< 3 Mosebog 12 >

1 Og HERREN talede til Moses og sagde:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
2 Tal til Israeliterne og sig: Naar en Kvinde bliver frugtsommelig og føder en Dreng, skal hun være uren i syv Dage; ligesom i den Tid hun har sin maanedlige Urenhed, skal hun være uren.
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Mkazi akakhala woyembekezera, nabala mwana wa mwamuna, mkaziyo adzakhala wodetsedwa kwa masiku asanu ndi awiri, ngati pa masiku ake akusamba.
3 Paa den ottende Dag skal Drengen omskæres paa sin Forhud.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, mwanayo achite mdulidwe.
4 Derefter skal hun holde sig hjemme i tre og tredive Dage, medens hun har sit Renselsesblod; hun maa ikke røre ved noget helligt eller komme til Helligdommen, før hendes Renselsestid er omme.
Mkaziyo adikire masiku ena 33 kuti ayeretsedwe ku matenda ake. Asakhudze kanthu kalikonse koyera kapena kulowa mʼmalo wopatulika mpaka masiku a kuyeretsedwa kwake atatha.
5 Føder hun derimod et Pigebarn, skal hun være uren i to Uger ligesom under sin maanedlige Urenhed; og derpaa skal hun holde sig hjemme i seks og tresindstyve Dage, medens hun har sit Renselsesblod.
Ngati abala mwana wamkazi, adzakhala wodetsedwa kwa masabata awiri, monga zikhalira pa nthawi yake yosamba. Ndipo mkaziyo adikire masiku ena 66, kuti ayeretsedwe ku matenda akewo.
6 Naar hendes Renselsestid er omme, skal hun, baade efter et Drengebarn og et Pigebarn, bringe et aargammelt Lam som Brændoffer og en Dueunge eller Turteldue som Syndoffer til Præsten ved Aabenbaringsteltets Indgang;
“‘Masiku ake wodziyeretsa akatha, kaya ndi a mwana wamwamuna kapena a mwana wamkazi, abwere kwa wansembe ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi pa khomo la tenti ya msonkhano kuti ikhale nsembe yopsereza. Abwerenso ndi chiwunda cha nkhunda kapena njiwa kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
7 og han skal frembære det for HERRENS Aasyn og skaffe hende Soning, saa hun bliver ren efter sit Blodtab. Det er Loven om en Kvinde, der føder, hvad enten det er en Dreng eller en Pige.
Wansembeyo apereke zimenezi pamaso pa Yehova pochita mwambo wopepesera mkaziyo. Ndipo mkaziyo adzakhala woyeretsedwa ku msambo wake. “‘Amenewa ndiwo malamulo a mkazi amene wabala mwana wamwamuna kapena wamkazi.
8 Men hvis hun ikke evner at give et Lam, skal hun tage to Turtelduer eller Dueunger, en til Brændoffer og en til Syndoffer, og Præsten skal skaffe hende Soning, saa hun bliver ren.
Ngati mkaziyo sangathe kupeza mwana wankhosa, abwere ndi njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri: imodzi ikhale ya nsembe yopsereza ndipo inayo ikhale ya nsembe yopepesera machimo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera wa mkaziyo ndipo adzayeretsedwa.’”

< 3 Mosebog 12 >