< Matthæus 15 >

1 Da kommer der fra Jerusalem Farisæere og skriftkloge til Jesus og sige:
Pamenepo Afarisi ena ndi aphunzitsi amalamulo anabwera kwa Yesu kuchokera ku Yerusalemu ndipo anamufunsa kuti,
2 „Hvorfor overtræde dine Disciple de gamles Overlevering? thi de to ikke deres Hænder, naar de holde Maaltid.”
“Chifukwa chiyani ophunzira anu amaphwanya mwambo wa akuluakulu? Iwo sasamba mʼmanja pakudya!”
3 Men han svarede og sagde til dem: „Hvorfor overtræde ogsaa I Guds Bud for eders Overleverings Skyld?
Yesu anayankha kuti, “Nanga chifukwa chiyani inu mumaphwanya lamulo la Mulungu chifukwa cha mwambo wa makolo anu?
4 Thi Gud har paabudt og sagt: „Ær din Fader og din Moder;” og: „Den, som bander Fader eller Moder, skal visselig dø.”
Pakuti Mulungu anati, ‘Lemekeza abambo ako ndi amayi ako’ ndipo ‘aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.’
5 Men I sige: „Den, som siger til sin Fader eller sin Moder: „Det, hvormed du skulde være hjulpet af mig, skal være en Tempelgave,” han skal ingenlunde ære sin Fader eller sin Moder.”
Koma inu mumati, ngati munthu anena kwa abambo ake kapena amayi ake kuti, ‘Thandizo lililonse mukalirandira kuchokera kwa ine ndi mphatso yoperekedwa kwa Mulungu,’
6 Og I have ophævet Guds Lov for eders Overleverings Skyld.
iye sakulemekeza nayo abambo ake ndipo ndi khalidwe lotere inu mumapeputsa nalo Mawu a Mulungu chifukwa cha mwambo wanu.
7 I Hyklere! Rettelig profeterede Esajas om eder, da han sagde:
Inu anthu achiphamaso, Yesaya ananenera za inu kuti,
8 „Dette Folk ærer mig med Læberne; men deres Hjerte er langt borte fra mig.
“‘Anthu awa amandilemekeza Ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.
9 Men de dyrke mig forgæves, idet de lære Lærdomme, som ere Menneskers Bud.”
Amandilambira Ine kwachabe ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.’”
10 Og han kaldte Folkeskaren til sig og sagde til dem: „Hører og forstaar!
Yesu anayitana gulu la anthu nati, “Mverani ndipo zindikirani.
11 Ikke det, som gaar ind i Munden, gør Mennesket urent, men det, som gaar ud af Munden, dette gør Mennesket urent.”
Chimene chimalowa mʼkamwa mwa munthu sichimuchititsa kukhala woyipa, koma chimene chimatuluka mʼkamwa mwake, icho ndi chimene chimamuchititsa kukhala woyipa.”
12 Da kom hans Disciple hen og sagde til ham: „Ved du, at Farisæerne bleve forargede, da de hørte den Tale?”
Pamenepo ophunzira anabwera kwa Iye ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mukudziwa kuti Afarisi anakhumudwa pamene anamva mawu aja?”
13 Men han svarede og sagde: „Enhver Plantning, som min himmelske Fader ikke har plantet, skal oprykkes med Rode.
Iye anayankha kuti, “Mbewu iliyonse imene Atate anga akumwamba sanadzale idzazulidwa ndi mizu yomwe.
14 Lader dem fare, det er blinde Vejledere for blinde; men naar en blind leder en blind, falde de begge i Graven.”
Alekeni, ndi atsogoleri osaona. Ngati munthu wosaona atsogolera wosaona mnzake, onse awiri adzagwera mʼdzenje.”
15 Men Peter svarede og sagde til ham: „Forklar os Lignelsen!”
Petro anati, “Timasulireni fanizoli.”
16 Og han sagde: „Ere ogsaa I endnu saa uforstandige?
Yesu anawafunsa kuti, “Kani ngakhale inunso simumvetsa?
17 Forstaa I endnu ikke, at alt, hvad der gaar ind i Munden, gaar i Bugen og føres ud ad den naturlige Vej?
Kodi inu simudziwa kuti chilichonse cholowa mʼkamwa chimapita mʼmimba ndipo kenaka chimatuluka kunja kwa thupi?
18 Men det, som gaar ud af Munden, kommer ud fra Hjertet, og det gør Mennesket urent.
Koma zinthu zimene zituluka mʼkamwa zimachokera mu mtima ndipo zimenezi zimamuchititsa munthu kukhala woyipa.
19 Thi ud fra Hjertet kommer der onde Tanker, Mord, Hor, Utugt, Tyverier, falske Vidnesbyrd, Forhaanelser.
Pakuti mu mtima mumatuluka maganizo oyipa, zakupha, zachigololo, zadama, zakuba, zaumboni wonama ndi zachipongwe.
20 Det er disse Ting, som gøre Mennesket urent; men at spise med utoede Hænder gør ikke Mennesket urent.”
Izi ndi zimene zimachititsa munthu kukhala woyipa; koma kudya ndi mʼmanja mosasamba sikumuchititsa munthu kukhala woyipa.”
21 Og Jesus gik bort derfra og drog til Tyrus's og Sidons Egne.
Yesu atachoka kumalo amenewo anapita kudera la ku Turo ndi ku Sidoni.
22 Og se, en kananæisk Kvinde kom fra disse Egne, raabte og sagde: „Herre, Davids Søn! forbarm dig over mig! min Datter plages ilde af en ond Aand.”
Mayi wa Chikanaani wochokera dera la komweko anabwera kwa Iye akulira, nati, “Ambuye, Mwana wa Davide, ndichitireni chifundo! Mwana wanga wamkazi akuzunzika kwambiri ndi chiwanda.”
23 Men han svarede hende ikke et Ord. Da traadte hans Disciple til, bade ham og sagde: „Skil dig af med hende, thi hun raaber efter os.”
Yesu sanayankhe kanthu. Ndipo ophunzira ake anabwera namupempha Iye kuti, “Muwuzeni achoke chifukwa akulira mofuwula pambuyo pathu.”
24 Men han svarede og sagde: „Jeg er ikke udsendt uden til de fortabte Faar af Israels Hus.”
Iye anayankha kuti, “Ine ndinatumidwa kwa nkhosa zotayika za Israeli zokha.”
25 Men hun kom og kastede sig ned for ham og sagde: „Herre, hjælp mig!”
Mayiyo anabwera ndi kugwada pamaso pake, nati, “Ambuye ndithandizeni!”
26 Men han svarede og sagde: „Det er ikke smukt at tage Børnenes Brød og kaste det for de smaa Hunde.”
Iye anayankha kuti, “Sibwino kutenga chakudya cha ana ndi kuponyera agalu.”
27 Men hun sagde: „Jo, Herre! de smaa Hunde æde jo dog ogsaa af de Smuler, som falde fra deres Herrers Bord.”
Mayiyo anati, “Inde Ambuye. Komatu ngakhale agalu amadya nyenyeswa zimene zimagwa kuchokera pa tebulo la mbuye wawo.”
28 Da svarede Jesus og sagde til hende: „O Kvinde, din Tro er stor, dig ske, som du vil!” Og hendes Datter blev helbredet fra samme Time.
Pomwepo Yesu anayankha kuti, “Mayi iwe uli ndi chikhulupiriro chachikulu! Pempho lako lamveka.” Ndipo mwana wake wamkazi anachira nthawi yomweyo.
29 Og Jesus gik bort derfra og kom hen til Galilæas Sø, og han gik op paa Bjerget og satte sig der.
Yesu anachoka kumeneko napita mʼmbali mwa nyanja ya Galileya. Ndipo anakwera ku phiri nakhala pansi.
30 Og store Skarer kom til ham og havde lamme, blinde, stumme, Krøblinger og mange andre med sig; og de lagde dem for hans Fødder, og han helbredte dem,
Gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Iye ndi anthu olumala, osaona, ofa ziwalo, osayankhula ndi ena ambiri nawagoneka pa mapazi ake ndipo Iye anawachiritsa.
31 saa at Skaren undrede sig, da de saa, at stumme talte, Krøblinger bleve raske, lamme gik, og blinde saa; og de priste Israels Gud.
Anthu ataona osayankhula akuyankhula, ofa ziwalo akuchira, olumala miyendo akuyenda ndi osaona akuona anadabwa kwambiri. Ndipo analemekeza Mulungu wa Israeli.
32 Men Jesus kaldte sine Disciple til sig og sagde: „Jeg ynkes inderligt over Skaren; thi de have allerede tøvet hos mig tre Dage og have intet at spise; og lade dem gaa fastende bort vil jeg ikke, for at de ikke skulle vansmægte paa Vejen.”
Yesu anayitana ophunzira ake nati, “Ndili ndi chifundo ndi anthu awa; akhala kale ndi Ine masiku atatu ndipo alibe chakudya. Ine sindifuna kuti apite kwawo ndi njala chifukwa angakomoke pa njira.”
33 Og hans Disciple sige til ham: „Hvorfra skulle vi faa saa mange Brød i en Ørken, at vi kunne mætte saa mange Mennesker?”
Ophunzira anayankha kuti, “Ndikuti kumene tingakapeze buledi mʼtchire muno okwanira kudyetsa gulu lotere?”
34 Og Jesus siger til dem: „Hvor mange Brød have I?” Men de sagde: „Syv og nogle faa Smaafisk.”
Yesu anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati?” Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri ndi tinsomba pangʼono.”
35 Og han bød Skaren at sætte sig ned paa Jorden
Iye anawuza gululo kuti likhale pansi.
36 og tog de syv Brød og Fiskene, takkede, brød dem og gav Disciplene dem, og Disciplene gave dem til Skarerne.
Kenaka anatenga malofu asanu ndi awiri aja ndi tinsombato ndipo atayamika anagawa napatsa ophunzira ake ndipo iwo anagawira anthuwo.
37 Og de spiste alle og bleve mætte; og de opsamlede det, som blev tilovers af Stykkerne, syv Kurve fulde.
Onse anadya ndipo anakhuta. Pomaliza ophunzira anatolera zotsalira nadzaza madengu asanu ndi awiri.
38 Men de, som spiste, vare fire Tusinde Mænd, foruden Kvinder og Børn.
Chiwerengero cha anthu amene anadya chinali 4,000 kupatula amayi ndi ana.
39 Og da han havde ladet Skarerne gaa bort, gik han om Bord i Skibet og kom til Magadans Egne.
Yesu atatha kuwuza gululo kuti lipite kwawo, analowa mʼbwato ndipo anapita kudera la Magadala.

< Matthæus 15 >