< 2 Mosebog 33 >
1 HERREN sagde til Moses: »Drag nu bort herfra med Folket, som du førte ud af Ægypten, til det Land, jeg tilsvor Abraham, Isak og Jakob med de Ord: Dit Afkom vil jeg give det! —
Ndipo Yehova anati, “Chokani pa malo ano, iwe ndi anthu amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto. Pitani ku dziko limene ine ndinalonjeza ndi lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo kuti, ‘Ine ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’
2 Jeg sender en Engel foran dig, og han skal drive Kana'anæerne, Amoriterne, Hetiterne, Perizziterne, Hivviterne og Jebusiterne bort —
Ndipo ndidzatumiza mngelo patsogolo panu kuthamangitsa Akanaani, Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
3 til et Land, der flyder med Mælk og Honning. Men selv vil jeg ikke drage med i din Midte, thi du er et halsstarrigt Folk; drog jeg med, kunde jeg tilintetgøre dig undervejs!«
Pitani ku dziko loyenda mkaka ndi uchi. Koma ine sindidzapita nanu, chifukwa anthu inu ndinu nkhutukumve ndipo nditha kukuwonongani mʼnjiramo.”
4 Da Folket hørte denne onde Tidende, sørgede de, og ingen tog sine Smykker paa.
Anthu atamva mawu owopsawa, anayamba kulira ndipo palibe anavala zodzikometsera.
5 Da sagde HERREN til Moses: »Sig til Israeliterne; I er et halsstarrigt Folk! Vandrede jeg kun et eneste Øjeblik i din Midte, maatte jeg tilintetgøre dig. Tag du dine Smykker af, saa skal jeg tænke over, hvad jeg vil gøre for dig!«
Pakuti Yehova anali atanena kwa Mose kuti, “Awuze Aisraeli kuti, ‘Inu ndinu nkhutukumve.’ Ngati ine ndipita ndi inu kwa kanthawi, nditha kukuwonongani. Tsopano vulani zodzikometsera zanu ndipo ine ndidzaganiza choti ndichite nanu.”
6 Da aflagde Israeliterne deres Smykker fra Horebs Bjerg af.
Kotero Aisraeli anavula zodzikometsera zawo pa phiri la Horebu.
7 Moses plejede at tage Teltet og slaa det op udenfor Lejren i nogen Afstand derfra; han gav det Navnet »Aabenbaringsteltet«. Enhver som vilde raadspørge HERREN, gik ud til Aabenbaringsteltet uden for Lejren.
Tsono Mose ankatenga tenti ndi kukayimanga kunja kwa msasa chapatalipo, ndipo ankayitcha “tenti ya msonkhano.” Aliyense wofuna kukafunsa kanthu kwa Yehova amapita ku tenti ya msonkhano kunja kwa msasa.
8 Men hver Gang Moses gik ud til Teltet, rejste alt Folket sig op og stillede sig alle ved Indgangen til deres Telte og saa efter Moses, indtil han kom ind i Teltet.
Ndipo nthawi ina iliyonse imene Mose amapita ku tenti anthu onse amanyamuka ndi kuyimirira pa makomo amatenti awo, kumuyangʼana Mose mpaka atalowa mu tentimo.
9 Og naar Moses kom ind Teltet, sænkede Skystøtten sig og stillede sig ved Indgangen til Teltet; da talede HERREN med Moses.
Mose akamalowa mu tenti, chipilala cha mtambo chimatsika ndi kukhala pa khomo pamene Yehova amayankhula ndi Mose.
10 Men naar alt Folket saa Skystøtten staa ved Indgangen til Teltet, rejste de sig alle op og tilbad ved Indgangen til deres Telte.
Nthawi zonse anthu akaona chipilala cha mtambo chitayima pa khomo la tentiyo amayimirira ndi kupembedza, aliyense ali pa khomo la tenti yake.
11 Saa talede HERREN med Moses Ansigt til Ansigt, som naar den ene Mand taler med den anden, og derpaa vendte Moses tilbage til Lejren; men hans Medhjælper Josua, Nuns Søn, en ung Mand, veg ikke fra Teltet.
Yehova amayankhula ndi Mose maso ndi maso ngati mmene munthu amayankhulira ndi bwenzi lake. Kenaka Mose amabwerera ku msasa koma womuthandiza wake, Yoswa, mwana wa Nuni samachoka pa tentiyo.
12 Moses sagde til HERREN: »Se, du siger til mig: Før dette Folk frem! Men du har ikke ladet mig vide, hvem du vil sende med mig; og dog har du sagt: Jeg kender dig ved Navn, og du har fundet Naade for mine Øjne!
Mose anati kwa Yehova, “Inu mwakhala mukundiwuza kuti, ‘Tsogolera anthu awa,’ koma simunandiwuze amene mudzamutuma kuti apite pamodzi nane. Inu mwanena kuti, ‘Ndikukudziwa bwino kwambiri ndipo wapeza chisomo pamaso panga.’
13 Hvis jeg nu virkelig har fundet Naade for dine Øjne, saa lær mig dine Veje at kende, at jeg kan kende dig og finde Naade for dine Øjne; tænk dog paa, at dette Folk er dit Folk!«
Ngati mwakondwera nane ndiphunzitseni njira zanu kuti ndikudziweni ndi kupitiriza kupeza chisomo pamaso panu. Kumbukirani kuti mtundu uwu ndi anthu anu.”
14 Han svarede: »Skal mit Aasyn da vandre med, og skal jeg saaledes føre dig til Maalet?«
Yehova anayankha kuti, “Ine ndemwe ndidzapita pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakupatsa mpumulo.”
15 Da sagde Moses til ham: »Hvis dit Aasyn ikke vandrer med, saa lad os ikke drage herfra!
Kenaka Mose anati kwa Yehova, “Ngati inu simupita nafe, musatitumize kuti tipite, kutichotsa pano.
16 Hvorpaa skal det dog kendes, at jeg har fundet Naade for dine Øjne, jeg og dit Folk? Mon ikke paa, at du vandrer med os, og der saaledes vises os, mig og dit Folk, en Udmærkelse fremfor alle andre Folkeslag paa Jorden?«
Kodi wina adzadziwa bwanji kuti inu mwandikomera mtima pamodzi ndi anthu awa ngati simupita nafe? Kodi nʼchiyani chomwe chidzatisiyanitse pakati pa anthu onse amene ali pa dziko lapansi?”
17 HERREN svarede Moses: »Ogsaa hvad du der siger, vil jeg gøre, thi du har fundet Naade for mine Øjne, og jeg kalder dig ved Navn.«
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzachita zimene iwe wandipempha chifukwa Ine ndikukondwera nawe, ndikukudziwa bwino lomwe.”
18 Da sagde Moses: »Lad mig dog skue din Herlighed!«
Kenaka Mose anati, “Tsopano ndionetseni ulemerero wanu.”
19 Han svarede: »Jeg vil lade al min Rigdom drage forbi dig og udraabe HERRENS Navn foran dig, thi jeg viser Naade, mod hvem jeg vil, og Barmhjertighed, mod hvem jeg vil!«
Ndipo Yehova anati, “Ine ndidzakuonetsa ulemerero wanga wonse ndipo ndidzatchula dzina langa lakuti Yehova pamaso pako. Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”
20 Og han sagde: »Du kan ikke skue mit Aasyn, thi intet Menneske kan se mig og leve.«
Iye anati, “Koma iwe sungaone nkhope yanga, pakuti palibe munthu amene amaona Ine nakhala ndi moyo.”
21 Og HERREN sagde: »Se, her er et Sted i min Nærhed, stil dig paa Klippen der!
Ndipo Yehova anati, “Pali malo pafupi ndi ine pomwe ungathe kuyima pa thanthwe.
22 Naar da min Herlighed drager forbi, vil jeg lade dig staa i Klippehulen, og jeg vil dække dig med min Haand, indtil jeg er kommet forbi.
Pamene ulemerero wanga udutsa, ndidzakuyika mʼphanga la thanthwe ndi kukuphimba ndi dzanja langa mpaka nditadutsa.
23 Saa tager jeg min Haand bort, og da kan du se mig bagfra; men mit Aasyn kan ingen skue!«
Kenaka ine ndidzachotsa dzanja langa ndipo iwe udzaona msana wanga, koma nkhope yanga sidzaoneka.”