< Job 40 >
1 Og HERREN svarede Job og sagde:
Yehova anati kwa Yobu:
2 Vil den trættekære tvistes med den Almægtige? Han, som revser Gud, han svare herpaa!
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Da svarede Job HERREN og sagde:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 Se, jeg er ringe, hvad skal jeg svare?
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 Jeg lægger min Haand paa min Mund! Een Gang har jeg talt, gentager det ikke, to Gange, men gør det ej mer!
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Da svarede HERREN Job ud fra Stormvejret og sagde:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 Omgjord som en Mand dine Lænder, jeg vil spørge, og du skal lære mig!
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Mon du vil gøre min Ret til intet, dømme mig, for at du selv kan faa Ret?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 Har du en Arm som Gud, kan du tordne med Brag som han?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Smyk dig med Højhed og Storhed, klæd dig i Glans og Herlighed!
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Udgyd din Vredes Strømme, slaa de stolte ned med et Blik,
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 bøj med et Blik de stolte og knus paa Stedet de gudløse,
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 skjul dem i Støvet til Hobe og lænk deres Aasyn i Skjulet!
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Saa vil jeg ogsaa love dig for Sejren, din højre har vundet.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 Se Nilhesten! Den har jeg skabt saavel som dig. Som Oksen æder den Græs.
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Se, hvilken Kraft i Lænderne og hvilken Styrke i Bugens Muskler!
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 Halen holder den stiv som en Ceder, Bovens Sener er flettet sammen;
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 dens Knogler er Rør af, Kobber, Benene i den som Stænger af Jern.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 Den er Guds ypperste Skabning, skabt til at herske over de andre;
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 thi Foder til den bærer Bjergene, hvor Markens Vildt har Legeplads.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 Den lægger sig hen under Lotusbuske, i Skjul af Siv og Rør;
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 Lotusbuskene giver den Tag og Skygge, Bækkens Pile yder den Hegn.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Den taber ej Modet, naar Jordan stiger, er rolig, om Strømmen end svulmer mod dens Gab.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 Hvem kan gribe den i dens Tænder og trække Reb igennem dens Snude?
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?