< Lukas 5 >
1 Men det skete, da Folkeskaren trængte sig sammen om ham og hørte Guds Ord, og han stod ved Genezareths Sø,
Tsiku lina Yesu anayima mʼmbali mwa nyanja ya Genesareti, gulu la anthu litamuzungulira likumvetsera mawu a Mulungu.
2 da saa han to Skibe staa ved Søen; men Fiskerne vare gaaede fra dem og toede Garnene.
Iye anaona mabwato awiri ali mʼmphepete mwa nyanja, asodzi amene ankachapa makhoka awo atawasiya pamenepo.
3 Og han gik om Bord i et af Skibene, som var Simons, og bad ham at lægge lidt fra Land; og han satte sig og lærte Skarerne fra Skibet.
Iye analowa mʼbwato limodzi limene linali la Simoni, ndi kumupempha kuti alikankhire mʼkati mwa nyanja pangʼono. Kenaka Iye anakhala pansi nayamba kuphunzitsa anthu ali mʼbwatomo.
4 Men da han holdt op med at tale, sagde han til Simon: „Far ud paa Dybet, og kaster eders Garn ud til en Dræt!”
Atatha kuyankhula anati kwa Simoni, “Kankhirani kwa kuya ndipo muponye makhoka kuti mugwire nsomba.”
5 Og Simon svarede og sagde til ham: „Mester! vi have arbejdet hele Natten og fik intet; men paa dit Ord vil jeg kaste Garnene ud.”
Simoni anayankha kuti, “Ambuye, tagwira ntchito molimbika usiku wonse, koma sitinagwire kanthu. Koma pakuti mwatero, ndiponya makhoka.”
6 Og da de gjorde det, fangede de en stor Mængde Fisk, og deres Garn sønderreves.
Atachita izi, anagwira nsomba zambiri kotero kuti makhoka awo anayamba kungʼambika.
7 Og de vinkede ad deres Stalbrødre i det andet Skib, at de skulde komme og hjælpe dem; og de kom, og de fyldte begge Skibene, saa at de vare nær ved at synke.
Choncho anakodola anzawo a bwato linalo kuti abwere ndi kuwathandiza, ndipo anabwera nadzaza mabwato onse awiri mpaka kuyamba kumira.
8 Men da Simon Peter saa det, faldt han ned for Jesu Knæ og sagde: „Gaa bort fra mig, thi jeg er en syndig Mand, Herre!”
Simoni Petro ataona izi, anagwa pa mawondo a Yesu nati, “Chokani kwa ine Ambuye: Ine ndine munthu wochimwa!”
9 Thi en Rædsel var paakommen ham og alle dem, som vare med ham, over den Fiskedræt, som de havde faaet;
Iye ndi anzake onse anadabwa ndi nsomba zimene anagwira,
10 ligeledes ogsaa Jakob og Johannes, Zebedæus's Sønner, som vare Simons Stalbrødre. Og Jesus sagde til Simon: „Frygt ikke, fra nu af skal du fange Mennesker.”
chimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anzake a Simoniyo. Kenaka Yesu anati kwa Simoni, “Musachite mantha; kuyambira tsopano ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
11 Og de lagde Skibene til Land og forlode alle Ting og fulgte ham.
Kenaka anakokera mabwato awo ku mtunda, nasiya zonse namutsata Iye.
12 Og det skete, medens han var i en af Byerne, se, da var der en Mand fuld af Spedalskhed; og da han saa Jesus, faldt han paa sit Ansigt, bad ham og sagde: „Herre! om du vil, kan du rense mig.”
Yesu ali ku mudzi wina, munthu amene anali ndi khate thupi lonse anabwera kwa Iye. Munthuyo ataona Yesu, anagwa chafufumimba ndipo anamupempha Iye kuti, “Ambuye, ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
13 Og han udrakte Haanden og rørte ved ham og sagde: „Jeg vil; bliv ren!” Og straks forlod Spedalskheden ham.
Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo. Iye anati, “Ine ndikufuna, yeretsedwa!” Ndipo nthawi yomweyo khate lake linachoka.
14 Og han bød ham, at han skulde ikke sige det til nogen, men „gaa bort, og fremstil dig for Præsten, og offer for din Renselse, saaledes som Moses har befalet, til Vidnesbyrd for dem!”
Kenaka Yesu anamulamula kuti, “Usawuze wina aliyense, koma pita, kadzionetse kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose anakulamulirani za kuyeretsedwa kwanu monga umboni kwa iwo.”
15 Men Rygtet om ham udbredte sig end mere, og store Skarer kom sammen for at høre og for at helbredes for deres Sygdomme.
Koma mbiri yake inafalikirabe kwambiri kotero kuti magulu a anthu anabwera kudzamvetsera ndi kuti achiritsidwe ku matenda awo.
16 Men han gik bort til Ørkenerne og bad.
Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.
17 Og det skete en af de Dage, at han lærte, og der sad Farisæere og Lovlærere, som vare komne fra enhver Landsby i Galilæa og Judæa og fra Jerusalem; og Herrens Kraft var hos ham til at helbrede.
Tsiku lina pamene ankaphunzitsa, Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, amene anachokera ku midzi yonse ya Galileya ndi ku Yudeya ndi Yerusalemu, anakhala pansi pomwepo. Ndipo mphamvu ya Ambuye inalipo yakuti Iye achiritse odwala.
18 Og se, nogle Mænd bare paa en Seng en Mand, som var værkbruden, og de søgte at bære ham ind og lægge ham foran ham.
Amuna ena anabwera atanyamula munthu wofa ziwalo pa mphasa ndipo anayesa kumulowetsa mʼnyumba kuti amugoneke pamaso pa Yesu.
19 Og da de ikke fandt nogen Vej til at bære ham ind for Skarens Skyld, stege de op oven paa Taget og firede ham tillige med Sengen ned imellem Tagstenene midt iblandt dem foran Jesus.
Atalephera kupeza njira yochitira zimenezi chifukwa cha gulu la anthu, anakwera naye pa denga ali pa mphasa pomwepo ndi kumutsitsira mʼkati pakati pa gulu la anthu, patsogolo penipeni pa Yesu.
20 Og da han saa deres Tro, sagde han: „Menneske! dine Synder ere dig forladte.”
Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati, “Mnzanga, machimo ako akhululukidwa.”
21 Og de skriftkloge og Farisæerne begyndte at tænke saaledes ved sig selv: „Hvem er denne, som taler Gudsbespottelser? Hvem kan forlade Synder, uden Gud alene?”
Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anayamba kuganiza mwa iwo okha kuti, “Kodi munthu uyu ndi ndani amene ayankhula zamwano? Kodi ndani amene angakhululukire machimo kupatula Mulungu?”
22 Men da Jesus kendte deres Tanker, svarede han og sagde til dem: „Hvad tænke I paa i eders Hjerter?
Yesu anadziwa zomwe iwo amaganiza ndipo anafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukuganiza zimenezi mʼmitima mwanu?
23 Hvilket er lettest at sige: Dine Synder ere dig forladte? eller at sige: Staa op og gaa?
Kodi chapafupi ndi chiti: kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Nyamuka ndipo yenda?’”
24 Men for at I skulle vide, at Menneskesønnen har Magt paa Jorden til at forlade Synder,” saa sagde han til den værkbrudne: „Jeg siger dig, staa op, og tag din Seng, og gaa til dit Hus!”
Koma kuti inu mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo, Iye anati kwa munthu wofa ziwaloyo, “Ine ndikuwuza iwe kuti, ‘Imirira, nyamula mphasa ndipo uzipita kwanu.’”
25 Og han stod straks op for deres Øjne og tog det, som han laa paa, og gik hen til sit Hus og priste Gud.
Nthawi yomweyo anayimirira patsogolo pawo, nanyamula mphasa yake ndipo anapita kwawo akuyamika Mulungu.
26 Og Forfærdelse betog alle, og de priste Gud; og de bleve fulde af Frygt og sagde: „Vi have i Dag set utrolige Ting.”
Aliyense anadabwa ndi kuchita mantha ndipo anayamika Mulungu. Iwo anadabwa kwambiri ndipo anati, “Lero taona zinthu zosayiwalika.”
27 Og derefter gik han ud og saa en Tolder ved Navn Levi sidde ved Toldboden, og han sagde til ham: „Følg mig!”
Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.”
28 Og han forlod alle Ting og stod op og fulgte ham.
Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.
29 Og Levi gjorde et stort Gæstebud for ham i sit Hus; og der var en stor Skare af Toldere og andre, som sade til Bords med dem.
Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi.
30 Og Farisæerne og deres skriftkloge knurrede imod hans Disciple og sagde: „Hvorfor spise og drikke I med Toldere og Syndere?”
Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
31 Og Jesus svarede og sagde til dem: „De raske trænge ikke til Læge, men de syge.
Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala.
32 Jeg er ikke kommen for at kalde retfærdige, men Syndere til Omvendelse.”
Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”
33 Men de sagde til ham: „Johannes's Disciple faste ofte og holde Bønner og Farisæernes ligesaa; men dine spise og drikke?”
Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”
34 Men Jesus sagde til dem: „Kunne I vel faa Brudesvendene til at faste, saa længe Brudgommen er hos dem?
Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo?
35 Men der skal komme Dage, da Brudgommen bliver tagen fra dem; da skulle de faste i de Dage.”
Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”
36 Men han sagde ogsaa en Lignelse til dem: „Ingen river en Lap af et nyt Klædebon og sætter den paa et gammelt Klædebon; ellers river han baade det nye sønder, og Lappen fra det nye vil ikke passe til det gamle.
Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale.
37 Og ingen kommer ung Vin paa gamle Læderflasker; ellers sprænger den unge Vin Læderflaskerne, og den spildes, og Læderflaskerne ødelægges.
Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka.
38 Men man skal komme ung Vin paa nye Læderflasker, saa blive de begge bevarede.
Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano.
39 Og ingen, som har drukket den gamle, vil have den unge; thi han siger: Den gamle er god.”
Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’”