< 1 Mosebog 43 >
1 Men Hungersnøden var haard i Landet;
Njala inakula kwambiri mʼdzikomo.
2 og da de havde fortæret det Korn, de havde hentet i Ægypten, sagde deres Fader til dem: »Køb os igen lidt Føde!«
Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”
3 Men Juda svarede ham: »Manden sagde os ganske afgjort: I bliver ikke stedt for mit Aasyn, medmindre eders Broder er med!
Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’
4 Hvis du derfor vil sende vor Broder med os, vil vi rejse ned og købe dig Føde;
Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya.
5 men sender du ham ikke med, saa rejser vi ikke derned, thi Manden sagde til os: I bliver ikke stedt for mit Aasyn, medmindre eders Broder er med!«
Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’”
6 Saa sagde Israel: »Hvorfor handlede I ilde imod mig og fortalte Manden, at I havde en Broder til?«
Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”
7 De svarede: »Manden spurgte os nøje ud om os og vor Slægt og sagde: Lever eders Fader endnu? Har I en Broder til? Og vi svarede ham paa hans Spørgsmaal; kunde vi vide, at han vilde sige: Bring eders Broder herned!«
Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”
8 Men Juda sagde til sin Fader Israel: »Send dog Drengen med mig, saa vi kan komme af Sted og blive i Live og undgaa Døden, baade vi og du og vore Børn!
Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo.
9 Jeg svarer for ham, af min Haand maa du kræve ham: bringer jeg ham ikke til dig og stiller ham for dit Aasyn, vil jeg være din Skyldner for bestandig;
Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse.
10 havde vi nu ikke spildt Tiden, kunde vi have været tilbage to Gange!«
Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”
11 Saa sagde deres Fader Israel til dem: »Kan det ikke være anderledes, gør da i alt Fald saaledes: Tag noget af det bedste, Landet frembringer, med i eders Sække og bring Manden en Gave, lidt Mastiksbalsam, lidt Honning, Tragakantgummi, Cistusharpiks, Pistacienødder og Mandler;
Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
12 og tag dobbelt saa mange Penge med, saa I bringer de Penge tilbage, som var lagt oven i eders Sække; maaske var det en Fejltagelse;
Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa.
13 og tag saa eders Broder og drag atter til Manden!
Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga.
14 Gud den Almægtige lade eder finde Barmhjertighed hos Manden, saa han lader eders anden Broder og Benjamin fare — men skal jeg være barnløs, saa lad mig da blive det!«
Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”
15 Saa tog Mændene deres Gave og dobbelt saa mange Penge med; ogsaa Benjamin tog de med, brød op og drog ned til Ægypten, hvor de fremstillede sig for Josef.
Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe.
16 Da Josef saa Benjamin iblandt dem, sagde han til sin Hushovmester: »Bring de Mænd ind i mit Hus, lad slagte og lave til, thi de skal spise til Middag hos mig.«
Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”
17 Manden gjorde, som Josef bød, og førte Mændene ind i Josefs Hus.
Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe.
18 Men Mændene blev bange, da de førtes ind i Josefs Hus, og sagde: »Det er for de Penges Skyld, der forrige Gang kom tilbage i vore Sække, at vi føres herind, for at de kan vælte sig ind paa os og kaste sig over os, gøre os til Trælle og tage vore Æsler.«
Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”
19 Derfor traadte de hen til Josefs Hushovmester ved Døren til Huset
Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti,
20 og sagde: »Hør os, Herre! Vi drog en Gang før herned for at købe Føde,
“Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya
21 og da vi kom til vort Natteherberge og aabnede vore Sække, se, da laa vore Penge oven i hver enkelts Sæk, vore Penge til sidste Hvid. Men nu har vi bragt dem med tilbage
koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo.
22 og desuden andre Penge for at købe Føde. Vi ved ikke, hvem der har lagt Pengene i vore Sække!«
Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”
23 Men han svarede: »Vær ved godt Mod, frygt ikke! Eders Gud og eders Faders Gud har lagt en Skat i eders Sække — eders Penge har jeg modtaget!« Og han førte Simeon ud til dem.
Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.
24 Saa førte Manden dem ind i Josefs Hus og gav dem Vand til at tvætte deres Fødder og Foder til Æslerne.
Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo.
25 Og de fremtog deres Gave, før Josef kom hjem ved Middagstid, thi de hørte, at de skulde spise der.
Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.
26 Da Josef traadte ind i Huset, bragte de ham den Gave, de havde med, og kastede sig til Jorden for ham.
Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi.
27 Han hilste paa dem og spurgte: »Gaar det eders gamle Fader vel, ham, I talte om? Lever han endnu?«
Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”
28 De svarede: »Det gaar din Træl, vor Fader, vel; han lever endnu!« Og de bøjede sig og kastede sig til Jorden.
Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.
29 Da han saa fik Øje paa sin kødelige Broder Benjamin, sagde han: »Er det saa eders yngste Broder, som I talte til mig om?« Og han sagde: »Gud være dig naadig, min Søn!«
Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.”
30 Men Josef brød hurtigt af, thi Kærligheden til Broderen blussede op i ham, og han kæmpede med Graaden; derfor gik han ind i sit Kammer og græd der.
Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.
31 Men da han havde badet sit Ansigt, kom han ud, og han beherskede sig og sagde: »Sæt Maden frem!«
Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.
32 Saa blev Maden sat frem særskilt for ham og for dem og for de Ægyptere, der spiste hos ham; thi Ægypterne kan ikke spise sammen med Hebræere, det er dem en Vederstyggelighed.
Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri.
33 De blev bænket foran ham efter Alder, den førstefødte øverst og den yngste nederst, og Mændene undrede sig og saa paa hverandre;
Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa.
34 og han lod dem bringe Mad fra sit eget Bord, og Benjamin fik fem Gange saa meget som hver af de andre. Og de drak og blev lystige sammen med ham.
Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.