< 1 Mosebog 44 >

1 Derefter befalede han sin Hushovmester: »Fyld Mændenes Sække med Korn, saa meget de kan have med sig, og læg hvers Pengesum oven i hans Sæk
Pambuyo pake Yosefe analamulira wantchito wa mʼnyumba mwake kuti, “Adzazire chakudya anthuwa mʼmatumba mwawo monga mmene anganyamulire, ndipo uwayikire ndalama zawo pakamwa pa matumba awowo.
2 og læg mit eget Sølvbæger oven i den yngstes Sæk sammen med Pengene for hans Korn!« Og han gjorde, som Josef bød.
Tsono uyike chikho changa cha siliva chija, pakamwa pa thumba la wamngʼono kwambiriyu pamodzi ndi ndalama zake za chakudya” Ndipo iye anachita monga Yosefe ananenera.
3 Da Morgenen gryede, fik Mændene Lov at drage bort med deres Æsler.
Mmawa kutacha anthu aja analoledwa kuti apite ndi abulu awo.
4 Men før de var kommet ret langt fra Byen, bød Josef sin Hushovmester: »Sæt efter Mændene, og naar du indhenter dem, sig saa til dem: Hvorfor har I gengældt godt med ondt?
Atangotuluka mu mzinda muja, koma asanapite patali, Yosefe anati kwa wantchito wake, “Nyamuka atsatire anthu aja msanga. Ndipo ukawapeza, uwafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoyipa ndi zabwino?
5 Hvorfor har I stjaalet mit Sølvbæger? Det er jo min Herres Mundbæger, som han bruger til at tage Varsler af! Ilde har I handlet ved at gøre saaledes!«
Mwaberanji chikho chimene mbuye wanga amamweramo ndi kugwiritsa ntchito akafuna kuwombeza? Chimene mwachitachi ndi chinthu choyipa.’”
6 Og da han havde indhentet dem, sagde han det til dem.
Wantchito uja atawapeza ananena mawu anawuzidwa aja.
7 Men de svarede: »Hvor kan min Herre tale saaledes? Det være langt fra dine Trælle at gøre sligt!
Koma iwo anati kwa iye, “Kodi mbuye wanga mukuneneranji zimenezi? Sizingatheke ndi pangʼono pomwe kuti antchito anufe nʼkuchita zoterozo ayi!
8 Se, de Penge, vi fandt oven i vore Sække, bragte vi tilbage til dig fra Kana'ans Land — hvorfor skulde vi da stjæle Guld eller Sølv fra din Herres Hus!
Paja ife pobwera kuchokera ku Kanaani tinatenga ndalama kubwezera zimene tinazipeza mʼmatumba mwathu. Ndiye pali chifukwa chanji kuti tikabe siliva kapena golide mʼnyumba mwa mbuye wanu?
9 Den af dine Trælle, det findes hos, skal dø, og desuden vil vi andre være din Herres Trælle!«
Ngati wantchito wanu wina pano atapezeka nacho chikhocho, ameneyo aphedwe ndipo ena tonsefe tidzakhala akapolo anu, mbuye wathu.”
10 Han svarede: »Vel, lad det blive, som I siger: Den, Bægeret findes hos, skal være min Træl, men I andre skal være sagesløse!«
Iye anati, “Chabwino, tsono zikhale monga mwaneneramu. Komatu aliyense amene angapezeke nacho chikhocho adzakhala kapolo wanga, ndipo ena nonsenu muzipita mwaufulu.”
11 Saa skyndte de sig at løfte hver sin Sæk ned paa Jorden og aabne den,
Tsono onse anafulumira kutsitsa pansi aliyense thumba lake ndi kulitsekula.
12 og han undersøgte dem fra den ældstes til den yngstes, og Bægeret blev fundet i Benjamins Sæk.
Kenaka anayamba kufufuza, kuyambira pa wamkulu mpaka pa wamngʼono. Ndipo chikhocho chinapezeka mʼthumba mwa Benjamini.
13 Da sønderrev de deres Klæder, og efter at have læsset Sækkene hver paa sit Æsel vendte de tilbage til Byen.
Apo onse anangʼamba zovala zawo ndi chisoni. Ndipo anasenzetsa abulu katundu wawo nabwerera ku mzinda konkuja.
14 Da Juda og hans Brødre kom ind i Josefs Hus, hvor han endnu var, kastede de sig til Jorden for ham;
Pamene Yuda ndi abale ake ankafika ku nyumba kwa Yosefe nʼkuti Yosefe akanali komweko. Ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pake.
15 men Josef sagde til dem: »Hvad har I gjort! Ved I ikke, at en Mand som jeg forstaar sig paa hemmelige Kunster?«
Yosefe anafunsa kuti, “Nʼchiyani mwachitachi? Kodi simudziwa kuti munthu ngati ine ndikhoza kuona zinthu mwakuwombeza?”
16 Da sagde Juda: »Hvad skal vi svare min Herre, hvad skal vi sige, og hvorledes skal vi retfærdiggøre os? Gud har fundet dine Trælles Brøde! Se, vi er min Herres Trælle, baade vi andre og han, Bægeret fandtes hos!«
Yuda anayankha, “Kodi tinganenenji kwa mbuye wanga? Tinena chiyani? Tingadzilungamitse bwanji? Mulungu waulula kulakwa kwa antchito anu. Ndipo tsopano ndife akapolo a mbuye wanga, ife tonse pamodzi ndi amene wapezeka ndi chikhocho.”
17 Men han svarede: »Det være langt fra mig at handle saaledes; den, Bægeret fandtes hos, skal være min Træl, men I andre kan i Fred drage hjem til eders Fader.«
Koma Yosefe anati, “Sindingachite choncho ayi! Yekhayo amene wapezeka ndi chikhocho ndi amene akhale kapolo wanga. Ena nonsenu, bwererani kwa abambo anu mu mtendere.”
18 Da traadte Juda hen til ham og sagde: »Hør mig, min Herre, lad din Træl tale et Ord for min Herres Øren og lad ikke Vreden blusse op i dig mod din Træl, thi du er jo som Farao!
Ndipo Yuda anamuyandikira iye nati, “Chonde mbuye wanga mulole kapolo wanune ndinene mawu pangʼono kwa mbuye wanga. Musandipsere mtima, kapolo wanune, popeza inu muli ngati Farao yemwe.
19 Min Herre spurgte sine Trælle Har I Fader eller Broder?
Mbuye wanga munafunsa akapolo anufe kuti, ‘Kodi muli ndi abambo anu kapena mʼbale wanu?’
20 Og vi svarede min Herre: Ja, vi har en gammel Fader, og der er en Dreng, som blev født i hans Alderdom; en Broder til ham er død, og selv er han den eneste, hans Moder efterlod sig, og hans Fader elsker ham.
Ndipo ife tinayankha, ‘Inde mbuye wathu, ife tili ndi abambo athu wokalamba, ndipo pali mwana wamwamuna wamngʼono amene anabadwa abambo athu atakalamba kale. Mʼbale wake anafa ndipo ndi yekhayo mʼmimba mwa amayi ake amene watsala ndipo abambo ake amamukonda.’
21 Saa sagde du til dine Trælle: Bring ham med herned til mig, at jeg kan se ham med egne Øjne!
“Ndipo inu munatiwuza kuti, ‘Mubwere naye kwa ine kuti ndidzamuone ndekha.’
22 Men vi svarede min Herre: Drengen kan ikke forlade sin Fader, thi hans Fader dør, hvis han forlader ham!
Ife tinati, ‘Mbuye wathu, mnyamatayo sangasiye abambo ake, akawasiya ndiye kuti abambo akewo adzafa.’
23 Saa sagde du til dine Trælle: Kommer eders yngste Broder ikke med herned, saa bliver I ikke mere stedt for mit Aasyn!
Koma inu munatichenjeza kuti, ‘Pokhapokha mutabwera naye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri, simudzandionanso.’
24 Vi rejste saa op til din Træl, min Fader, og fortalte ham, hvad min Herre havde sagt.
Ndiye pamene tinafika kwa kapolo wanu, abambo athu tinawawuza zonse zimene munanena.
25 Da vor Fader siden sagde: Rejs atter hen og køb os lidt Føde!
“Abambo athu anatiwuza kuti, ‘Pitaninso mukagule kachakudya pangʼono.’
26 svarede vi: Vi kan ikke rejse derned, hvis ikke vor yngste Broder følger med, thi vi bliver ikke stedt for Mandens Aasyn, medmindre vor yngste Broder er med!
Koma tinati, ‘Sitingathe kupitanso. Sitingapite pokhapokha mngʼono wathuyu apite nafe chifukwa munthu uja anati sitingaonane naye ngati mngʼono wathuyu sakhala nafe.’
27 Saa sagde din Træl, min Fader, til os: I ved jo, at min Hustru fødte mig to Sønner;
“Koma kapolo wanu, abambo athu anatiwuza kuti, ‘Inu mukudziwa kuti mkazi wanga anandiberekera ana aamuna awiri.
28 den ene gik bort fra mig, og jeg sagde: Han er sikkerlig revet ihjel! Og jeg har ikke set ham siden;
Mmodzi wa iwo anandisiya. Ine ndimati anadyedwa ndi chirombo popeza sindinamuonenso mpaka lero.
29 hvis I nu ogsaa tager denne fra mig, og der tilstøder ham en Ulykke, bringer I mine graa Haar i Dødsriget med Smerte! (Sheol h7585)
Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’ (Sheol h7585)
30 Kommer jeg derfor hjem til din Træl, min Fader, uden at Drengen, ved hvem han hænger med hele sin Sjæl, er med,
“Tsono ngati tizibwerera kwa mtumiki wanu, abambo athu popanda mnyamatayu, amene moyo wa abambo ake uli pa iyeyu,
31 saa bliver det hans Død, naar han ser, at Drengen ikke er med, og dine Trælle vil bringe din Træl vor Faders graa Haar i Dødsriget med Sorg. (Sheol h7585)
ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. (Sheol h7585)
32 Men din Træl skal svare sin Fader for Drengen, og jeg har forpligtet mig til at være hans Skyldner for bestandig, hvis jeg ikke bringer ham til ham;
Ndiponsotu ine ndinadzipereka kwa abambo anga kukhala chikole chotsimikiza kuti mnyamatayu ndidzamuteteza, ndipo ndinati, ‘Ngati sindibwerera naye mnyamatayu kwa inu, ndiye kuti ndidzakhala wochimwira inu abambo anga moyo wanga wonse.’
33 lad derfor din Træl blive tilbage i Drengens Sted som min Herres Træl, men lad Drengen drage hjem med sine Brødre!
“Tsono, chonde mulole kuti ine kapolo wanu nditsalire kuno kukhala kapolo wa mbuye wathu mʼmalo mwa mnyamatayu. Koma iye apite pamodzi ndi abale akewa.
34 Thi hvorledes skulde jeg kunne drage hjem til min Fader, naar jeg ikke har Drengen med? Jeg vil ikke kunne være Vidne til den Ulykke, der rammer min Fader!«
Ndingabwerere bwanji kwa abambo anga ngati sindingapite ndi mnyamatayu? Ayi! Sindifuna kukaona tsoka limene lingakagwere abambo anga.”

< 1 Mosebog 44 >