< Esajas 45 >

1 Saa siger HERREN til sin Salvede, til Kyros, hvis højre jeg greb for at nedstyrte Folk for hans Ansigt og løsne Kongernes Gjord, for at aabne Dørene for ham, saa Portene ikke var stængt:
Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2 Selv gaar jeg frem foran dig, Hindringer jævner jeg ud; jeg sprænger Porte af Kobber og sønderhugger Slaaer af Jern.
Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3 Jeg giver dig Mulmets Skatte, Rigdomme gemt i Løn, saa du kender, at den, der kaldte dig ved Navn, er mig, er HERREN, Israels Gud.
Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4 For Jakobs, min Tjeners, Skyld, for min udvalgtes, Israels, Skyld kalder jeg dig ved dit Navn, ved et Æresnavn, skønt du ej kender mig.
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5 HERREN er jeg, ellers ingen, uden mig er der ingen Gud; jeg omgjorder dig, endskønt du ej kender mig,
Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
6 saa de kender fra Solens Opgang til dens Nedgang: der er ingen uden mig. HERREN er jeg, ellers ingen,
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
7 Lysets Ophav og Mørkets Skaber, Velfærds Kilde og Ulykkes Skaber. Jeg er HERREN, der virker alt.
Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8 Lad regne, I Himle deroppe, nedsend Retfærd, I Skyer, Jorden aabne sit Skød, saa Frelse maa spire frem og Retfærd vokse tillige. Jeg, HERREN, lader det ske.
“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9 Ve den, der trættes med sit Ophav, et Skaar kun blandt Skaar af Jord! Siger Ler til Pottemager: »Hvad kan du lave?« hans Værk: »Du har ikke Hænder!«
“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
10 Ve den, der siger til sin Fader: »Hvad kan du avle?« til sin Moder: »Hvad kan du føde?«
Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11 Saa siger HERREN, Israels Hellige, Fremtidens Ophav: I spørger mig om mine Børn, for mine Hænders Værk vil I raade!
“Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12 Det var mig, som dannede Jorden og skabte Mennesket paa den; mine Hænder udspændte Himlen, jeg opbød al dens Hær;
Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13 det var mig, som vakte ham i Retfærd, jeg jævner alle hans Veje; han skal bygge min By og give mine bortførte fri — ikke for Løn eller Gave, siger Hærskarers HERRE.
Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14 Saa siger HERREN: Ægyptens Løn, Ætiopiens Vinding, Sebæernes granvoksne Mænd, de skal komme og tilhøre dig, og dig skal de følge; de skal komme i Lænker og kaste sig ned for dig og bønfalde dig: »Kun hos dig er Gud, der er ingen anden Gud.«
Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
15 Sandelig, du er en Gud, som er skjult, Israels Gud er en Frelser!
Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16 Skam og Skændsel bliver alle hans Fjender til Del, til Hobe gaar Gudemagerne om med Skændsel.
Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
17 Israel frelses ved HERREN, en evig Frelse, i Evighed bliver I ikke til Skam og Skændsel.
Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
18 Thi saa siger HERREN, Himlens Skaber, han, som er Gud, som dannede Jorden, frembragte, grundfæsted den, ej skabte den øde, men danned den til at bebos: HERREN er jeg, ellers ingen.
Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
19 Jeg talede ikke i Løndom, i Mørkets Land, sagde ikke til Jakobs Æt: »Søg mig forgæves!« Jeg, HERREN, taler hvad ret er, forkynder, hvad sandt er.
Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
20 Kom samlede hid, træd frem til Hobe, I Folkenes undslupne! Uvidende er de, som bærer et Billede af Træ, de, som beder til en Gud, der ikke kan frelse.
Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21 Forkynd det, kom frem dermed, lad dem raadslaa sammen: Hvo kundgjorde dette tilforn, forkyndte det forud? Mon ikke jeg, som er HERREN? Uden mig er der ingen Gud, uden mig er der ingen retfærdig, frelsende Gud.
Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
22 Vend dig til mig og bliv frelst, du vide Jord, thi Gud er jeg, ellers ingen;
“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23 jeg svor ved mig selv, fra min Mund kom Sandhed, mit Ord vender ikke tilbage: Hvert Knæ skal bøjes for mig, hver Tunge sværge mig til.
Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24 »Kun hos HERREN, « skal man sige, »er Retfærd og Styrke; til ham skal alle hans Avindsmænd komme med Skam.«
Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25 Ved HERREN naar al Israels Æt til sin Ret og jubler.
Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.

< Esajas 45 >