< Malakias 4 >
1 Thi se, Dagen kommer, luende som en Ovn; og alle de frække og alle, som øver Gudløshed, skal blive som Straa, og Dagen, som kommer, skal lade dem gaa op i Luer, siger Hærskarers HERRE, saa der ikke levnes Rod eller Gren af dem.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndithu tsiku likubwera; lidzayaka ngati ngʼanjo. Anthu onse odzikuza, ndi aliyense ochita zoyipa adzapsa ngati chiputu, ndipo pa tsiku limene likubweralo adzapserera ndi moto. Sipadzatsalira muzu kapena nthambi.
2 Men for eder, som frygter mit Navn, skal Retfærds Sol opgaa med Lægedom under sine Vinger, og I skal gaa ud og boltre eder som Kalve, der kommer fra Stalden,
Koma inu amene mumaopa dzina langa, dzuwa lachilungamo lidzakutulukirani lili ndi kuwala kokuchiritsani. Ndipo inu mudzatuluka ndi kulumphalumpha ngati ana angʼombe amene atulutsidwa mʼkhola.
3 og trampe de gudløse ned; thi de skal blive til Støv under eders Fodsaaler, den Dag jeg griber ind, siger Hærskarers HERRE.
Tsiku limenelo inu mudzapondereza anthu oyipa; adzakhala phulusa ku mapazi anu pa tsiku limene Ine ndidzachite zinthu zimenezi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 Kom min Tjener Moses's Lov i Hu, hvem jeg paalagde Vedtægter og Lovbud om alt Israel paa Horeb.
Kumbukirani zophunzitsa za mtumiki wanga Mose, malamulo ndi malangizo amene ndinamupatsa pa Horebu kuti awuze Aisraeli onse.
5 Se, jeg sender eder Profeten Elias, før HERRENS store og frygtelige Dag kommer.
“Taonani, ndidzakutumizirani mneneri Eliya lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Yehova.
6 Han skal vende Fædrenes Hjerte til Sønnerne og Sønnernes til Fædrene, at jeg ikke skal komme og slaa Landet med Band.
Iye adzabweza mitima ya makolo kwa ana awo, ndi mitima ya ana kwa makolo awo. Kupanda kutero ndidzabwera kudzakantha dziko lanu ndi temberero.”