< Job 19 >
1 Saa tog Job til Orde og svarede:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Hvor længe vil I krænke min Sjæl og slaa mig sønder med Ord?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 I haaner mig nu for tiende Gang, mishandler mig uden Skam.
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 Har jeg da virkelig fejlet, hænger der Fejl ved mig?
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 Eller gør I jer store imod mig og revser mig ved at smæde?
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 Saa vid da, at Gud har bøjet min Ret, omspændt mig med sit Net.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Se, jeg skriger: Vold! men faar ikke Svar, raaber om Hjælp, der er ingen Ret.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 Han spærred min Vej, jeg kom ikke frem, han hylled mine Stier i Mørke;
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 han klædte mig af for min Ære, berøved mit Hoved Kronen,
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 brød mig ned overalt, saa jeg maa bort, oprykked mit Haab som Træet;
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 hans Vrede blussede mod mig, han regner mig for sin Fjende;
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 samlede rykker hans Flokke frem og bryder sig Vej imod mig, de lejrer sig om mit Telt.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 Mine Brødre har fjernet sig fra mig, Venner er fremmede for mig,
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 mine nærmeste og Kendinge holder sig fra mig, de, der er i mit Hus, har glemt mig;
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 mine Piger regner mig for en fremmed, vildfremmed er jeg i deres Øjne;
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 ej svarer min Træl, naar jeg kalder, jeg maa trygle ham med min Mund;
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 ved min Aande væmmes min Hustru, mine egne Brødre er jeg en Stank;
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 selv Drenge agter mig ringe, naar jeg rejser mig, taler de mod mig;
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 Standsfæller væmmes til Hobe ved mig, de, jeg elskede, vender sig mod mig.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 Benene hænger fast ved min Hud, med Kødet i Tænderne slap jeg bort.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Naade, mine Venner, Naade, thi Guds Haand har rørt mig!
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Hvi forfølger og I mig som Gud og mættes ej af mit Kød?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 Ak, gid mine Ord blev skrevet op, blev tegnet op i en Bog,
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 med Griffel af Jern, med Bly indristet i Klippen for evigt!
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 Men jeg ved, at min Løser lever, over Støvet vil en Forsvarer staa frem.
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 Naar min sønderslidte Hud er borte, skal jeg ud fra mit Kød skue Gud,
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 hvem jeg skal se paa min Side; ham skal mine Øjne se, ingen fremmed! Mine Nyrer forgaar i mit Indre!
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 Naar I siger: »Hor vi skal forfølge ham, Sagens Rod vil vi udfinde hos ham!«
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 saa tag jer i Vare for Sværdet; thi Vrede rammer de lovløse, at I skal kende, der kommer en Dom!
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”