< 1 Mosebog 7 >
1 Derpaa sagde HERREN til Noa: »Gaa ind i Arken med hele dit Hus, thi dig har jeg fundet retfærdig for mine Øjne i denne Slægt.
Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu.
2 Af alle rene Dyr skal du tage syv Par, Han og Hun, og af alle urene Dyr eet Par, Han og Hun,
Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso.
3 ligeledes af Himmelens Fugle syv Par, Han og Hun, for at de kan forplante sig paa hele Jorden.
Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi.
4 Thi om syv Dage vil jeg lade det regne paa Jorden i fyrretyve Dage og fyrretyve Nætter og udslette alle Væsener, som jeg har gjort, fra Jordens Flade.«
Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”
5 Og Noa gjorde ganske som HERREN havde paalagt ham.
Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.
6 Noa var 600 Aar gammel, da Vandfloden kom over Jorden.
Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600.
7 Noa gik med sine Sønner, sin Hustru og sine Sønnekoner ind i Arken for at undslippe Flodens Vande.
Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula.
8 De rene og de urene Dyr, Fuglene og alt, hvad der kryber paa Jorden,
Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo.
9 gik Par for Par ind i Arken til Noa, Han og Hundyr, som Gud havde paalagt Noa.
Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu.
10 Da nu syv Dage var omme, kom Flodens Vande over Jorden;
Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.
11 i Noas 600de Leveaar paa den syttende Dag i den anden Maaned, den Dag brast det store Verdensdybs Kilder, og Himmelens Sluser aabnedes,
Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka.
12 og Regnen faldt over Jorden i fyrretyve Dage og fyrretyve Nætter.
Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.
13 Selv samme Dag gik Noa ind i Arken og med ham hans Sønner Sem, Kam og Jafet, hans Hustru og hans tre Sønnekoner
Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo.
14 og desuden alle vildtlevende Dyr efter deres Arter, alt Kvæg efter dets Arter, alt Kryb paa Jorden efter dets Arter og alle Fugle efter deres Arter, alle Fugle, alt, hvad der har Vinger;
Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake.
15 af alt Kød, som har Livsaande, gik Par for Par ind i Arken til Noa;
Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse.
16 Han og Hundyr af alt Kød gik ind, som Gud havde paabudt, og HERREN lukkede efter ham.
Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.
17 Da kom Vandfloden over Jorden i fyrretyve Dage, og Vandet steg og løftede Arken, saa den hævedes over Jorden.
Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko.
18 Og Vandet steg og stod højt over Jorden, og Arken flød paa Vandet;
Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo.
19 og Vandet steg og steg over Jorden, saa de højeste Bjerge under Himmelen stod under Vand;
Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa.
20 femten Alen stod Vandet over dem, saa Bjergene stod helt under Vand.
Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri.
21 Da omkom alt Kød, som rørte sig paa Jorden, Fugle, Kvæg, vildtlevende Dyr og alt Kryb paa Jorden og alle Mennesker;
Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu.
22 alt, i hvis Næse det var Livets Aande, alt, hvad der var paa det faste Land, døde.
Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa.
23 Saaledes udslettedes alle Væsener, der var paa Jordens Flade, Mennesker, Kvæg, Kryb og Himmelens Fugle; de udslettedes af Jorden, og tilbage blev kun Noa og de, der var hos ham i Arken.
Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.
24 Vandet steg over Jorden i 150 Dage.
Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.