< 1 Mosebog 8 >

1 Da ihukom Gud Noa og alle de vilde Dyr og Kvæget, som var hos ham i Arken; og Gud lod en Storm fare hen over Jorden, saa at Vandet begyndte at falde;
Tsono Mulungu anakumbukira Nowa ndi nyama zonse zakuthengo ndi ziweto zimene anali nazo mu chombo. Yehova anatumiza mphepo pa dziko lapansi ndipo madzi anaphwera.
2 Verdensdybets Kilder og Himmelens Sluser lukkedes, Regnen fra Himmelen standsede,
Tsono akasupe a madzi ambiri a pansi pa dziko ndi zitseko za madzi a kumwamba zinatsekedwa, ndipo mvula inaleka kugwa.
3 og Vandet veg lidt efter lidt bort fra Jorden, og Vandet tog af efter de 150 Dages Forløb.
Madzi amaphwabe pa dziko lapansi. Pakutha pa masiku 150, madzi anatsika,
4 Paa den syttende Dag i den syvende Maaned sad Arken fast paa Ararats Bjerge,
ndipo pa tsiku la 17 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, chombo chija chinakakhazikika pa mapiri a Ararati.
5 og Vandet vedblev at synke indtil den tiende Maaned, og paa den første Dag i denne Maaned dukkede Bjergenes Toppe frem.
Madzi anapitirira kuphwa mpaka mwezi wa khumi, ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wa khumiwo msonga za mapiri zinayamba kuonekera.
6 Da der var gaaet fyrretyve Dage: aabnede Noa den Luge, han havde lavet paa Arken,
Patapita masiku makumi anayi, Nowa anatsekula zenera limene anapanga mʼchombomo
7 og sendte en Ravn ud; den fløj frem og tilbage, indtil Vandet var tørret bort fra Jorden.
natulutsa khwangwala, koma khwangwalayo ankangowuluka uku ndi uku mpaka madzi anawuma pa dziko lapansi.
8 Da sendte han en Due ud for at se, om Vandet var sunket fra Jordens Overflade;
Kenaka anatulutsa nkhunda kuti aone ngati madzi aphwa pa dziko.
9 men Duen fandt intet Sted at sætte sin Fod og vendte tilbage til ham i Arken, fordi der endnu var Vand over hele Jorden; og han rakte Haanden ud og tog den ind i Arken til sig.
Koma nkhunda sinapeze poti nʼkutera chifukwa panali madzi ponseponse pa dziko lapansi. Choncho inabwerera kwa Nowa mʼchombo. Nowa anatulutsa dzanja lake kunja ndi kutenga nkhundayo kuyibwezera mʼchombo mmene iye anali.
10 Derpaa biede han yderligere syv Dage og sendte saa atter Duen ud fra Arken;
Choncho anadikirabe masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatulutsanso nkhundayo mʼchombo muja.
11 ved Aftenstid kom Duen tilbage til ham, og se, den havde et friskt Olieblad i Næbbet. Da skønnede Noa, at Vandet var svundet bort fra Jorden.
Pamene nkhunda inabwerera madzulo ake, inali itanyamula tsamba laliwisi la mtengo wa olivi. Motero Nowa anadziwa kuti madzi aphwadi pa dziko lapansi.
12 Derpaa biede han syv Dage til, og da han saa sendte Duen ud, kom den ikke mere tilbage til ham.
Iye anadikira masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatumizanso nkhunda ija, koma nthawi imeneyi sinabwererenso kwa iye.
13 I Noas 601ste Leveaar paa den første Dag i den første Maaned var Vandet tørret bort fra Jorden. Da tog Noa Dækket af Arken, og da han saa sig om, se, da var Jordens Overflade tør.
Pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba wa chaka chimene Nowa anakwanitsa zaka 601, madzi anawuma pa dziko lapansi. Ndipo Nowa anachotsa denga la chombo ndipo anaona kuti kunja kwawuma.
14 Paa den syv og tyvende Dag i den anden Maaned var Jorden tør.
Pokwana tsiku la 27 la mwezi wachiwiri dziko lapansi linawumiratu.
15 Da sagde Gud til Noa:
Tsono Mulungu anawuza Nowa kuti,
16 »Gaa ud af Arken med din Hustru, dine Sønner og dine Sønnekoner
“Iwe, mkazi wako, ana ako pamodzi ndi akazi awo tulukani mʼchombomo.
17 og for alle Dyr, der er hos dig, alt Kød, Fugle, Kvæg og alt Kryb, der kryber paa Jorden, ud med dig, at de kan vrimle paa Jorden og blive frugtbare og mangfoldige paa Jorden!«
Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwe, mbalame, nyama ndi zokwawa zonse kuti ziswane ndi kuchulukana pa dziko lapansi.”
18 Da gik Noa ud med sine Sønner, sin Hustru og sine Sønnekoner;
Nowa anatuluka pamodzi ndi ana ake aamuna, mkazi wake ndi akazi a ana ake.
19 og alle de vildtlevende Dyr, alt Kvæget, alle Fuglene og alt Krybet, der kryber paa Jorden, efter deres Slægter, gik ud af Arken.
Nyama zonse, zokwawa zonse, mbalame zonse, chilichonse choyenda pa dziko lapansi, zinatuluka mʼchombo motsogozana monga mwa mitundu yawo.
20 Derpaa byggede Noa HERREN et Alter og tog nogle af alle de rene Dyr og Fugle og ofrede Brændofre paa Alteret.
Pamenepo Nowa anamanga guwa lansembe la Yehova ndipo anatengako mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya ndi mbalame zoti nʼkudya naperekapo nsembe yopsereza.
21 Og da HERREN indaandede den liflige Duft, sagde han til sig selv: »Jeg vil aldrig mere forbande Jorden for Menneskenes Skyld, thi Menneskehjertets Higen er ond fra Ungdommen af, og jeg vil aldrig mere tilintetgøre alt, hvad der lever, saaledes som jeg nu har gjort!
Yehova atamva fungo labwino anati mu mtima mwake: “Sindidzatembereranso nthaka chifukwa cha munthu, ngakhale kuti maganizo a mu mtima mwake ndi oyipa kuyambira ubwana wake. Ndipo sindidzawononganso zolengedwa zonse zamoyo monga ndachitiramu.
22 Herefter skal, saa længe Jorden staar, Sæd og Høst, Kulde og Hede, Sommer og Vinter, Dag og Nat ikke ophøre!«
“Nthawi zonse mmene dziko lapansi lidzakhalire, nthawi yodzala ndi nthawi yokolola yozizira ndi yotentha, dzinja ndi chilimwe, usana ndi usiku, sizidzatha.”

< 1 Mosebog 8 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark