< Hoseas 10 >

1 En frodig Vinstok var Israel, som bar sin Frugt, jo flere Frugter, des flere Altre; som Landet gik frem, des skønnere Støtter.
Israeli anali mpesa wotambalala; anabereka zipatso zambiri. Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka, anawonjezera kumanga maguwa ansembe. Pamene dziko lake linkatukuka, anakongoletsa miyala yake yopatulika.
2 Deres Hjerte var glat, saa lad dem da bøde! Han skal slaa Altrene ned, lægge Støtterne øde.
Mtima wawo ndi wonyenga ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Yehova adzagumula maguwa awo ansembe ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.
3 De siger jo nu: »Vi har ingen Konge; thi HERREN frygter vi ej; en Konge, hvad gavner han os?«
Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu chifukwa sitinaope Yehova. Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu, kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”
4 Med Ord slaar de om sig, gør Mened og indgaar Forbund, saa Ret bliver Gifturt, der gror langs Markens Furer.
Mafumu amalonjeza zambiri, amalumbira zabodza pochita mapangano. Kotero maweruzo amaphuka ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.
5 For Bet-Avens Kalv skal Samarias Borgere ængstes, ja, over den skal dens Folk og dens Præster sørge, jamre over deres Skat, thi den bortføres fra dem;
Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni. Anthu ake adzalirira fanolo, chimodzimodzinso ansembe ake adamawo, amene anakondwera ndi kukongola kwake, chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.
6 som Gave til Storkongen føres og den til Assur. Efraim høster kun Skændsel, Israel Skam af sin Afgud.
Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya ngati mphatso kwa mfumu yayikulu. Efereimu adzachititsidwa manyazi chifukwa cha mafano ake amitengo.
7 Samarias Konge slettes som Skum paa Vandets Flade.
Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali ngati kanthambi koyenda pa madzi.
8 Øde er Afgudshøjene, Israels Synd, og paa deres Altre skal Torn og Tidsel gro. De siger til Bjergene: »Skjul os!« til Højene: »Fald ned over os!«
Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa. Ili ndiye tchimo la Israeli. Minga ndi mitungwi zidzamera ndi kuphimba maguwa awo ansembe. Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!” ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”
9 Du syndede, Israel, helt fra Gibeas Dage. Der i Gibea sagde man: »Krig skal ej naa os!« Men jeg kom over de Niddinger, revsede dem;
“Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya, ndipo wakhala uli pomwepo. Kodi nkhondo sinagonjetse anthu ochita zoyipa ku Gibeya?
10 Stammerne samled sig mod dem til Tugt for tvefold Brøde.
Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo; mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo, kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.
11 En tilvænnet Kvie var Efraim, tærskede villigt, Aaget lagde jeg selv paa dens skønne Hals; for Ploven spændte jeg Efraim, Juda for Harven.
Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa amene amakonda kupuntha tirigu, choncho Ine ndidzayika goli mʼkhosi lake lokongolalo. Ndidzasenzetsa Efereimu goli, Yuda ayenera kulima, ndipo Yakobo ayenera kutipula.
12 Saa eders Sæd i Retfærd, høst i Fromhed; bryd eder Kundskabs Nyjord og søg saa HERREN, til Retfærds Frugt bliver eder til Del.
Mufese nokha chilungamo ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika. Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo; pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova, mpaka Iye atabwera kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.
13 I pløjede Gudløshed, høstede Uret, fortærede Løgnens Frugt. Fordi du slaar Lid til dine Vogne og mange Helte,
Koma inu munadzala zolakwa, mwakolola zoyipa; mwadya chipatso cha chinyengo. Chifukwa mumadalira mphamvu zanu ndiponso ankhondo anu ochulukawo,
14 skal Kampgny staa i dine Byer og alle dine Borge. De skal ødelægges, som da Sjalman ødelagde Bet-Arbel paa Stridens Dag. Moder skal knuses hos Børn.
phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka, monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo; pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.
15 Det voldte Betel eder. For din Ondskabs Skyld skal Israels Konge ved Morgengry gøres til intet.
Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu. Tsiku limeneli likadzafika, mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.

< Hoseas 10 >