< Job 41 >
1 Kan du trække Krokodillen op med Krog og binde dens Tunge med Snøre?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 Kan du mon stikke et Siv i dens Snude, bore en Krog igennem dens Kæber?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 Mon den vil trygle dig længe og give dig gode Ord?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 Mon den vil indgaa en Pagt med dig, saa du faar den til Træl for evigt?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 Han du mon lege med den som en Fugl og tøjre den for dine Pigebørn?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 Falbyder Fiskerlauget den og stykker den ud mellem Sælgerne?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 Mon du kan spække dens Hud med Kroge og med Harpuner dens Hoved?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Læg dog engang din Haand paa den! Du vil huske den Kamp og gør det ej mer.
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 Det Haab vilde blive til Skamme, alene ved Synet laa du der.
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 Ingen drister sig til at tirre den, hvem holder Stand imod den?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Hvem møder den og slipper fra det hvem under hele Himlen?
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 Jeg tier ej om dens Lemmer, hvor stærk den er, hvor smukt den er skabt.
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Hvem har trukket dens Klædning af, trængt ind i dens dobbelte Panser?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 Hvem har aabnet dens Ansigts Døre? Rundt om dens Tænder er Rædsel.
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 Dens Ryg er Reder af Skjolde, dens Bryst er et Segl af Sten;
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 de sidder tæt ved hverandre, Luft kommer ikke ind derimellem;
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 de hænger fast ved hverandre, uadskilleligt griber de ind i hverandre.
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 Dens Nysen fremkalder straalende Lys, som Morgenrødens Øjenlaag er dens Øjne.
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 Ud af dens Gab farer Fakler, Ildgnister spruder der frem.
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 Em staar ud af dens Næsebor som af en ophedet, kogende Kedel.
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 Dens Aande tænder som glødende Kul, Luer staar ud af dens Gab.
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 Styrken bor paa dens Hals, og Angsten hopper foran den.
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 Tæt sidder Kødets Knuder, som støbt til Kroppen; de rokkes ikke;
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 fast som Sten er dens Hjerte støbt, fast som den nederste Møllesten.
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 Naar den rejser sig, gyser Helte, fra Sans og Samling gaar de af Skræk.
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 Angriberens Sværd holder ikke Stand, ej Kastevaaben, Spyd eller Pil.
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 Jern regner den kun for Halm og Kobber for trøsket Træ;
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 Buens Søn slaar den ikke paa Flugt, Slyngens Sten bliver Straa for den,
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 Stridskøllen regnes for Rør, den ler ad det svirrende Spyd.
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 Paa Bugen er der skarpe Rande, dens Spor i Dyndet er som Tærskeslædens;
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 Dybet faar den i Kog som en Gryde, en Salvekedel gør den af Floden;
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 bag den er der en lysende Sti, Dybet synes som Sølverhaar.
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 Dens Lige findes ikke paa Jord, den er skabt til ikke at frygte.
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Alt, hvad højt er, ræddes for den, den er Konge over alle stolte Dyr.
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”