< 2 Mosebog 3 >
1 Moses vogtede nu Smaakvæget for sin Svigerfader Jetro, Præsten i Midjan, og drev engang Smaakvæget hen hinsides Ørkenen og kom til Guds Bjerg Horeb.
Tsono Mose amaweta ziweto za mpongozi wake Yetero, wansembe uja wa ku Midiyani. Tsiku lina iye anazitsogolera kupita ku chipululu ndipo anafika ku phiri la Mulungu lotchedwa Horebu.
2 Da aabenbarede HERRENS Engel sig for ham i en Ildslue, der slog ud af en Tornebusk, og da han saa nærmere til, se, da stod Tornebusken i lys Lue, uden at den blev fortæret.
Kumeneko mngelo wa Yehova anaonekera kwa iye mʼmalawi amoto mʼchitsamba. Mose anaona kuti ngakhale chitsambacho chimayaka koma sichimanyeka.
3 Da sagde Moses: »Lad mig gaa hen og se paa dette underfulde Skue, hvorfor Tornebusken ikke brænder op.«
Tsono Mose anati mu mtima mwake, “Ine ndipita komweko ndikaone zodabwitsazi, chitsamba sichikunyeka chifukwa chiyani?”
4 Men da HERREN saa, at han gik hen for at se derpaa, raabte Gud til ham fra Tornebusken: »Moses, Moses!« Og han svarede: »Se, her er jeg!«
Yehova ataona kuti Mose anapatuka kuti adzaonetsetse, Mulungu anamuyitana Mose kuchokera mʼchitsambamo nati, “Mose! Mose!” Ndipo anayankha, “Wawa.”
5 Da sagde han: »Kom ikke nærmere! Drag dine Sko af dine Fødder, thi det Sted, du staar paa, er hellig Jord!«
Mulungu anati, “Usayandikire kuno. Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.”
6 Og han sagde: »Jeg er din Faders Gud, Abrahams Gud, Isaks Gud og Jakobs Gud.« Da skjulte Moses sit Ansigt, thi han frygtede for at skue Gud.
Mulungu anati, “Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo.” Atamva zimenezi, Mose anaphimba nkhope yake chifukwa anaopa kuona Mulungu.
7 Derpaa sagde HERREN: »Jeg har set mit Folks Elendighed i Ægypten, og jeg har hørt deres Klageskrig over deres Undertrykkere, ja, jeg kender deres Lidelser;
Yehova anati, “Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo chifukwa cha anthu amene akuwapsinja, ndipo ndakhudzidwa ndi masautso awo.
8 og jeg er steget ned for at udfri dem af Ægyptens Haand og føre dem bort fra dette Land til et godt og vidtstrakt Land, til et Land, der flyder med Mælk og Honning, til Kana'anæernes, Hetiternes, Amoriternes, Perizziternes, Hivviternes og Jebusiternes Egn.
Choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse mʼdzanja la Aigupto, kuwatulutsa mʼdzikolo ndi kukawalowetsa mʼdziko labwino ndi lalikulu, dziko loyenda mkaka ndi uchi, kwawo kwa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
9 Se, nu er Israeliternes Klageskrig naaet til mig, og jeg har ogsaa set den Trængsel, Ægypterne har bragt over dem.
Ine ndamva ndithu kulira kwa Aisraeli, ndipo ndaona mmene Aigupto akuwazunzira.
10 Derfor vil jeg nu sende dig til Farao, og du skal føre mit Folk, Israeliterne, ud af Ægypten!«
Kotero tsopano, pita. Ine ndikukutuma kwa Farao kuti ukatulutse anthu anga, Aisraeli mʼdziko la Igupto.”
11 Men Moses sagde til Gud: »Hvem er jeg, at jeg skulde kunne gaa til Farao og føre Israeliterne ud af Ægypten?«
Koma Mose anafunsa Mulungu, “Ine ndine yani kuti ndipite kwa Farao ndi kukatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto?”
12 Han svarede: »Jo, jeg vil være med dig! Og dette skal være dig Tegnet paa, at det er mig, der har sendt dig: Naar du har ført Folket ud af Ægypten, skal I dyrke Gud paa dette Bjerg!«
Ndipo Mulungu anati, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro kwa iwe kuti ndine amene ndakutuma; Ukadzatulutsa anthu anga mʼdziko la Igupto, udzapembedza Mulungu pa phiri lino.”
13 Men Moses sagde til Gud: »Naar jeg kommer til Israeliterne og siger dem, at deres Fædres Gud har sendt mig til dem, hvad skal jeg saa svare dem, hvis de spørger om hans Navn?«
Mose anati kwa Mulungu, “Ngati ndipita kwa Aisraeli ndi kukawawuza kuti, ‘Mulungu wa makolo anu wandituma kwa inu,’ ndipo iwo nʼkukandifunsa kuti ‘Dzina lake ndi ndani?’ Tsono ine ndikawawuze chiyani?”
14 Gud svarede Moses: »Jeg er den, jeg er!« Og han sagde: »Saaledes skal du sige til Israeliterne: JEG ER har sendt mig til eder!«
Mulungu anati kwa Mose, “NDINE AMENE NDILI. Izi ndi zimene ukanene kwa Aisraeli: ‘NDINE wandituma kwa inu.’”
15 Og Gud sagde fremdeles til Moses: »Saaledes skal du sige til Israeliterne: HERREN, eders Fædres Gud, Abrahams Gud, Isaks Gud og Jakobs Gud, har sendt mig til eder; dette er mit Navn til evig Tid, og saaledes skal jeg kaldes fra Slægt til Slægt.
Mulungu anatinso kwa Mose, “Ukanene kwa Aisraeli kuti ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo, wandituma kwa inu.’ Ili ndilo dzina langa mpaka muyaya, ndipo mibado ya mʼtsogolomo izidzanditchula ndi dzina limeneli.
16 Gaa nu hen og kald Israels Ældste sammen og sig til dem: HERREN, eders Fædres Gud, Abrahams, Isaks og Jakobs Gud, har aabenbaret sig for mig og sagt: Jeg har givet Agt paa eder og paa, hvad man har gjort imod eder i Ægypten,
“Pita, ukawasonkhanitse akuluakulu a Israeli ndipo ukati kwa iwo, ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, anandionekera ndipo akuti Iye wadzakuyenderani ndipo waona mmene Aigupto akukuzunzirani.
17 og jeg har sat mig for at føre eder ud af Ægyptens Elendighed til Kana'anæernes, Hetiternes, Amoriternes, Perizziternes, Hivviternes og Jebusiternes Land, til et Land, der flyder med Mælk og Honning!
Choncho wanenetsa kuti adzakutulutsani mʼdziko la Igupto, dziko la masautsoli kupita ku dziko la Akanaani, Ahiti, Aamori Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’
18 De vil høre paa dig, og du skal sammen med Israels Ældste gaa til Ægypterkongen, og I skal sige til ham: HERREN, Hebræernes Gud, har mødt os, tillad os derfor at drage tre Dagsrejser ud i Ørkenen og ofre til HERREN vor Gud!
“Akuluakulu a Israeli akakumvera. Kenaka iwe ndi akuluakuluwo mukapite kwa mfumu ya Igupto ndipo mukanene kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri, wakumana nafe. Tsono tikukupemphani kuti mutilole tipite pa ulendo wa masiku atatu mʼchipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu.’
19 Jeg ved vel, at Ægypterkongen ikke vil tillade eder at drage bort uden med Magt;
Koma Ine ndikudziwa kuti mfumu ya Igupto sikakulolani kuti mupite pokhapokha Ine nditayikakamiza.
20 men jeg skal udrække min Haand og ramme Ægypten med alle mine Undergerninger, som jeg vil gøre der; saa skal han give eder Lov til at drage af Sted.
Tsono Ine ndidzatambasula dzanja langa ndi kukantha Aigupto ndi zodabwitsa zanga zimene ndidzazichita pakati pawo. Zikadzatha izi, Iye adzakulolani kuti mupite.
21 Og jeg vil stemme Ægypterne gunstigt mod dette Folk, saa at I, naar I drager bort, ikke skal drage bort med tomme Hænder.
“Ndipo ine ndidzafewetsa mtima wa Aigupto pa anthu anga, kotero kuti mukadzatuluka simudzapita wopanda kanthu.
22 Enhver Kvinde skal bede sin Naboerske og de Kvinder, som er til Huse hos hende, om Sølv og Guldsmykker og Klæder, og I skal give eders Sønner og Døtre det paa. Saaledes skal I tage Bytte fra Ægypterne.«
Mkazi aliyense adzapemphe Mwigupto woyandikana naye ndiponso mkazi amene akukhala mʼnyumba yake, kuti amupatse ziwiya za siliva ndi golide ndiponso zovala zimene mudzaveka ana anu aamuna ndi aakazi. Ndipo potero mudzawalanda zonse Aiguptowo.”