< Job 39 >
1 Kender du Tiden, da Stengeden føder, tager du Vare paa Hindenes Veer,
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 tæller du mon deres Drægtigheds Maaneder, kender du Tiden, de føder?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 De lægger sig ned og føder og kaster Kuldet,
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Ungerne trives, gror til i det frie, løber bort og kommer ej til dem igen.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Hvem slap Vildæslet løs, hvem løste mon Steppeæslets Reb,
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 som jeg gav Ørkenen til Hjem, den salte Steppe til Bolig?
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 Det ler ad Byens Larm og hører ej Driverens Skælden;
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 det ransager Bjerge, der har det sin Græsgang, det leder hvert Græsstraa op.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 Er Vildoksen villig at trælle for dig, vil den staa ved din Krybbe om Natten?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Binder du Reb om dens Hals, pløjer den Furerne efter dig?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Stoler du paa dens store Kræfter; overlader du den din Høst?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Tror du, den kommer tilbage og samler din Sæd paa Loen?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 Mon Strudsens Vinge er lam, eller mangler den Dækfjer og Dun,
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 siden den betror sine Æg til Jorden og lader dem varmes i Sandet,
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 tænker ej paa, at en Fod kan knuse dem, Vildtet paa Marken træde dem sønder?
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 Haard ved Ungerne er den, som var de ej dens; spildt er dens Møje, det ængster den ikke.
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Thi Gud lod den glemme Visdom og gav den ej Del i Indsigt.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 Naar Skytterne kommer, farer den bort, den ler ad Hest og Rytter.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 Giver du Hesten Styrke, klæder dens Hals med Manke
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 og lærer den Græshoppens Spring? Dens stolte Prusten indgyder Rædsel.
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Den skraber muntert i Dalen, gaar Brynjen væligt i Møde;
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 den ler ad Rædselen, frygter ikke og viger ikke for Sværdet;
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 Koggeret klirrer over den, Spydet og Køllen blinker;
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 den sluger Vejen med gungrende Vildskab, den tøjler sig ikke, naar Hornet lyder;
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 et Stød i Hornet, straks siger den: Huj! Den vejrer Kamp i det fjerne, Kampskrig og Førernes Raab.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Skyldes det Indsigt hos dig, at Falken svinger sig op og breder sin Vinge mod Sønden?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Skyldes det Bud fra dig, at Ørnen flyver højt og bygger sin højtsatte Rede?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 Den bygger og bor paa Klipper, paa Klippens Tinde og Borg;
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 den spejder derfra efter Æde, viden om skuer dens Øjne.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Ungerne svælger i Blod; hvor Valen findes, der er den!
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”