< Esajas 4 >

1 Syv Kvinder skal paa hin Dag gribe fat i een Mand og sige: »Vi vil æde vort eget Brød og holde os selv med Klæder, blot vi maa bære dit Navn. Tag Vanæren fra os!«
Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi, nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu, ndi kuvala zovala zathu; inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu. Tichotseni manyazi aumbeta!”
2 Paa hin Dag Bliver HERRENS Spire til Fryd og Ære og Landets Frugt til Stolthed og Smykke for de undslupne i Israel.
Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli.
3 Den, som er levnet i Zion og blevet tilovers i Jerusalem, skal kaldes hellig, enhver, der er indskrevet til Livet i Jerusalem,
Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu.
4 naar Herren faar aftvættet Zions Døtres Smuds og bortskyllet Jerusalems Blodskyld fra dets Midte med Doms og Udrensnings Aand.
Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto.
5 Da skaber Herren over hvert et Sted paa Zions Bjerg og over dets Festforsamlinger en Sky om Dagen og Røg med luende Ildskær om Natten; thi over alt, hvad herligt er, skal der være et Dække
Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova.
6 og Ly til Skygge mod Hede og til Skærm og Skjul mod Skybrud og Regn.
Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.

< Esajas 4 >