< 4 Mosebog 15 >
1 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Tal til Israeliterne og sig til dem: Naar I kommer til det Land, jeg vil give eder at bo i,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo,
3 og I vil ofre HERREN et Ildoffer, Brændoffer eller Slagtoffer, af Hornkvæg eller Smaakvæg for at indfri et Løfte eller af fri Drift eller i Anledning af eders Højtider for at berede HERREN en liflig Duft,
ndipo mukamadzapereka kwa Yehova, nsembe yotentha pa moto ya ngʼombe kapena nkhosa monga fungo lokoma kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena nsembe zina, nsembe yapadera chifukwa cha lumbiro kapena nsembe yoperekedwa mwaufulu kapenanso yoperekedwa pa chikondwerero,
4 saa skal den, der bringer HERREN sin Offergave, som Afgrødeoffer bringe en Tiendedel Efa fint Hvedemel, rørt i en Fjerdedel Hin Olie;
munthu amene akubweretsa zopereka zake, azikapereka kwa Yehova chopereka chachakudya cholemera kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta wokwana lita imodzi.
5 desuden skal du som Drikoffer til hvert Lam ofre en Fjerdedel Hin Vin, hvad enten det er Brændoffer eller Slagtoffer.
Pamodzi ndi mwana wankhosa aliyense wa nsembe yopsereza kapena nsembe ina, muzikakonzanso lita imodzi la vinyo ngati chopereka cha chakumwa.’”
6 Men til en Væder skal du som Afgrødeoffer ofre to Tiendedele Efa fint Hvedemel, rørt i en Tredjedel Hin Olie;
“Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, muzikakonzanso chopereka cha chakudya cholemera makilogalamu awiri a ufa wosalala, wosakaniza ndi mafuta okwanira lita imodzi ndi theka,
7 desuden skal du som Drikoffer frembære en Tredjedel Hin Vin til en liflig Duft for HERREN.
ndi vinyo wokwanira lita imodzi ndi theka ngati chopereka cha chakumwa. Muzikapereka monga nsembe yopereka fungo lokoma kwa Yehova.
8 Og naar du ofrer en ung Tyr som Brændoffer eller Slagtoffer for at indfri et Løfte eller som Takoffer til HERREN,
“‘Pamene mukukonza mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse: ya lumbiro lapadera kapena nsembe yachiyanjano kwa Yehova,
9 skal du foruden Tyren frembære som Afgrødeoffer tre Tiendedele Efa fint Hvedemel, rørt i en halv Hin Olie;
pamodzi ndi mwana wangʼombe wamwamunayo muzibweretsa nsembe yachakudya yolemera makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta okwana malita awiri.
10 desuden skal du som Drikoffer frembære en halv Hin Vin, et Ildoffer til en liflig Duft for HERREN.
Komanso muzibweretsa vinyo wokwanira malita awiri monga chopereka chachakumwa. Imeneyi idzakhala chopereka chotentha pa moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
11 Saaledes skal der gøres for hver enkelt Tyr, hver enkelt Væder eller hvert Lam eller Ged;
Ngʼombe yayimuna iliyonse kapena nkhosa yayimuna iliyonse, mwana wankhosa aliyense kapena mbuzi yayingʼono, zizikonzedwa motere.
12 saaledes skal I gøre for hvert enkelt Dyr, saa mange I nu ofrer.
Ngakhale zingachuluke chotani, chitani izi kwa iliyonse ya nyamazo.
13 Enhver indfødt skal gøre disse Ting paa denne Maade, naar han vil bringe et Ildoffer til en liflig Duft for HERREN.
“‘Mbadwa iliyonse ya mu Israeli izichita zimenezi pamene ibweretsa nsembe yotentha pa moto kuti ikhale fungo lokoma kwa Yehova.
14 Og naar en fremmed bor hos eder, eller nogen i de kommende Tider bor iblandt eder, og han vil bringe et Ildoffer til en liflig Duft for HERREN, skal han gøre paa samme Maade som I selv.
Ku mibado yanu yonse ya mʼtsogolo, pamene mlendo kapena wina aliyense wokhala pakati panu apereka chopereka chotentha pa moto kuti chikhale fungo lokoma kwa Yehova, azichita mofanana ndi momwe inu mumachitira.
15 Inden for Forsamlingen skal en og samme Anordning gælde for eder og den fremmede, der bor hos eder; det skal være eder en evig gyldig Anordning fra Slægt til Slægt: hvad der gælder for eder, skal ogsaa gælde for den fremmede for HERRENS Aasyn;
Gulu lonse likhale ndi malamulo ofanana a inu kapena mlendo wokhala pakati panu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya kwa mibado imene ikubwera. Inuyo ndi mlendo mudzakhala wofanana pamaso pa Yehova.
16 samme Lov og Ret gælder for eder og den fremmede, der bor hos eder.
Mudzakhale ndi malamulo ndi miyambo yofanana, inuyo ndi mlendo wokhala pakati panu.’”
17 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anawuza Mose kuti,
18 Tal til Israeliterne og sig til dem: Naar I kommer til det Land, jeg fører eder til,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo unene kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukutengeraniko
19 og spiser af Landets Brød, skal I yde HERREN en Offerydelse.
ndipo mukakadya chakudya cha mʼdzikolo, mukapereke gawo lina kwa Yehova monga chopereka.
20 Som Førstegrøde af eders Grovmel skal I yde en Kage som Offerydelse; paa samme Maade som Offerydelsen af Tærskepladsen skal I yde den.
Pa buledi wanu woyamba, mukapereke mmodzi monga nsembe, ngati chopereka chochokera ku malo wopunthira tirigu.
21 Af Førstegrøden af eders Grovmel skal I give HERREN en Offerydelse, Slægt efter Slægt.
Pa mibado yanu yonse muzidzapereka chopereka ichi kwa Yehova kuchokera ku zakudya zanu zoyamba za mʼnthaka.
22 Dersom I synder af Vanvare og undlader at udføre noget af alle de Bud, HERREN har kundgjort Moses,
“‘Ndipo ngati muchimwa mosadziwa posasunga ena mwa malamulo awa amene Yehova wapereka kwa Mose,
23 noget af alt det, HERREN har paalagt eder gennem Moses, fra den Dag HERREN udstedte sit Bud og frem i Tiden fra Slægt til Slægt,
lina lililonse mwa malamulo a Yehova amene wapereka kwa inu kudzera mwa Mose, kuyambira tsiku limene Yehova anawapereka mpaka mibado ya mʼtsogolo,
24 saa skal hele Menigheden, hvis det sker af Vanvare uden Menighedens Vidende, ofre en ung Tyr som Brændoffer til en liflig Duft for HERREN med det efter Lovbudene dertil hørende Afgrødeoffer og Drikoffer og desuden en Gedebuk som Syndoffer.
ndipo ngati zimenezi zachitika osati mwadala ndipo gulu lonse silinadziwe, zikatero gulu lonselo lipereke mwana wangʼombe wamwamuna monga nsembe yopsereza kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova pamodzinso ndi chopereka chachakudya ndi chopereka cha chakumwa ndi mbuzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo potsata zimene zinalamulidwa.
25 Og Præsten skal skaffe hele Israeliternes Menighed Soning, og dermed opnaar de Tilgivelse; thi det skete af Vanvare, og de bar bragt deres Offergave som et Ildoffer til HERREN og desuden deres Syndoffer for HERRENS Aasyn, for hvad de gjorde af Vanvare.
Wansembe apereke nsembe yopepesera machimo a gulu lonse la Aisraeli, ndipo adzakhululukidwa, pakuti linali tchimo lochita mosadziwa. Ndipo chifukwa cha tchimo lawolo, abweretse kwa Yehova nsembe yotentha pa moto ndi nsembe yopepesera machimo.
26 Saaledes faar baade hele Israeliternes Menighed og den fremmede, der bor hos dem, Tilgivelse; thi alt Folket har Del i den Synd, der bliver begaaet af Vanvare.
Gulu lonse la Aisraeli ndi alendo okhala pakati pawo adzakhululukidwa chifukwa anthu onsewo anachimwa mosadziwa.
27 Men hvis et enkelt Menneske synder af Vanvare, skal han bringe en aargammel Ged som Syndoffer.
“‘Koma ngati munthu mmodzi achimwa mosadziwa, ayenera kubweretsa mbuzi yayikazi ya chaka chimodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
28 Og Præsten skal skaffe den, der synder af Vanvare, Soning for HERRENS Aasyn ved at udføre Soningen for ham, og saaledes opnaar han Tilgivelse.
Wansembe apereke nsembe yopepesera machimowo pamaso pa Yehova chifukwa cha munthu yemwe anachimwa mosadziwayo. Nsembe yopepesera tchimo lakelo ikaperekedwa, munthuyo adzakhululukidwa.
29 For den indfødte hos Israeliterne og den fremmede, der bor iblandt dem, for eder alle gælder en og samme Lov; naar nogen synder af Vanvare.
Lamulo lomweli ligwiritsidwe ntchito kwa aliyense wochimwa mosadziwa, kaya ndi mbadwa ya mu Israeli kapena mlendo.
30 Men den, der handler med Forsæt, hvad enten han er indfødt eller fremmed, han haaner Gud, og det Menneske skal udryddes af sit Folk.
“‘Koma aliyense amene achimwa mwadala, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, nachitira chipongwe Yehova, ameneyo achotsedwe ndithu pakati pa anthu ake.
31 Thi han har ringeagtet HERRENS Ord og brudt hans Bud; det Menneske skal udryddes, hans Misgerning kommer over ham.
Popeza wanyoza mawu a Yehova ndi kuphwanya malamulo ake. Munthu ameneyo achotsedwe ndithu, kuchimwa kwake kudzakhala pa iyeyo.’”
32 Medens Israeliterne opholdt sig i Ørkenen, traf de en Mand, som sankede Brænde paa en Sabbat.
Aisraeli ali mʼchipululu, munthu wina anapezeka akutola nkhuni tsiku la Sabata.
33 De, der traf ham i Færd med at sanke Brænde, bragte ham til Moses, Aron og hele Menigheden,
Amene anamupeza akutola nkhunizo anabwera naye kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa gulu lonse
34 og de satte ham i Varetægt, da der ikke forelaa nogen bestemt Kendelse for, hvad der skulde gøres ved ham.
ndipo anamutsekera mʼndende chifukwa sankadziwa choti achite naye.
35 Da sagde HERREN til Moses: Den Mand skal lide Døden; hele Menigheden skal stene ham uden for Lejren!
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Munthu ameneyu ayenera kuphedwa. Gulu lonse liyenera kumugenda ndi miyala kunja kwa msasa.”
36 Hele Menigheden førte ham da uden for Lejren og stenede ham til Døde, som HERREN havde paalagt Moses.
Choncho gululo linamutengera kunja kwa msasa ndi kumupha pomugenda ndi miyala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
37 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anawuza Mose kuti,
38 Tal til Israeliterne og sig til dem, at de Slægt efter Slægt skal sætte Kvaster paa Fligene af deres Klæder, og at de paa hver enkelt Kvast skal sætte en violet Purpursnor.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pa mibado yanu yonse muzisokerera mphonje pa ngodya za zovala zanu ndipo pa ngodya ya mphonje iliyonse azisokererapo chingwe chobiriwira.
39 Det skal tjene eder til Tegn, saa at I, hver Gang I ser dem, skal komme alle HERRENS Bud i Hu og handle efter dem og ikke lade eder vildlede af eders Hjerter eller Øjne, af hvilke I lader eder forlede til Bolen —
Mudzakhala ndi mphonje zimenezi kuti mukaziona muzikakumbukira malamulo onse a Yehova ndi kuwamvera kuti musamatsatenso zilakolako za mʼmitima mwanu ndi za maso anu.
40 for at I kan komme alle mine Bud i Hu og handle efter dem og blive hellige for eders Gud.
Motero mudzakumbukira kumvera malamulo anga ndipo mudzakhala opatulikira a Mulungu wanu.
41 Jeg er HERREN eders Gud, som førte eder ud af Ægypten for at være eders Gud. Jeg er HERREN eders Gud!
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”