< Esajas 60 >

1 Gør dig rede, bliv Lys, thi dit Lys er kommet, HERRENS Herlighed er oprundet over dig.
“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
2 Thi se, Mørke skjuler Jorden og Dunkelhed Folkene, men over dig skal HERREN oprinde, over dig skal hans Herlighed ses.
Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
3 Til dit Lys skal Folkene vandre, og Konger til dit straalende Skær.
Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
4 Løft Øjnene, se dig om, de samles, kommer alle til dig. Dine Sønner kommer fra det fjerne, dine Døtre bæres paa Hofte;
“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
5 da straaler dit Øje af Glæde, dit Hjerte banker og svulmer; thi Havets Skatte bliver dine, til dig kommer Folkenes Rigdom;
Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
6 Kamelernes Vrimmel skjuler dig, Midjans og Efas Foler, de kommer alle fra Saba; Guld og Røgelse bærer de og kundgør HERRENS Pris;
Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
7 alt Kedars Smaakvæg samles til dig, dig tjener Nebajots Vædre, til mit Velbehag ofres de til mig, mit Bedehus herliggøres.
Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
8 Hvem flyver mon der som Skyer, som Duer til Dueslag?
“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
9 Det er Skibe, der kommer med Hast, i Spidsen er Tarsisskibe, for at bringe dine Sønner fra det fjerne; deres Sølv og Guld har de med til HERREN din Guds Navn, Israels Hellige, han gør dig herlig.
Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
10 Udlændinge skal bygge dine Mure, og tjene dig skal deres Konger; thi i Vrede slog jeg dig vel, men i Naade forbarmer Jeg mig over dig.
“Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
11 Dine Porte holdes altid aabne, de lukkes hverken Dag eller Nat, at Folkenes Rigdom kan bringes dig med deres Konger som Førere.
Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
12 Thi det Folk og Rige, som ikke tjener dig, skal gaa til Grunde, og Folkene skal lægges øde i Bund og Grund.
Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
13 Til dig skal Libanons Herlighed komme, baade Cypresser og Elm og Gran, for at smykke min Helligdoms Sted, saa jeg ærer mine Fødders Skammel.
“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
14 Dine Undertrykkeres Sønner kommer bøjet til dig, og alle, som haaned dig, kaster sig ned for din Fod og kalder dig HERRENS By, Israels Helliges Zion.
Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
15 Medens du før var forladt og hadet, saa ingen drog gennem dig, gør jeg dig til evig Højhed, til Glæde fra Slægt til Slægt.
“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
16 Du skal indsuge Folkenes Mælk og die Kongernes Bryst. Du skal kende, at jeg, HERREN, er din Frelser, din Genløser Jakobs Vældige.
Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
17 Guld sætter jeg i Stedet for Kobber og Sølv i Stedet for Jern, Kobber i Stedet for Træ og Jern i Stedet for Sten. Til din Øvrighed sætter jeg Fred, til Hersker over dig Retfærd.
Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
18 Der høres ej mer i dit Land om Uret, om Vold og Ufærd inden dine Grænser; du kalder Frelse dine Mure og Lovsang dine Porte.
Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
19 Ej mer skal Solen være dit Lys eller Maanen Skinne for dig: HERREN skal være dit Lys for evigt, din Gud skal være din Herlighed.
Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
20 Din Sol skal ej mer gaa ned, din Maane skal ej tage af; thi HERREN skal være dit Lys for evigt, dine Sørgedage har Ende.
Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
21 Enhver i dit Folk er retfærdig, evigt ejer de Landet, et Skud, som HERREN har plantet, hans Hænders Værk, til hans Ære.
Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
22 Den mindste bliver en Stamme, den ringeste et talrigt Folk. Jeg er HERREN; naar Tid er inde, vil jeg fremme det i Hast.
Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”

< Esajas 60 >