< 4 Mosebog 13 >

1 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 »Send nogle Mænd af Sted for at undersøge Kana'ans Land, som jeg vil give Israeliterne; een Mand af hver Fædrenestamme skal I sende, og kun Mænd, der er Øverster iblandt dem!«
“Tuma anthu kuti akazonde dziko la Kanaani limene ndikupereka kwa Aisraeli. Kuchokera pa fuko lililonse utume munthu mmodzi amene ndi mtsogoleri wawo.”
3 Da udsendte Moses dem fra Parans Ørken paa HERRENS Bud, Mænd, der alle var Overhoveder for Israeliterne.
Monga mwa mawu a Yehova, Mose anawatuma kuchokera ku chipululu cha Parani. Onsewo anali atsogoleri a Aisraeli.
4 Deres Navne var følgende: Af Rubens Stamme Sjammua, Zakkurs Søn,
Mayina awo ndi awa: kuchokera ku fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri;
5 af Simeons Stamme Sjafat, Horis Søn,
kuchokera ku fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori;
6 af Judas Stamme Kaleb, Jefunnes Søn,
kuchokera ku fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune;
7 af Issakars Stamme Jig'al, Josefs Søn,
kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;
8 af Efraims Stamme Hosea, Nuns Søn,
kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;
9 af Benjamins Stamme Palti, Rafus Søn,
kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;
10 af Zebulons Stamme Gaddiel, Sodis Søn,
kuchokera ku fuko la Zebuloni, Gadieli mwana wa Sodi;
11 af Josefs Stamme, det er Manasses Stamme, Gaddi, Susis Søn,
kuchokera ku fuko la Manase (fuko la Yosefe), Gadi mwana wa Susi;
12 af Dans Stamme Ammiel, Gemallis Søn,
kuchokera ku fuko la Dani, Amieli mwana wa Gemali;
13 af Asers Stamme Setur, Mikaels Søn,
kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;
14 af Naftalis Stamme Nabi, Vofsis Søn,
kuchokera ku fuko la Nafutali, Naabi mwana wa Vofisi;
15 af Gads Stamme Ge'uel, Makis Søn.
kuchokera ku fuko la Gadi, Geuweli mwana wa Maki.
16 Det var Navnene paa de Mænd, Moses udsendte for at undersøge Landet. Men Moses gav Hosea, Nuns Søn, Navnet Josua.
Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).
17 Og Moses sendte dem af Sted for at undersøge Kana'ans Land. Og han sagde til dem: »Drag herfra op i Sydlandet og drag op i Bjergene
Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri.
18 og se, hvordan Landet er, og om Folket, som bor der, er stærkt eller svagt, faatalligt eller talrigt,
Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri.
19 om Landet, de bor i, er godt eller daarligt, og om Byerne, de bor i, er Teltlejre eller Fæstninger,
Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga?
20 og om Landet er fedt eller magert, om der findes Træer deri eller ej. Vær ved godt Mod og tag noget af Landets Frugt med tilbage!« Det var netop ved den Tid, de første Druer var modne.
Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).
21 Saa drog de af Sted og undersøgte Landet lige fra Zins Ørken til Rehob, Egnen hen imod Hamat.
Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati.
22 Saa begav de sig op i Sydlandet og kom til Hebron; der boede Ahiman, Sjesjaj og Talmaj, Anaks Efterkommere. Men Hebron var grundlagt syv Aar før Zoan i Ægypten.
Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto).
23 Da de naaede Esjkoldalen, afskar de en Ranke med en Drueklase, som der maatte to Mand til at bære paa en Bærestang, og plukkede nogle Granatæbler og Figener.
Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu.
24 Man kaldte dette Sted Esjkoldalen med Hentydning til den Drueklase, Israeliterne der skar af.
Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko.
25 Efter fyrretyve Dages Forløb vendte de tilbage efter at have undersøgt Landet;
Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.
26 og de kom til Moses og Aron og hele Israeliternes Menighed i Parans Ørken i Kadesj og aflagde Beretning for dem og hele Menigheden og viste dem Landets Frugt.
Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo.
27 De fortalte ham: »Vi kom til Landet, du sendte os til; det er virkelig et Land, der flyder med Mælk og Honning, og her er Flugt derfra;
Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi.
28 men stærkt er Folket, som bor i Landet, og Byerne er befæstede og meget store; ja, vi saa ogsaa Efterkommere af Anak der.
Koma anthu amene amakhala mʼdzikomo ndi amphamvu, mizinda yawo ndi ya malinga aakulu kwambiri. Tinaonanso Aanaki kumeneko.
29 Amalek bor i Sydlandet, Hetiterne, Jebusiterne og Amoriterne i Bjerglandet og Kana'anæerne ved Havet og langs Jordan.«
Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”
30 Da søgte Kaleb at bringe Folket til Tavshed over for Moses og sagde: »Lad os kun drage op og underlægge os det, thi vi kan sikkert tage det!«
Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”
31 Men de Mænd, der havde været med ham deroppe, sagde: »Vi kan ikke drage op imod dette Folk, thi det er stærkere end vi!«
Koma anthu aja amene anapita naye anati, “Sitingathe kulimbana ndi anthuwo popeza ndi amphamvu kuposa ifeyo.”
32 Og de talte nedsættende til Israeliterne om Landet, som de havde undersøgt, og sagde: »Landet, som vi har rejst igennem og undersøgt, er et Land, der fortærer sine Indbyggere, og alle de Folk, vi saa der, var kæmpestore.
Choncho anthuwo anafalitsa pakati pa Aisraeli mbiri yoyipa ya dziko lomwe anakalionalo. Iwo anati, “Dziko limene tinapita kukalizonda limawononga anthu okhala mʼmenemo. Ndipo anthu onse amene tinakawaona kumeneko ndi ataliatali.
33 Vi saa der Kæmperne — Anaks Sønner, der er af Kæmpeslægten — og vi forekom baade os selv og dem som Græshopper!«
Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”

< 4 Mosebog 13 >