< Nehemias 6 >

1 Da det nu kom Sanballat, Araberen Gesjem og vore andre Fjender for Øre, at jeg havde bygget Muren, og at der ikke var flere Huller i den — dog havde jeg paa den Tid ikke sat Fløje i Portene —
Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata.
2 sendte Sanballat og Gesjem Bud og opfordrede mig til en Sammenkomst i Kefirim i Onodalen. Men de havde ondt i Sinde imod mig.
Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.” Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko.
3 Derfor sendte jeg Bud til dem og lod sige: »Jeg har et stort Arbejde for og kan derfor ikke komme derned; hvorfor skulde Arbejdet standse? Og det vilde ske, hvis jeg lod det ligge for at komme ned til eder.
Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?”
4 Fire Gange sendte de mig samme Bud, og hver Gang gav jeg dem samme Svar.
Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.
5 Da sendte Sanballat for femte Gang sin Tjener til mig med samme Bud, og han havde et aabent Brev med,
Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata.
6 i hvilket der stod: Det hedder sig blandt Folkene, og Gasjmu bekræfter det, at du og Jøderne pønser paa Oprør; derfor er det, du bygger Muren, og at du vil være deres Konge.
Mu kalatamo munali mawu akuti, “Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo.
7 Og du skal endog have faaet Profeter til i Jerusalem at udraabe dig til Konge i Juda. Dette Rygte vil nu komme Kongen for Øre; kom derfor og lad os tales ved!
Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”
8 Men jeg sendte ham det Bud: Slige Ting, som du omtaler, er slet ikke sket; det er dit eget Paafund!
Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”
9 Thi de havde alle til Hensigt at indjage os Skræk, idet de tænkte, at vi skulde lade Hænderne synke, saa Arbejdet ikke blev til noget. Men styrk du nu mine Hænder!
Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.” Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”
10 Og da jeg gik ind i Sjemajas, Mehetab'els Søn Delajas Søns, Hus, som ved den Tid maatte holde sig inde, sagde han: Lad os tales ved i Guds Hus, i Helligdommens Indre, og stænge Dørene, thi der kommer nogle Folk, som vil dræbe dig; de kommer i Nat for at dræbe dig!«
Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”
11 Men jeg svarede: Skulde en Mand som jeg flygte? Og hvorledes skulde en Mand som jeg kunne betræde Helligdommen og blive i Live? Jeg gaar ikke derind!
Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!”
12 Thi jeg skønnede, at det ikke var Gud, som havde sendt ham, men at han var kommet med det Udsagn om mig, fordi Tobija og Sanballat havde lejet ham dertil,
Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi.
13 for at jeg skulde blive bange og forsynde mig ved slig Adfærd og de faa Anledning til ilde Omtale, saa de kunde bagvaske mig.
Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.
14 Kom Tobija og Sanballat i Hu, min Gud, efter deres Gerninger, ligeledes Profetinden Noadja og de andre Profeter, der vilde gøre mig bange!
Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”
15 Saaledes blev Muren færdig den fem og tyvende Dag i Elul Maaned efter to og halvtredsindstyve Dages Forløb.
Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52.
16 Og da alle vore Fjender hørte det, blev alle Hedningerne rundt om os bange og saare nedslaaede, idet de skønnede, at dette Værk var udført med vor Guds Hjælp.
Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.
17 Men der gik ogsaa i de Dage en Mængde Breve frem og tilbage mellem Tobija og de store i Juda;
Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo,
18 thi mange i Juda stod i Edsforbund med ham, da han var Svigersøn af Sjekanja, Aras Søn, og hans Søn Johanan var gift med en Datter af Mesjullam, Berekjas Søn.
pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya.
19 Ogsaa plejede de baade at tale godt om ham til mig og at forebringe ham mine Ord; Tobija sendte ogsaa Breve for at gøre mig bange.
Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.

< Nehemias 6 >