< Dommer 10 >

1 Efter Abimelek fremstod som Israels Befrier Tola, en Søn af Dodos Søn Pua, en Mand af Issakar, som boede i Sjamir i Efraims Bjerge.
Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu.
2 Han var Dommer i Israel i tre og tyve Aar. Da han døde, blev han jordet i Sjamir.
Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.
3 Efter ham fremstod Gileaditen Ja'ir; han var Dommer i Israel i to og tyve Aar.
Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22.
4 Han havde tredive Sønner, som red paa tredive Æsler, og de havde tredive Byer, som endnu den Dag i Dag kaldes Ja'irs Teltbyer; de ligger i Gilead.
Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi.
5 Da Ja'ir døde, blev han jordet i Kamon.
Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.
6 Men Israeliterne blev ved at gøre, hvad der var ondt i HERRENS Øjne, idet de dyrkede Ba'alerne og Astarterne og Aramæernes, Zidons, Moabs, Ammoniternes og Filisternes Guder og faldt fra HERREN og undlod at dyrke ham.
Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova.
7 Da blussede HERRENS Vrede op mod Israel, og han gav dem til Pris for Filisterne og Ammoniterne,
Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni.
8 som kuede og mishandlede Israeliterne i det Aar; i atten Aar kuede de alle Israeliterne hinsides Jordan i Amoriternes Land i Gilead.
Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi.
9 Og Ammoniterne satte over Jordan for ogsaa at angribe Juda, Benjamin og Efraims Slægt, saa at Israeliterne kom i stor Nød.
Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri.
10 Da raabte Israeliterne til HERREN og sagde: »Vi har syndet imod dig, thi vi har forladt HERREN vor Gud og dyrket Ba'alerne!«
Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”
11 Men HERREN svarede Israeliterne: »Har ikke Ægypterne, Amoriterne, Ammoniterne, Filisterne,
Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti?
12 Zidonierne, Amalekiterne og Midjaniterne mishandlet eder? Og da I raabte til mig, frelste jeg eder af deres Haand.
Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa?
13 Men I forlod mig og dyrkede andre Guder! Derfor vil jeg ikke mere frelse eder!
Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso.
14 Gaa nu hen og raab til de Guder, I udvalgte eder, og lad dem frelse eder i eders Nød!«
Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”
15 Da sagde Israeliterne til HERREN: »Vi har syndet! Gør med os, hvad dig tykkes godt, men frels os blot nu!«
Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.”
16 Og de skilte sig af med de fremmede Guder og dyrkede HERREN; da kunde han ikke længer holde ud at se Israels Nød.
Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.
17 Ammoniterne stævnedes sammen, og de slog Lejr i Gilead; ogsaa Israeliterne samlede sig, og de slog Lejr i Mizpa.
Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa.
18 Da sagde Folket, Gileads Høvdinger, til hverandre: »Hvis der findes en Mand, som vil tage Kampen op med Ammoniterne, skal han være Høvding over alle Gileads Indbyggere!«
Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”

< Dommer 10 >