< Job 27 >

1 Job vedblev at fremsætte sit Tankesprog:
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Saa sandt Gud lever, som satte min Ret til Side, den Almægtige, som gjorde mig mod i Hu:
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
3 Saa længe jeg drager Aande og har Guds Aande i Næsen,
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
4 skal mine Læber ej tale Uret, min Tunge ej fare med Svig!
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
5 Langt være det fra mig at give jer Ret; til jeg udaander, opgiver jeg ikke min Uskyld.
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
6 Jeg hævder min Ret, jeg slipper den ikke, ingen af mine Dage piner mit Sind.
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
7 Som den gudløse gaa det min Fjende, min Modstander som den lovløse!
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
8 Thi hvad er den vanhelliges Haab, naar Gud bortskærer og kræver hans Sjæl?
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
9 Hører mon Gud hans Skrig, naar Angst kommer over ham?
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
10 Mon han kan fryde sig over den Almægtige, føjer han ham, naar han paakalder ham?
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
11 Jeg vil lære jer om Guds Haand, den Almægtiges Tanker dølger jeg ikke;
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
12 se, selv har I alle set det, hvi har I saa tomme Tanker?
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
13 Det er den gudløses Lod fra Gud, Arven, som Voldsmænd faar fra den Almægtige:
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
14 Vokser hans Sønner, er det for Sværdet, hans Afkom mættes ikke med Brød;
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
15 de øvrige bringer Pesten i Graven, deres Enker kan ej holde Klage over dem.
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
16 Opdynger han Sølv som Støv og samler sig Klæder som Ler —
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
17 han samler, men den retfærdige klæder sig i dem, og Sølvet arver den skyldfri;
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
18 han bygger sit Hus som en Edderkops, som Hytten, en Vogter gør sig;
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
19 han lægger sig rig, men for sidste Gang, han slaar Øjnene op, og er det ej mer;
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
20 Rædsler naar ham som Vande, ved Nat river Stormen ham bort;
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
21 løftet af Østenstorm farer han bort, den fejer ham væk fra hans Sted.
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
22 Skaanselsløst skyder han paa ham, i Hast maa han fly fra hans Haand;
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
23 man klapper i Hænderne mod ham og piber ham bort fra hans Sted!
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”

< Job 27 >