< Hoseas 2 >
1 Kald eders Broder Mit-Folk og eders Søster Naaderig.
“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
2 Gaa i rette med eders Moder, gaa i rette, thi hun er ikke min Hustru, og jeg er ej hendes Mand. For Hormærket fri hun sit Ansigt, for Bolemærket sit Bryst.
“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
3 Jeg klæder hende ellers nøgen, stiller hende frem, som hun fødtes; jeg reder hende til som en Ørk, som et Tørkeland gør jeg hende, lader hende tørste ihjel.
Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
4 Jeg ynkes ej over hendes Børn, fordi de er Horebørn;
Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
5 thi Horkvinde var deres Moder, skamløs var hun, som bar dem. Thi hun sagde: »Mine Elskere holder jeg mig til, som giver mig mit Brød og mit Vand, min Uld og min Hør, min Olie og Vin.«
Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
6 Se, derfor spærrer jeg med Tjørn hendes Vej, foran hende murer jeg en Mur, saa hun ikke kan finde sine Stier.
Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
7 Efter Elskerne kan hun saa løbe, hun naar dem alligevel ikke; hun søger dem uden at finde, og da skal hun sige: »Jeg gaar paa ny til min første Mand; da havde jeg det bedre end nu.«
Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
8 Ja hun, hun skønner ikke, at det var mig, som gav hende Korn og Most og Olie, gav hende rigeligt Sølv og Guld, som de gjorde til Ba'aler.
Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
9 Derfor tager jeg atter mit Korn, naar Tiden er til det, min Most, naar Timen er inde, borttager min Uld og min Hør, som hun skjuler sin Nøgenhed med.
“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
10 Jeg blotter nu hendes Skam lige for Elskernes Øjne, af min Haand frier ingen hende ud.
Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
11 Jeg gør Ende paa al hendes Glæde, Fester, Nymaaner, Sabbater, hver en Højtid, hun har.
Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
12 Jeg ødelægger hendes Vinstok og Figentræ, om hvilke hun sagde: »Her er min Skøgeløn, den, mine Elskere gav mig.« Jeg skaber dem om til Krat, af Markens Dyr skal de ædes.
Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
13 Jeg hjemsøger hende for Ba'alernes Fester, paa hvilke hun bragte dem Ofre, smykket med Ring og Kæde. Sine Elskere holdt hun sig til, mig glemte hun, lyder det fra HERREN.
Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
14 Se, derfor vil jeg lokke og føre hende ud i Ørkenen og tale hende kærligt til.
“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
15 Saa giver jeg hende hendes Vingaarde der og Akors Dal til en Haabets Dør. Der skal hun synge som i Ungdommens Dage, som da hun drog op fra Ægyptens Land.
Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
16 Paa hin Dag, lyder det fra HERREN, skal hun paakalde sin Ægtemand, og ikke mere Ba'alerne.
“Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
17 Ba'alsnavnene fjerner jeg fra hendes Mund, ej mer skal Navnene huskes.
Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
18 Paa hin Dag slutter jeg en Pagt for dem med Markens Dyr og Himmelens Fugle og Jordens Kryb; Bue, Sværd og Stridsvaaben sønderbryder jeg i Landet, og jeg lader dem bo trygt.
Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
19 Jeg trolover mig med dig for evigt, jeg trolover mig med dig med Retfærd og Ret, med Miskundhed og Barmhjertighed;
Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
20 jeg trolover mig med dig i Troskab, og du skal kende HERREN.
Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
21 Da skal det ske paa hin Dag, at jeg bønhører, lyder det fra HERREN, ja, at jeg bønhører Himlen, at den saa bønhører Jorden,
“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
22 og Jorden bønhører Kornet, Mosten og Olien, og de bønhører Jizre'el.
ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
23 Jeg saar hende ud i Landet, mod Naadeløs er jeg naadig og siger til Ikke-mit-Folk: »Mit Folk er du!« og han skal sige: »Min Gud!«
Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”