< Matthæus 22 >

1 Og Jesus tog til Orde og talte atter i Lignelser til dem og sagde:
Yesu anayankhula nawonso mʼmafanizo, nati,
2 „Himmeriges Rige lignes ved en Konge, som gjorde Bryllup for sin Søn.
“Ufumu wakumwamba uli ngati mfumu imene inakonzera phwando mwana wake wamwamuna.
3 Og han udsendte sine Tjenere for at kalde de budne til Brylluppet; og de vilde ikke komme.
Anatumiza antchito ake kwa amene anayitanidwa kuphwando koma anakana kubwera.
4 Han udsendte atter andre Tjenere og sagde: Siger til de budne: Se, jeg har beredt mit Maaltid, mine Okser og Fedekvæget er slagtet, og alting er rede; kommer til Brylluppet!
“Kenaka anatumiza antchito ena nati, ‘Awuzeni oyitanidwa kuti phwando lakonzedwa: ndapha ngʼombe yayimuna ndi nyama zina zonenepa ndipo zonse zakonzedwa. Bwerani ku phwando laukwati.’
5 Men de brøde sig ikke derom og gik hen, den ene paa sin Mark, den anden til sit Købmandsskab;
“Koma iwo sanalabadire ndipo anachoka; wina anapita ku munda wake ndi wina ku malonda ake.
6 og de øvrige grebe hans Tjenere, forhaanede og ihjelsloge dem.
Ndipo otsalawo anagwira antchito ake, nawazunza ndi kuwapha.
7 Men Kongen blev vred og sendte sine Hære ud og slog disse Manddrabere ihjel og satte Ild paa deres Stad.
Mfumu inakwiya. Inatumiza asilikali ake ndipo anawononga opha anzawowo ndi kutentha mzinda wawo.
8 Da siger han til sine Tjenere: Brylluppet er beredt, men de budne vare det ikke værd.
“Pamenepo anati kwa antchito ake, ‘Phwando laukwati lakonzedwa, koma amene ndinawayitana sanali oyenera.
9 Gaar derfor ud paa Skillevejene og byder til Brylluppet saa mange, som I finde!
Pitani ku mphambano za misewu ndipo kayitaneni aliyense amene mukamupeze kuti abwere ku phwando.’
10 Og de Tjenere gik ud paa Vejene og samlede alle dem, de fandt, baade onde og gode; og Bryllupshuset blev fuldt af Gæster.
Pamenepo antchitowo anapita ku misewu nakasonkhanitsa anthu onse amene anakawapeza, abwino ndi oyipa omwe, ndipo nyumba ya madyerero inadzaza ndi oyitanidwa.
11 Da nu Kongen gik ind for at se Gæsterne, saa han der et Menneske, som ikke var iført Bryllupsklædning.
“Koma pamene mfumu inabwera kudzaona oyitanidwawo, inaona munthu amene sanavale zovala zaukwati.
12 Og han siger til ham: Ven! hvorledes er du kommen herind og har ingen Bryllupsklædning paa? Men han tav.
Inamufunsa kuti, ‘Bwenzi walowa bwanji muno wopanda zovala zaukwati?’ Munthuyo anakhala chete.
13 Da sagde Kongen til Tjenerne: Binder Fødder og Hænder paa ham, og kaster ham ud i Mørket udenfor; der skal der være Graad og Tænders Gnidsel.
“Pamenepo mfumuyo inawuza otumikira kuti, ‘Mʼmangeni manja ndi miyendo, ndipo muponyeni kunja, ku mdima kumene kudzakhale kulira ndi kukuta mano.’
14 Thi mange ere kaldede, men faa ere udvalgte.”
“Popeza oyitanidwa ndi ambiri koma osankhidwa ndi ochepa.”
15 Da gik Farisæerne hen og holdt Raad om, hvorledes de kunde fange ham i Ord.
Kenaka Afarisi anatuluka nakakonza njira zomupezera zifukwa Yesu mʼmawu ake.
16 Og de sende deres Disciple til ham tillige med Herodianerne og sige: „Mester! vi vide, at du er sanddru og lærer Guds Vej i Sandhed og ikke bryder dig om nogen; thi du ser ikke paa Menneskers Person.
Anatumiza ophunzira awo kwa Iye pamodzi ndi Aherodia. Anati, “Aphunzitsi, tidziwa kuti ndinu wangwiro ndi kuti mumaphunzitsa mawu a Mulungu monga mwa choonadi. Simutekeseka ndi anthu, popeza simusamala kuti kodi ndi ndani?
17 Sig os derfor: Hvad tykkes dig? Er det tilladt at give Kejseren Skat, eller ej?”
Tiwuzeni tsono maganizo anu ndi otani, kodi nʼkololedwa kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?”
18 Men da Jesus mærkede deres Ondskab, sagde han: „I Hyklere, hvorfor friste I mig?
Koma Yesu podziwa maganizo awo oyipa anati, “Inu achiphamaso, bwanji mufuna kundipezera chifukwa?
19 Viser mig Skattens Mønt!” Og de bragte ham en Denar.
Onetseni ndalama imene mumapereka msonkho.” Iwo anabweretsa dinari,
20 Og han siger til dem: „Hvis Billede og Overskrift er dette?”
ndipo anawafunsa kuti, “Kodi chithunzi ichi ndi malemba awa ndi za ndani?”
21 De sige til ham: „Kejserens.” Da siger han til dem: „Saa giver Kejseren, hvad Kejserens er, og Gud, hvad Guds er!”
Iwo anayankha kuti, “Ndi za Kaisara.” Pamenepo anawawuza kuti, “Perekani kwa Kaisara zake za Kaisara, ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.”
22 Og da de hørte det, undrede de sig, og de forlode ham og gik bort.
Atamva izi, anadabwa, ndipo anamusiya Iye, nachoka.
23 Samme Dag kom der Saddukæere til ham, hvilke sige, at der ingen Opstandelse er, og de spurgte ham og sagde:
Tsiku lomwelo Asaduki amene amati kulibe za kuukanso, anabwera kwa Iye ndi funso.
24 „Mester! Moses har sagt: Naar nogen dør og ikke har Børn, skal hans Broder for Svogerskabets Skyld tage hans Hustru til Ægte og oprejse sin Broder Afkom.
Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatiwuza kuti munthu akamwalira wosasiya ana, mʼbale wake akuyenera kukwatira mkazi wamasiyeyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
25 Men nu var der hos os syv Brødre; og den første giftede sig og døde; og efterdi han ikke havde Afkom, efterlod han sin Hustru til sin Broder.
Tsopano panali abale asanu ndi awiri pakati pathu. Woyambayo anakwatira ndipo anamwalira, ndipo popeza analibe ana, mʼbale wake analowa chokolo.
26 Ligesaa ogsaa den anden og den tredje, indtil den syvende;
Izi zinachitikiranso mʼbale wa chiwiri ndi wachitatu mpaka wachisanu ndi chiwiri.
27 men sidst af alle døde Hustruen.
Pa mapeto pake mkaziyo anamwaliranso.
28 Hvem af disse syv skal nu have hende til Hustru i Opstandelsen? thi de have alle haft hende.”
Tsopano, kodi akadzaukitsidwa adzakhala mkazi wa ndani mwa asanu ndi awiriwa popeza aliyense anamukwatirapo?”
29 Men Jesus svarede og sagde til dem: „I fare vild, idet I ikke kende Skrifterne, ej heller Guds Kraft.
Yesu anayankha kuti, “Inu mukulakwitsa chifukwa simukudziwa malemba kapena mphamvu ya Mulungu.
30 Thi i Opstandelsen tage de hverken til Ægte eller bortgiftes, men de ere ligesom Guds Engle i Himmelen.
Anthu akadzaukitsidwa, sadzakwatira kapena kukwatiwa; adzakhala ngati angelo kumwamba.
31 Men hvad de dødes Opstandelse angaar, have I da ikke læst, hvad der er talt til eder af Gud, naar han siger:
Koma za kuukitsidwa kwa akufa, kodi simunawerenge zimene Mulungu ananena kwa inu kuti,
32 „Jeg er Abrahams Gud og Isaks Gud og Jakobs Gud.” Han er ikke dødes, men levendes Gud.”
‘Ine ndine Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo?’ Iyeyo si Mulungu wa akufa koma wa amoyo.”
33 Og da Skarerne hørte dette, bleve de slagne af Forundring over hans Lære.
Magulu a anthu atamva zimenezi, anazizwa ndi chiphunzitso chake.
34 Men da Farisæerne hørte, at han havde stoppet Munden paa Saddukæerne, forsamlede de sig.
Pakumva kuti Yesu anawakhalitsa chete Asaduki, Afarisi anasonkhana pamodzi.
35 Og en af dem, en lovkyndig, spurgte og fristede ham og sagde:
Mmodzi wa iwo, katswiri wa malamulo anamuyesa Iye ndi funso ndipo anati,
36 „Mester, hvilket er det store Bud i Loven?”
“Aphunzitsi, kodi lamulo lalikulu koposa mu malamulo ndi liti?”
37 Men han sagde til ham: „Du skal elske Herren din Gud med hele dit Hjerte og med hele din Sjæl og med hele dit Sind.
Yesu anayankha kuti, “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse ndi moyo wako wonse ndi nzeru zako zonse.
38 Dette er det store og første Bud.
Ili ndi lamulo loyamba ndi loposa onse.
39 Men et andet er dette ligt: Du skal elske din Næste som dig selv.
Ndipo lachiwiri ndi lofanana nalo: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’
40 Af disse to Bud afhænger hele Loven og Profeterne.”
Malamulo onse ndi aneneri zakhazikika pa malamulo awiriwa.”
41 Men da Farisæerne vare forsamlede, spurgte Jesus dem og sagde:
Afarisi atasonkhana pamodzi, Yesu anawafunsa kuti,
42 „Hvad tykkes eder om Kristus? Hvis Søn er han?” De sige til ham: „Davids.”
“Kodi mukuganiza bwanji za Khristu? Ndi Mwana wa ndani?” Iwo anayankha kuti, “Mwana wa Davide.”
43 Han siger til dem: „Hvorledes kan da David i Aanden kalde ham Herre, idet han siger:
Iye anawawuza kuti, “Nanga zikutheka bwanji kuti Davide poyankhula mwa Mzimu Woyera amatchula Iye ‘Ambuye?’ Pakuti akuti,
44 Herren sagde til min Herre: Sæt dig ved min højre Haand, indtil jeg faar lagt dine Fjender under dine Fødder.
“Ambuye anati kwa Ambuye wanga: ‘Khala pa dzanja langa lamanja mpaka ndiyike adani ako pansi pa mapazi ako.’
45 Naar nu David kalder ham Herre, hvorledes er han da hans Søn?”
Ngati tsono Davide amamutchula ‘Ambuye,’ zingatheke bwanji kukhala mwana wake?”
46 Og ingen kunde svare ham et Ord, og ingen vovede mere at rette Spørgsmaal til ham efter den Dag.
Panalibe wina anatha kuyankha, ndipo kuchokera pamenepo, panalibe wina anayerekeza kumufunsa funso.

< Matthæus 22 >