< Dommer 18 >

1 I de Dage var der ingen Konge i Israel, og i de Dage var Daniternes Stamme i Færd med at søge sig en Arvelod, hvor de kunde bo, thi hidindtil var der ikke tilfaldet dem nogen Arvelod blandt Israels Stammer.
Masiku amenewo munalibe mfumu mu Israeli. Ndipo anthu a fuko la Dani amafunafuna malo okhalamo ngati cholowa chawo, chifukwa kufikira nthawi imeneyo anali asanalandire cholowa chawo pakati pa mafuko a Israeli.
2 Daniterne udtog da af deres Slægt fem stærke Mænd fra Zor'a og Esjtaol og udsendte dem for at udspejde og undersøge Landet, og de sagde til dem: »Drag hen og undersøg Landet!« De kom da til Mikas Hus i Efraims Bjerge og overnattede der.
Choncho fuko la Dani linatumiza kuchokera ku mabanja awo onse anthu olimba mtima asanu. Anthuwa anachokera ku Zora ndi ku Esitaoli ndipo anatumidwa kukazonda ndi kuliyendera dzikolo. Anthu amenewa ankayimira fuko lonse la Dani. Anthuwa anawawuza kuti, “Pitani mukazonde dzikolo.” Anthuwa anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ndi kupita ku nyumba ya Mika komwe anakagona.
3 Da de kom i Nærheden af Mikas Hus og kendte den unge Levits Stemme, tog de derind og spurgte ham: »Hvem har ført dig herhen, hvad tager du dig for paa dette Sted, og hvorfor er du her?«
Ali ku nyumba ya Mika anazindikira mawu a mnyamata, Mlevi uja. Choncho anapita kwa iye namufunsa kuti, “Unabwera ndi ndani kuno? Nanga ukuchita chiyani ku malo ano? Komanso nʼchifukwa chiyani uli kuno?”
4 Han svarede dem: »Det og det har Mika gjort for mig; han har lejet mig til Præst.«
Iye anawawuza zimene Mika anamuchitira ndipo anati, “Iye anandilemba ntchito ndipo ndine wansembe wake.”
5 Da sagde de til ham: »Adspørg da Gud, at vi kan faa at vide, om vor Færd skal lykkes!«
Kenaka iwo anati kwa iye, “Chonde tifunsire kwa Mulungu kuti tidziwe ngati ulendo wathuwu tiyende bwino.”
6 Præsten sagde da til dem: »Far med Fred, HERREN vaager over eders Færd!«
Wansembeyo anawayankha kuti, “Pitani mu mtendere, Yehova ali ndi inu pa ulendo wanuwu.”
7 Saa drog de fem Mænd videre og kom til Lajisj; og de saa, at Byen levede trygt paa Zidoniernes Vis, at Folket der levede sorgløst og trygt og ikke manglede nogen Verdens Ting, men var rigt, og at de boede langt fra Zidonierne og intet havde med Aramæerne at gøre.
Choncho anthu asanuwo ananyamuka ndipo anafika ku Laisi, kumene anaona kuti anthu ankakhala mwabata monga anthu a ku Sidoni. Anali anthu opanda chowavuta ndiponso aphee. Tsono popeza mʼdziko mwawo analibe chosowa, iwo anali a chuma. Anaonanso kuti anthuwo ankakhala kutali ndi Sidoni ndipo analibe ubale ndi wina aliyense.
8 Da de kom tilbage til deres Brødre i Zor'a og Esjtaol, spurgte disse dem: »Hvad har I at melde?«
Ozonda dziko aja atabwerera kwa abale awo ku Zora ndi Esitaoli, abale awowo anawafunsa kuti, “Mwaonako zotani?”
9 De svarede: »Kom, lad os drage op til Lajisj, thi vi har set Landet, og se, det er saare godt! Hvorfor holder I eder uvirksomme? Nøl ikke med at drage hen og underlægge eder Landet!
“Tiyeni tikamenyane nawo nkhondo popeza taliona dziko lawolo kuti ndi lachonde kwambiri. Kodi simuchitapo kanthu? Musachite mphwayi kupita mʼdzikomo ndi kukalilanda.
10 Thi Gud har givet det i eders Haand — et Sted, hvor der ikke er Mangel paa nogen Verdens Ting! Naar I kommer derhen, kommer I til et Folk, der lever i Tryghed, og det er et vidtstrakt Land!«
Mukalowa, mukapeza anthu amene ali osatekeseka ndi dziko lalikulu. Yehova wakupatsani dziko limeneli. Malowo ngosasowa kanthu kalikonse kopezeka pa dziko lapansi.”
11 Saa brød 600 væbnede Mænd af Daniternes Slægt op fra Zor'a og Esjtaol,
Kenaka anthu 600 a fuko la Dani ananyamuka ku Zora ndi Esitaoli atanyamula zida za nkhondo.
12 og de drog op og slog Lejr i Kirjat-Jearim i Juda; derfor kalder man endnu den Dag i Dag dette Sted hans Lejr; det ligger vesten for Kirjat-Jearim.
Tsono anakamanga msasa ku Kiriati-Yearimu mʼdziko la Yuda. Malowa ali kumadzulo kwa Kiriati-Yearimu. Ichi ndi chifukwa chake malowo akutchedwa Mahane Dani mpaka lero.
13 Derfra drog de over til Efraims Bjerge; og da de kom til Mikas Hus,
Kuchokera kumeneko anapita ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anafika ku nyumba ya Mika.
14 tog de fem Mænd, der havde været henne at udspejde Landet, til Orde og sagde til deres Brødre: »Ved I, at der i Husene her findes en Efod, en Husgud og et udskaaret og støbt Billede? Saa indser I vel, hvad I har at gøre!«
Anthu asanu amene anakazonda dziko la Laisi anati kwa abale awo, “Kodi mukudziwa kuti imodzi mwa nyumba izi muli efodi, mafano a mʼnyumba otchedwa terafimu, fano losema ndiponso fano lokuta ndi siliva? Ndiye mudziwe chochita.”
15 De begav sig derhen og kom til den unge Levits Hus, Mikas Hus, og hilste paa ham,
Choncho anthuwa anapatuka napita ku nyumba ya Mika kumene mnyamata, Mlevi uja ankakhala ndipo anamufunsa za mmene zinthu zilili.
16 medens de 600 væbnede danitiske Mænd stod ved Porten.
Nthawi imeneyi nʼkuti anthu 600 a fuko la Dani aja atayima pa chipata atanyamula zida za nkhondo.
17 Og de fem Mænd, der havde været henne at udspejde Landet, gik op og tog det udskaarne og støbte Billede, Efoden og Husguden, medens Præsten og de 600 væbnede Mænd stod ved Porten.
Anthu asanu amene anakazonda dziko aja analowa ndi kukatenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba lotchedwa terafimu, ndi fano lokutidwa ndi siliva. Nthawiyi nʼkuti wansembe uja ndi anthu 600 okhala ndi zida za nkhondo aja ali chiyimire pa chipata.
18 Hine gik ind i Mikas Hus og tog det udskaarne og støbte Billede, Efoden og Husguden. Præsten sagde til dem: »Hvad er det, I gør?«
Anthuwo atalowa mʼnyumba ya Mika ndi kutenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba, ndi fano lokutidwa ndi siliva, wansembeyo anawafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
19 Og de svarede ham: »Stille, læg Fingeren paa Munden og følg med os og bliv vor Fader og Præst! Hvad baader dig vel bedst, at være Præst for een Mands Hus eller for en Stamme og Slægt i Israel?«
Iwo anamuyankha kuti, “Khala chete usayankhule. Tsagana nafe ndipo udzakhala mlangizi wathu ndi wansembe wathu. Kodi si kwabwino kwa iwe kukhala wansembe wa fuko lonse la Israeli mʼmalo mokhala wansembe wa munthu mmodzi yekha?”
20 Da blev Præsten glad, tog Efoden, Husguden og Gudebilledet og sluttede sig til Krigsfolkene.
Wansembeyo anakondwera ndipo anatenga efodi, fano la mʼnyumba ndi fano losema natsagana nawo.
21 Derpaa vendte de om og drog bort, idet de stillede Kvinderne og Børnene, Kvæget og Trosset forrest i Toget.
Choncho iwo anatembenuka nachoka, atatsogoza ana, zoweta ndi katundu wawo yense.
22 Da de var kommet et Stykke fra Mikas Hus, stævnedes Mændene i de Huse, der laa ved Mikas Hus, sammen, og de indhentede Daniterne.
Atayenda mtunda pangʼono kuchokera pa nyumba ya Mika, anthu amene amakhala pafupi ndi nyumba ya Mika anasonkhana kulondola a fuko la Dani aja, ndipo anawapeza.
23 Da de raabte efter Daniterne, vendte disse sig om og sagde til Mika: »Hvad er der i Vejen, siden du har kaldt Folk til Hjælp?«
Atawafuwulira, a fuko la Dani aja anachewuka ndipo anafunsa Mika kuti, “Chavuta nʼchiyani kuti usonkhanitse anthu chotere?”
24 Han svarede: »I har taget min Gud, som jeg havde lavet mig, tillige med Præsten og er rejst eders Vej! Hvad har jeg nu tilbage? Hvor kan I spørge mig, hvad der er i Vejen?«
Iye anayankha kuti, “Inu mwanditengera milungu imene ndinapanga pamodzi ndi wansembe nʼkumapita. Tsono ine ndatsala ndi chiyani? Ndiye inu mungafunse kuti chavuta nʼchiyani?”
25 Men Daniterne svarede ham: »Lad os ikke høre et Ord mere fra dig, ellers kunde det hænde, at nogle Mænd, som er bitre i Hu, faldt over eder, og at du satte baade dit eget og dine Husfolks Liv paa Spil!«
Anthu a fuko la Dani aja anayankha kuti, “Usayankhuleponso kanthu chifukwa anthu awa angapse mtima nakumenya ndipo iwe ndi banja lako lonse nʼkutayapo miyoyo yanu.”
26 Dermed drog Daniterne deres Vej, og da Mika saa, at de var ham for stærke, vendte han om og begav sig tilbage til sit Hus.
Choncho anthu a fuko la Dani anapitiriza ulendo wawo. Mika ataona kuti anthuwo anali amphamvu kuposa iye, anangotembenuka kubwerera kwawo.
27 De tog saa Guden, som Mika havde lavet, tillige med hans Præst og drog mod Lajisj, mod et Folk, der levede sorgløst og trygt, huggede dem ned med Sværdet og stak Ild paa Byen,
Anthu a fuko la Dani aja anatenga zinthu zimene Mika anapanga pamodzi ndi wansembe uja. Iwo anakafika ku Laisi kwa anthu a phee, osatekeseka aja ndipo anawathira nkhondo, nawapha ndi kutentha mzindawo ndi moto.
28 uden at nogen kunde komme den til Hjælp, thi den laa langt fra Zidon, og de havde intet med Aramæerne at gøre. Den ligger i Bet-Rehobs Dal. Saa byggede de Byen op igen og bosatte sig der;
Panalibe wowapulumutsa chifukwa anali kutali ndi Sidoni ndiponso sanali pa ubale ndi wina aliyense. Mzindawo unali mʼchigwa cha Beti-Rehobu. Anthu a fuko la Adaniwo anawumanganso mzindawo ndi kumakhalamo.
29 og de gav den Navnet Dan efter deres Stamfader Dan, Israels Søn; men før var Byens Navn Lajisj.
Iwo anawutcha mzindawo Dani, kutengera dzina la kholo lawo Dani, amene anali mwana wa Israeli, ngakhale kuti mzindawo poyamba unali Laisi.
30 Derpaa stillede Daniterne Gudebilledet op hos sig; og Jonatan, en Søn af Moses's Søn Gersom, og hans Efterkommere var Præster for Daniternes Stamme, indtil Landets Indbyggere førtes i Landflygtighed.
Anthu a fuko la Dani anayimiritsa fano losema lija. Yonatani mwana wa Geresomu, mwana wa Mose pamodzi ndi ana ake onse anakhala ansembe a fuko la Dani mpaka pa tsiku la ukapolo wa dzikolo.
31 Og det Gudebillede, Mika havde lavet sig, stillede de op hos sig, og det stod der, al den Tid Guds Hus var i Silo.
Choncho anthu a fuko la Dani ankapembedza fano limene Mika anapanga nthawi yonse pamene nyumba ya Mulungu inali ku Silo.

< Dommer 18 >