< Esajas 3 >

1 Thi se, Herren, Hærskarers HERRE, fratager Jerusalem og Juda støtte og Stav, hver Støtte af Brød og hver støtte af vand:
Taonani tsopano, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda zinthu pamodzi ndi thandizo; adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
2 Helt og Krigsmand, Dommer og Profet, Spaamand og Ældste,
anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo, oweruza ndi aneneri, anthu olosera ndi akuluakulu,
3 Halvhundredfører og Stormand, Raadsherre og Haandværksmester og den, der er kyndig i Trolddom.
atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka, aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.
4 Jeg giver dem Drenge til Øverster, Drengekaadhed skal herske over dem.
Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo; ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
5 I Folket undertrykker den ene den anden, hver sin Næste; Dreng sætter sig op imod Olding, Usling mod Hædersmand.
Anthu adzazunzana, munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake. Anthu wamba adzanyoza akuluakulu.
6 Naar da en Mand tager fat paa en anden i hans Fædrenehus og siger: »Du har en Kappe, du skal være vor Hersker, under dig skal dette faldefærdige Rige staa!«
Munthu adzagwira mʼbale wake mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati, “Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu; lamulira malo opasuka ano!”
7 saa svarer han paa hin Dag: »Jeg vil ikke være Saarlæge! Jeg har hverken Brød eller Klæder i Huset, gør ikke mig til Folkets Overhoved!«
Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti, “Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake. Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga; musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”
8 Thi Jerusalem snubler, og Juda falder, fordi de med Tunge og Gerning er mod HERREN i Trods mod hans Herligheds Øjne.
Yerusalemu akudzandira, Yuda akugwa; zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova, sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
9 Deres Ansigtsudtryk vidner imod dem; de kundgør deres Synd som Sodoma, dølger intet. Ve deres Sjæl, de styrted sig selv i Vaade.
Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa; amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu; salibisa tchimo lawolo. Tsoka kwa iwo odziputira okha mavuto.
10 Salige de retfærdige, dem gaar det godt, deres Gerningers Frugt skal de nyde;
Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino, pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
11 ve den gudløse, ham gaar det ilde; han faar, som hans Hænder har gjort.
Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo! Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.
12 Mit Folk har en Dreng ved Styret, og over det hersker Kvinder. Dine Ledere, mit Folk, leder vild, gør Vejen, du vandrer, vildsom.
Achinyamata akupondereza anthu anga, ndipo amene akuwalamulira ndi akazi. Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani; akukuchotsani pa njira yanu.
13 Til Rettergang er HERREN traadt frem, han staar og vil dømme sit Folk.
Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu; wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
14 HERREN møder til Doms med de Ældste i sit Folk og dets Fyrster: »Det er jer, som gnaved Vingaarden af, I har Rov fra den arme til Huse.
Yehova akuwazenga milandu akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake: “Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa; nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
15 Hvor kan I træde paa mit Folk og male de arme sønder?« saa lyder det fra Herren, Hærskarers HERRE.
Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga, nʼkudyera masuku pamutu amphawi?” Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
16 HERREN siger: Eftersom Zions Døtre bryster sig og gaar med knejsende Nakke og kælne Blikke, gaar med trippende Gang og med raslende Ankelkæder —
Yehova akunena kuti, “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri, akuyenda atakweza makosi awo, akukopa amuna ndi maso awo akuyenda monyangʼama akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
17 gør Herren Issen skaldet paa Zions Døtre og blotter deres Tindingers Lokker.
Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo; Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”
18 Paa hin Dag afriver Herren al deres Pynt: Ankelringe, Pandebaand, Halvmaaner,
Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi,
19 Perler, Armbaand, Flor,
ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope,
20 Hovedsmykker, Ankelkæder, Bælter, Lugtedaaser, Trylleringe,
maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa,
21 Fingerringe, Næseringe,
mphete ndi zipini,
22 Festklæder, Underdragter, Sjaler, Tasker,
zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama,
23 Spejle, Lin, Hovedbaand og Slør.
magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.
24 For Vellugt kommer der Stank, i Stedet for Bælte Reb, for Fletninger skaldet Isse, for Stadsklæder Sæk om Hofte, for Skønhedsmærke Brændemærke.
Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha, mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe; mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi; mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli; mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
25 Dine Mænd skal falde for Sværd, dit unge Mandskab i Strid.
Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga, asilikali ako adzafera ku nkhondo.
26 Hendes Porte skal sukke og klage og hun sidde ensom paa Jorden.
Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira; Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.

< Esajas 3 >