< 3 Mosebog 7 >
1 Dette er Loven om Skyldofferet. Det er højhelligt.
“‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
2 Der, hvor Brændofferet slagtes, skal Skyldofferet slagtes. Dets Blod skal sprænges rundt om paa Alteret,
Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
3 og alt dets Fedt skal frembæres. Fedthalen, Fedtet, der dækker Indvoldene, og alt Fedtet paa Indvoldene,
Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
4 begge Nyrerne med det Fedt, som sidder paa dem ved Lændemusklerne, og Leverlappen, som skal skilles fra ved Nyrerne.
Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
5 Og Præsten skal bringe det som Røgoffer paa Alteret, et Ildoffer for HERREN. Det er et Skyldoffer.
Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
6 Alle af Mandkøn blandt Præsterne maa spise det; paa et helligt Sted skal det spises; det er højhelligt.
Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
7 Det er med Skyldofferet som med Syndofferet, en og samme Lov gælder for dem: Det tilfalder den Præst, der skaffer Soning ved det.
“‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
8 Den Præst, som frembærer nogens Brændoffer, ham skal Huden af det Brændoffer, han frembærer, tilfalde.
Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
9 Ethvert Afgrødeoffer, der bages i Ovnen, eller som er tilberedt i Pande eller paa Plade, tilfalder den Præst, der frembærer det;
Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
10 men ethvert Afgrødeoffer, der er rørt i Olie eller tørt, tilfalder alle Arons Sønner, den ene lige saa vel som den anden.
Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
11 Dette er Loven om Takofferet, som bringes HERREN.
“‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
12 Hvis det bringes som Lovprisningsoffer, skal han sammen med Slagtofferet, der hører til hans Lovprisningsoffer, frembære usyrede Kager, rørte i Olie, usyrede Fladbrød, smurte med Olie, og fint Hvedemel, æltet til Kager, rørte i Olie;
“‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
13 sammen med syrede Brødkager skal han frembære sin Offergave som sit Lovprisningstakoffer.
Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
14 Han skal deraf frembære een Kage af hver Offergave som en Offerydelse til HERREN; den tilfalder den Præst, der sprænger Blodet af Takofferet paa Alteret.
Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
15 Kødet af hans Lovprisningstakoffer skal spises paa selve Offerdagen, intet deraf maa gemmes til næste Morgen.
Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
16 Er hans Offergaver derimod et Løfteoffer eller et Frivilligoffer, skal det vel spises paa selve Offerdagen, men hvad der levnes, maa spises Dagen efter;
“‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
17 men hvad der saa er tilbage af Offerkødet, skal opbrændes paa den tredje Dag;
Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
18 og hvis der spises noget af hans Takoffers Kød paa den tredje Dag, saa vil den, som bringer Offeret, ikke kunne finde Guds Velbehag, det skal ikke tilregnes ham, men regnes for urent Kød, og den, der spiser deraf, skal undgælde for sin Brøde.
Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
19 Det Kød, der kommer i Berøring med noget som helst urent, maa ikke spises, det skal opbrændes. I øvrigt maa enhver, der er ren, spise Kødet;
“‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
20 men enhver, som i uren Tilstand spiser Kød af HERRENS Takoffer, skal udryddes af sin Slægt;
Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
21 og naar nogen rører ved noget urent, enten menneskelig Urenhed eller urent Kvæg eller nogen Slags urent Kryb, og saa spiser Kød af HERRENS Takoffer, skal han udryddes af sin Slægt.
Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
22 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
23 Tal til Israeliterne og sig: I maa ikke spise noget som helst Fedt af Okser, Faar eller Geder.
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
24 Fedt af selvdøde og sønderrevne Dyr maa bruges til alt, men I maa under ingen Omstændigheder spise det.
Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
25 Thi enhver, der spiser Fedtet af det Kvæg, hvoraf der bringes HERREN Ildofre, den, der spiser noget deraf, skal udryddes af sit Folk.
Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
26 Og I maa heller ikke nyde noget som helst Blod af Fugle eller Kvæg, hvor I end opholder eder;
Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
27 enhver, der nyder noget som helst Blod, skal udryddes af sin Slægt.
Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
28 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
29 Tal til Israeliterne og sig: Den, der bringer HERREN sit Takoffer, skal af sit Takoffer frembære for HERREN den ham tilkommende Offergave;
“Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
30 med egne Hænder skal han frembære HERRENS Ildofre. Han skal frembære Fedtet tillige med Brystet; Brystet, for at Svingningen kan udføres dermed for HERRENS Aasyn;
Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
31 og Præsten skal bringe Fedtet som Røgoffer paa Alteret, men Brystet skal tilfalde Aron og hans Sønner.
Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
32 Desuden skal I give Præsten højre Kølle som Offerydelse af eders Takofre.
Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
33 Den af Arons Sønner, der frembærer Takofferets Blod og Fedtet, ham tilfalder højre Kølle som hans Del.
Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
34 Thi Svingningsbrystet og Offerydelseskøllen tager jeg fra Israeliterne af deres Takofre og giver dem til Præsten Aron og hans Sønner, en evig gyldig Rettighed, som de har Krav paa hos Israeliterne.
Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
35 Det er Arons og hans Sønners Del af HERRENS Ildofre, den, som blev givet dem, den Dag han lod dem træde frem for at gøre Præstetjeneste for HERREN,
Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
36 den, som HERREN, den Dag han salvede dem, bød Israeliterne at give dem, en evig gyldig Rettighed, som de har Krav paa fra Slægt til Slægt.
Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
37 Det er Loven om Brændofferet, Afgrødeofferet, Syndofferet, Skyldofferet, Indsættelsesofferet og Takofferet,
Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
38 som HERREN paalagde Moses paa Sinaj Bjerg, den Dag han bød Israeliterne at bringe HERREN deres Offergaver i Sinaj Ørken.
Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.