< Hoseas 3 >

1 Og HERREN sagde til mig: »Gaa atter hen og elsk en Kvinde, som har Elskere og boler, ligesom HERREN elsker Israeliterne, endskønt de vender sig til fremmede Guder og elsker Rosinkager.«
Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
2 Saa købte jeg mig hende for femten Sekel Sølv og en Homer og en Letek Byg.
Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
3 Og jeg sagde til hende: »I lang Tid skal du vente paa mig; du maa ikke bedrive Hor eller tilhøre nogen Mand; heller ikke jeg vil komme til dig.«
Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
4 Thi i lang Tid skal Israeliterne vente uden Konge og Fyrste, uden Slagtoffer og Stenstøtte, uden Efod og Husgud.
Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
5 Siden skal Israeliterne omvende sig og søge HERREN deres Gud og David, deres Konge, og bævende komme til HERREN og hans Velsignelse i de sidste Dage.
Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.

< Hoseas 3 >