< Job 12 >
1 Saa tog Job til Orde og svarede:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Ja, sandelig, I er de rette, med eder dør Visdommen ud!
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 Ogsaa jeg har som I Forstand, staar ikke tilbage for eder, hvo kender vel ikke sligt?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 Til Latter for Venner er den, der raabte til Gud og fik Svar, den retfærdige er til Latter.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 I Ulykke falder de fromme, den sorgløse spotter Faren, hans Fod staar fast, mens Fristen varer.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 I Fred er Voldsmænds Telte, og trygge er de, der vækker Guds Vrede, den, der fører Gud i sin Haand.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 Spørg dog Kvæget, det skal lære dig, Himlens Fugle, de skal oplyse dig,
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 se til Jorden, den skal lære dig lad Havets Fisk fortælle dig det!
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Hvem blandt dem alle ved vel ikke, at HERRENS Haand har skabt det;
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 han holder alt levendes Sjæl i sin Haand, alt Menneskekødets Aand!
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Prøver ej Øret Ord, og smager ej Ganen Maden?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Er Alderdom eet med Visdom, Dagenes Række med Indsigt?
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 Hos ham er der Visdom og Vælde, hos ham er der Raad og Indsigt.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Hvad han river ned, det bygges ej op, den, han lukker inde, kommer ej ud;
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 han dæmmer for Vandet, og Tørke kommer, han slipper det løs, og det omvælter Jorden.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Hos ham er der Kraft og Fasthed; den, der farer og fører vild, er hans Værk.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Raadsherrer fører han nøgne bort, og Dommere gør han til Taaber;
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 han løser, hvad Konger bandt, og binder dem Reb om Lænd;
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Præster fører han nøgne bort og styrter ældgamle Slægter;
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 han røver de dygtige Mælet og tager de gamles Sans;
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 han udøser Haan over Fyrster og løser de stærkes Bælte;
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 han drager det skjulte frem af Mørket og bringer Mulmet for Lyset,
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 gør Folkene store og lægger dem øde, udvider Folkeslags Grænser og fører dem atter bort;
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 han tager Jordens Høvdingers Vid og lader dem rave i vejløst Øde;
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 de famler i Mørke uden Lys og raver omkring som drukne.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.