsa madzi, chitsime iwe! Chiyimbireni nyimbo,
18 Brønd, som Høvdinger grov, som Folkets ædle bored med Herskerspir og Stave! Fra Ørkenen brød de op til Mattana;
chitsime chomwe anakumba mafumu, chomwe anakumba anthu omveka, ndi ndodo zawo zaufumu ndi ndodo zawo zoyendera.” Kenaka anachoka ku chipululu ndi kupita ku Matana.
19 fra Mattana til Nahaliel; fra Nahaliel til Bamot;
Kuchoka ku Matana anapita ku Nahalieli, kuchoka ku Nahalieli anapita ku Bamoti,
20 fra Bamot til Dalen paa Moabs Højslette, til Pisgas Top, som rager op over Ørkenen.
ndipo atachoka ku Bamoti anapita ku chigwa cha dziko la Mowabu kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, moyangʼanana ndi Yesimoni.
21 Israel sendte nu Sendebud til Amoriterkongen Sihon og lod sige:
Aisraeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, kuti,
22 »Lad mig faa Lov at drage igennem dit Land! Vi vil ikke dreje ind paa Marker eller i Vinhaver, vi vil ikke drikke Vand af Brøndene, vi vil følge Kongevejen, indtil vi er naaet igennem dit Land!«
“Tiloleni kuti tidutse mʼdziko mwanu. Sitidzapatukira mʼminda mwanu kapena mu mpesa wanu kapena kumwa madzi mʼchitsime chili chonse. Tidzayenda mu msewu waukulu wa mfumu mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
23 Men Sihon tillod ikke Israel at drage igennem sit Land; derimod samlede han alt sit Krigsfolk og rykkede ud i Ørkenen imod Israel, og da han naaede Jaza, angreb han Israel.
Koma Sihoni sanalole kuti Aisraeli adutse mʼdziko mwake. Iye anasonkhanitsa pamodzi ankhondo ake onse kuti akamenyane ndi Aisraeli mʼchipululu. Atafika pa Yahazi anamenyana ndi Aisraeli.
24 Men Israel slog ham med Sværdet og underlagde sig hans Land fra Arnon til Jabbok, til Ammoniternes Land; thi Ja'zer ligger ved Ammoniternes Grænse;
Koma Aisraeli anamupha ndi kulanda dziko lake kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki, kulekezera mʼmalire a dziko la Aamoni, chifukwa malire a dziko la Aamoni anali otetezedwa.
25 og Israel indtog alle disse Byer, og Israel bosatte sig i alle Amoriternes Byer, i Hesjbon og alle tilhørende Smaabyer.
Ndipo Aisraeli analanda mizinda yonse ya Aamori, nakhalamo kuphatikizapo Hesiboni ndi midzi yake yozungulira.
26 Thi Hesjbon var Amoriterkongen Sihons By; han havde angrebet Moabs forrige Konge og frataget ham hele hans Land indtil Arnon.
Hesiboni unali mzinda wa Sihoni mfumu ya Aamori, yemwe anamenyana ndi mfumu yakale ya dziko la Mowabu. Lonselo linakhala dziko lake mpaka ku Arinoni.
27 Derfor synger Skjaldene: Kom hid til Hesjbon, lad den blive bygget og grundfæstet, Sihons By!
Nʼchifukwa chake alakatuli amati: “Bwerani ku Hesiboni, mzindawo umangidwenso; mzinda wa Sihoni ukhazikike.
28 Thi Ild for ud fra Hesjbon, Ildslue fra Sihons Stad, den fortærede Moabs Byer, opaad Arnons Højder.
“Moto unabuka ku Hesiboni, malawi a moto kuchokera mu mzinda wa Sihoni. Unanyeketsa Ari mzinda wa ku Mowabu, nzika za ku malo okwera a Arinoni.
29 Ve dig, Moab! Det er ude med dig, Kemosj's Folk! Han gjorde sine Sønner til Flygtninge og sine Døtre til Krigsfanger for Sihon, Amoriternes Konge.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Mwawonongedwa inu anthu a ku Kemosi! Ana ake aamuna wawasandutsa ngati anthu othawathawa ndipo ana ake aakazi ngati akapolo, akapolo a Sihoni, mfumu ya Aamori.
30 Og vi skød dem ned, Hesjbon er tabt indtil Dibon; vi lagde dem øde til Nofa, som ligger ved Medeba.
“Koma ife tawagonjetsa; Hesiboni wawonongedwa mʼnjira monse mpaka kufika ku Diboni. Tawaphwasula mpaka ku mzinda wa Nofa, mzinda womwe umafika ku Medeba.
31 Saa bosatte Israel sig i Amoriternes Land.
“Choncho Aisraeli anakhala mʼdziko la Aamori.”
32 Derpaa sendte Moses Spejdere til Ja'zer; og de erobrede det tillige med tilhørende Smaabyer, og han drev de der boende Amoriter bort.
Mose atatumiza azondi ku Yazeri, Aisraeliwo analanda midzi yozungulira ndi kuthamangitsa Aamori omwe ankakhala kumeneko.
33 Derpaa vendte de om og drog ad Basan til. Da rykkede Og, Kongen af Basan, ud imod dem med alle sine Krigere og angreb dem ved Edre'i.
Kenaka anabwerera, nadzera njira ya ku Basani. Choncho Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anatuluka kukakumana nawo ndipo anamenyana nawo ku Ederi.
34 Men HERREN sagde til Moses: »Frygt ikke for ham! Thi jeg giver ham og alle hans Krigere og hans Land i din Haand, saa at du kan handle med ham, som du handlede med Amoriterkongen Sihon, der boede i Hesjbon.«
Yehova anati kwa Mose, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”
35 Da slog de ham og hans Sønner og alle hans Krigere, saa at ikke en eneste af dem undslap, og derpaa underlagde de sig hans Land.
Choncho Aisraeli anapha Ogi pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse la nkhondo. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala wamoyo, ndipo analanda dziko lakelo.