< Esajas 46 >

1 I Knæ er Bel, og Nebo er bøjet, deres Billeder gives til Dyr og Fæ, de læsses som Byrde paa trætte Dyr.
Beli wagwada pansi, Nebo wawerama; nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo. Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe. Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
2 De bøjes, i Knæ er de alle, de kan ikke frelse Byrden, og selv maa de vandre i Fangenskab.
Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo; sizikutha kupulumutsa katunduyo, izo zomwe zikupita ku ukapolo.
3 Hør mig, du Jakobs Hus, al Resten af Israels Hus, løftet fra Moders Liv, baaret fra Moders Skød.
Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo, inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli, Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu, ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
4 Til Alderdommen er jeg den samme, jeg bærer jer, til Haarene graaner; ret som jeg bar, vil jeg bære, jeg, jeg vil bære og redde.
Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi ndidzakusamalirani ndithu. Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani, ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
5 Med hvem vil I jævnstille, ligne mig, hvem vil I gøre til min Lige?
“Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani? Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
6 De øser Guld af Pung, Sølv faar de vejet paa Vægt, de lejer en Guldsmed, som gør det til en Gud, de bøjer sig, kaster sig ned;
Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo ndipo amayeza siliva pa masikelo; amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu, kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
7 de løfter den paa Skuldren og bærer den, sætter den paa Plads, og den staar, den rører sig ikke af Stedet; raaber de til den, svarer den ikke, den frelser dem ikke i Nød.
Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo; amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo. Singathe kusuntha pamalo pakepo. Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha; kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
8 Kom dette i Hu, lad jer raade, I frafaldne, læg jer det paa Sinde!
“Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi, Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
9 Kom i Hu, hvad er forudsagt før, thi Gud er jeg, ellers ingen, ja Gud, der er ingen som jeg,
Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana; chifukwa Ine ndine Mulungu ndipo palibe wina ofanana nane.
10 der forud forkyndte Enden, tilforn, hvad der ikke var sket, som sagde: »Mit Raad staar fast, jeg fuldbyrder al min Vilje, «
Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe. Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike. Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi. Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
11 som fra Øst kalder Ørnen hid, fra det fjerne mit Raads Fuldbyrder. Jeg taled og lader det ske, udtænkte og fuldbyrder det.
Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa. Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa. Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi; zimene ndafuna ndidzazichitadi.
12 Hør paa mig, I modløse, som tror, at Retten er fjern:
Ndimvereni, inu anthu owuma mtima, inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
13 Jeg bringer min Ret, den er ej fjern, min Frelse tøver ikke; jeg giver Frelse paa Zion, min Herlighed giver jeg Israel.
Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa; sichili kutali. Tsikulo layandikira ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.

< Esajas 46 >