< 2 Mosebog 22 >

1 Naar en Mand stjæler en Okse eller et Faar og slagter eller sælger dem, skal han give fem Okser i Erstatning for Oksen og fire Faar for Faaret.
“Ngati munthu aba ngʼombe kapena nkhosa ndi kuyipha kapena kuyigulitsa, iye abweze ngʼombe zisanu pa ngʼombe imodzi ndi nkhosa zinayi pa nkhosa imodzi.
2 (Hvis en Tyv gribes paa fersk Gerning ved et natligt Indbrud og bliver slaaet ihjel, da bliver der ikke Tale om Blodskyld;
“Ngati mbala ipezeka ikuthyola nyumba ndipo imenyedwa nʼkufa, amene wapha mbalayo sanalakwe.
3 men hvis Solen er staaet op, paadrager man sig Blodskyld). Erstatning skal han give, og ejer han intet, skal han sælges som Træl til Vederlag for det stjaalne;
Koma akayipha dzuwa litatuluka, woyiphayo ali ndi mlandu wakupha. “Mbala iyenera kubweza ndithu koma ngati ilibe kalikonse igulitsidwe, kulipira zomwe yabazo.
4 hvis derimod det stjaalne findes levende i hans Besiddelse, da skal han give dobbelt Erstatning, hvad enten det er en Okse, et Æsel, eller et Faar.
“Ngati chiweto chobedwacho chipezeka chamoyo mʼmanja mwake, kaya ndi ngʼombe kapena bulu kapena nkhosa, mbalayo ibwezere ziweto ziwiri pa chiweto chobedwacho.
5 Naar en Mand afsvider en Mark eller en Vingaard og lader Ilden brede sig, saa den antænder en andens Mark, da skal han give det bedste af sin Mark eller Vingaard i Erstatning;
“Ngati munthu alekerera ziweto zake kukalowa mʼmunda wa munthu wina kukadya mbewu zake, munthuyo amubwezere mwini mundawo mbewu zina zabwino kapena mpesa wina wabwino kwambiri.
6 men breder Ilden sig ved at tage fat i Tjørnekrat, og Kornneg eller Sæd brænder, eller en Mark svides af, saa skal den, der antændte Ilden, give simpel Erstatning.
“Ngati munthu ayatsa moto, motowo ndikukafika mpaka ku munda ndi kuwotcha mulu wa tirigu kapena tirigu wosadula, kapena munda wonse, ndiye kuti munthu amene anayatsa motoyo alipire.
7 Naar en Mand giver en anden Penge eller Sager i Varetægt, og de stjæles fra hans Hus, da skal Tyven, hvis han findes, give dobbelt Erstatning;
“Ngati munthu asungitsidwa ndi mnzake ndalama kapena katundu, ndipo zinthu zija nʼkubedwa mʼnyumba mwake, wakubayo ngati agwidwa, ayenera kubwezera kawiri chobedwacho.
8 men hvis Tyven ikke findes, skal Husets Ejer træde frem for Gud og sværge paa, at han ikke har forgrebet sig paa den andens Gods.
Koma ngati mbalayo sipezeka, mwini nyumbayo ayenera kukaonekera ku bwalo lamilandu kuti akamve ngati anaba katundu wa mnzakeyo.
9 I alle Tilfælde hvor det drejer sig om Uredelighed med en Okse, et Æsel, et Faar, en Klædning eller en hvilken som helst bortkommen Ting, hvorom der rejses Krav, skal de to Parters Sag bringes frem for Gud, og den, som Gud dømmer skyldig, skal give den anden dobbelt Erstatning.
Ngati pali kukangana kokhudza ngʼombe, bulu, nkhosa, zovala kapena kanthu kalikonse kotayika, ndipo mmodzi ndikunena kuti chinthucho nʼchake, awiriwo abwere nawo mlandu wawowo pamaso pa Mulungu ndipo amene mlandu umugomere adzayenera kumulipira mnzakeyo kawiri.
10 Naar en Mand giver en anden et Æsel, en Okse, et Faar eller et andet Stykke Kvæg i Varetægt, og Dyret dør, kommer til Skade eller røves, uden at nogen ser det,
“Ngati munthu wina anasungitsa mnzake bulu, ngʼombe, nkhosa, kapena chiweto chilichonse ndipo chiweto chija nʼkufa kapena kupweteka kapena kutengedwa popanda wina kuona,
11 da skal han sværge ved HERREN paa, at han ikke har forgrebet sig paa den andens Ejendom, og det skal være afgørende imellem dem; Dyrets Ejer skal tage Eden god, og den anden behøver ikke at give Erstatning.
ndiye kuti anthu awiriwo ayenera kulumbira pamaso pa Mulungu kuti asatenge chinthu cha mnzake. Zikatero mwini katundu uja avomereze zimenezi ndipo asabwezeredwe kanthu.
12 Stjæles det derimod fra ham, skal han give Ejeren Erstatning.
Koma ngati chiwetocho chinabedwa, iye ayenera kubwezera mwini wakeyo.
13 Hvis det sønderrives, skal han bringe det sønderrevne Dyr med som Bevis; det sønderrevne skal han ikke erstatte.
Ngati chinagwidwa ndi zirombo, iye ayenera kubweretsa zotsalira ngati umboni ndipo sadzalipira kanthu.
14 Naar en laaner et Dyr af en anden, og det kommer til Skade eller dør, uden at Ejeren er til Stede, skal han give Erstatning;
“Ngati munthu abwereka chiweto cha mnzake ndipo chiweto chija nʼkuvulala kapena kufa chikanali ndi iyebe, wobwerekayo ayenera kulipira.
15 er Ejeren derimod til Stede, skal han ikke give Erstatning; var det lejet, er Lejesummen Erstatning.
Koma ngati mwini wakeyo ali ndi chiwetocho, wobwerekayo sadzalipira. Ngati anapereka ndalama pobwereka chiwetocho, ndalama anaperekazo zilowa mʼmalo mwa chiweto chakufacho.
16 Naar en Mand forfører en Jomfru, der ikke er trolovet, og ligger hos hende, skal han udrede Brudekøbesummen for hende og tage hende til Hustru;
“Ngati munthu anyenga namwali wosadziwa mwamuna amene sanapalidwe ubwenzi ndi kugona naye, munthuyo ayenera kulipira malowolo ndipo adzakhala mkazi wake.
17 og hvis hendes Fader vægrer sig ved at give ham hende, skal han tilveje ham den sædvanlige Brudekøbesum for en Jomfru.
Ngati abambo ake akanitsitsa kwamtuwagalu kumupereka kuti amukwatire, munthuyo aperekebe malowolo woyenera namwaliyo.
18 En Troldkvinde maa du ikke lade leve.
“Musayilole mfiti yayikazi kuti ikhale ndi moyo.
19 Enhver, der har Omgang med Kvæg, skal lide Døden.
“Aliyense wogonana ndi chiweto ayenera kuphedwa.
20 Den, der ofrer til andre Guder end HERREN alene, skal der lægges Band paa.
“Aliyense wopereka nsembe kwa mulungu wina osati Yehova awonongedwe.
21 Den fremmede maa du ikke undertrykke eller forulempe, thi I var selv fremmede i Ægypten.
“Musazunze mlendo kapena kumuchitira nkhanza, pakuti inu munali alendo mʼdziko la Igupto.
22 Enken eller den faderløse maa I aldrig mishandle;
“Musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye.
23 hvis I mishandler dem, og de raaber om Hjælp til mig, vil jeg visselig høre paa deres Klageraab,
Ngati muwazunza ndipo iwo nʼkulirira kwa Ine, ndidzamva kulira kwawo.
24 og da vil min Vrede blusse op, og jeg vil slaa eder ihjel med Sværdet, saa eders egne Hustruer bliver Enker og eders Børn faderløse.
Ine ndidzakukwiyirani ndipo ndidzakuphani ndi lupanga. Akazi anu adzakhala amasiye ndiponso ana anu adzakhala wopanda abambo.
25 Naar du laaner Penge til en fattig Mand af mit Folk i dit Nabolag, maa du ikke optræde som en Aagerkarl over for ham. I maa ikke tage Renter af ham.
“Ngati mukongoza ndalama kwa mʼbale wanu amene ndi mʼmphawi pakati panu, musadzamuchite monga zimene amachita wokongoza ndalama. Musadzamuyikire chiwongoladzanja.
26 Hvis du tager din Næstes Kappe i Pant, skal du give ham den tilbage inden Solnedgang;
Mukatenga chovala cha mnzanu kuti chikhale chikole mumubwezere dzuwa lisanalowe
27 thi den er det eneste, han har at dække sig med, det er den, han hyller sit Legeme i; hvad skulde han ellers ligge med? Og naar han raaber til mig, vil jeg høre ham, thi jeg er barmhjertig.
chifukwa chovala chimene amadzifundira nacho nʼchomwecho. Nanga usiku adzafunda chiyani? Tsonotu ngati adzandilirira, Ine ndidzamva pakuti ndine wachifundo.
28 Gud maa du ikke spotte, og dit Folks Øvrighed maa du ikke forbande.
“Musachite chipongwe Mulungu wanu kapena kutemberera mtsogoleri wa anthu anu.
29 Din Lades Overflod og din Vinperses Saft maa du ikke holde tilbage. Den førstefødte af dine Sønner skal du give mig.
“Musachedwe kupereka kwa Ine zokolola zanu zochuluka ndi vinyo wanu wochuluka. “Mundipatse ana anu achisamba aamuna.
30 Ligesaa skal du gøre med dit Hornkvæg og dit Smaakvæg; i syv Dage skal det blive hos Moderen, men paa den ottende Dag skal I give mig det.
Muchite chimodzimodzi ndi ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu. Mwana woyamba kubadwa azikhala ndi amayi ake masiku asanu ndi awiri. Koma pa tsiku lachisanu ndi chitatu mwanayo muzimupereka kwa Ine.
31 I skal være mig hellige Mænd; Kød af sønderrevne Dyr maa I ikke spise, I skal kaste det for Hundene.
“Inu mukhale anthu anga opatulika. Choncho musadye nyama ya chiweto chimene chaphedwa ndi zirombo. Nyamayo muwaponyere agalu.”

< 2 Mosebog 22 >