< Dommer 14 >

1 Engang Samson kom ned til Timna, saa han en af Filisternes Døtre der.
Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
2 Og da han kom tilbage derfra, fortalte han sin Fader og Moder det og sagde: »Jeg har set en Kvinde i Timna, en af Filisternes Døtre; nu maa I hjælpe mig at faa hende til Hustru!«
Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
3 Hans Fader og Moder svarede ham: »Findes der da ingen Kvinde blandt dine Landsmænds Døtre eller i hele dit Folk, siden du vil gaa hen og tage dig en Hustru hos de uomskaarne Filistere?« Men Samson svarede sin Fader: »Nej, hende maa du hjælpe mig til, thi det er hende, jeg synes om!«
Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
4 Hans Fader og Moder forstod ikke, at det kom fra HERREN, som søgte en Anledning til Strid over for Filisterne. Paa den Tid havde Filisterne nemlig Magten over Israel.
(Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
5 Samson tog nu med sin Fader og Moder ned til Timna. Da de naaede Vingaardene uden for Timna, se, da kom en ung Løve brølende imod ham.
Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
6 Saa kom HERRENS Aand over ham, og han sønderrev den med sine bare Næver, som var det et Gedekid; men sin Fader og Moder fortalte han ikke, hvad han havde gjort.
Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
7 Derpaa drog han ned og bejlede til Kvinden; thi Samson syntes om hende.
Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
8 Da han efter nogen Tids Forløb vendte tilbage for at ægte hende, gik han hen for at se til Løvens Aadsel, og se, da var der en Bisværm og Honning i Løvens Krop.
Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
9 Han tog da Honningen i sine Hænder og spiste deraf, medens han gik videre; og da han kom til sin Fader og Moder, gav han dem noget deraf, og de spiste; men han sagde dem ikke, at han havde taget Honningen fra Løvens Krop.
Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
10 Saa drog Samson ned til Kvinden; og de holdt Gilde, som de unge havde for Skik.
Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
11 Da de saa ham, udvalgte de tredive Brudesvende til at ledsage ham.
Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
12 Og Samson sagde til dem: »Jeg vil give eder en Gaade at gætte; hvis I i Løbet af de syv Gildedage kan sige mig Løsningen, vil jeg give eder tredive Linnedkjortler og tredive Sæt klæder;
Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
13 men kan I ikke sige mig den, skal I give mig tredive Linnedkjortler og tredive Sæt klæder!« De svarede: »Sig din Gaade frem og lad os høre den!«
Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
14 Da sagde han til dem: »Fra Æderen kom Æde, fra den stærke Sødme!« Men da de tre Dage var omme, havde de ikke kunnet gætte Gaaden,
Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
15 og den fjerde Dag sagde de til Samsons Hustru: »Lok din Mand til at sige os Løsningen, ellers brænder vi dig og din Faders Hus inde! Har I budt os herhen for at tage alting fra os?«
Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
16 Da hang Samsons Hustru over ham med Graad og sagde: »Du hader mig jo og elsker mig ikke! Du har givet mine Landsmænd en Gaade at gætte, og mig har du ikke sagt Løsningen!« Han svarede hende: »Jeg har ikke sagt min Fader eller Moder den, og saa skulde jeg sige dig den!«
Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
17 Men hun hang over ham med Graad, de syv Dage Gildet varede; og den syvende Dag sagde han hende Løsningen, fordi hun plagede ham. Saa sagde hun sine Landsmænd Gaadens Løsning;
Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
18 og den syvende Dag, før han gik ind i Kammeret, sagde Byens Mænd til ham: »Hvad er sødere end Honning, og hvad er stærkere end en Løve?« Men han svarede dem: »Havde I ikke pløjet med min Kalv, havde I ikke gættet min Gaade!«
Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
19 Da kom HERRENS Aand over ham, og han drog ned til Askalon, slog tredive Mænd ihjel der, trak deres Tøj af dem og gav Klæderne til dem, der havde sagt Løsningen paa Gaaden. Og hans Vrede blussede op, og han drog tilbage til sin Faders Hus.
Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
20 Men Samsons Hustru blev givet til den Brudesvend, som havde været hans Brudefører.
Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.

< Dommer 14 >