< Ester 6 >
1 Samme Nat veg Søvnen fra Kongen. Da bød han, at man skulde hente Krøniken, i hvilken mindeværdige Tildragelser var optegnet, og man læste op for Kongen af den.
Usiku umenewo mfumu inalephera kugona tulo; Choncho inayitanitsa buku limene amalembamo mbiri ya zamakedzana kuti amuwerengere.
2 Man fandt da optegnet, hvorledes Mordokaj havde meldt, at Bigtana og Teresj, to kongelige Hofmænd, der hørte til Dørvogterne, havde søgt Lejlighed til at lægge Haand paa Kong Ahasverus.
Anapeza kuti mʼbukumo munalembedwa zoti Mordekai anawulula kuti Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa a mfumu amene ankalondera pa khomo la chipinda cha mfumu ndiwo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
3 Kongen spurgte da: »Hvilken Ære og Udmærkelse er der vist Mordokaj til Gengæld?« Kongens Folk, som gik ham til Haande, svarede: »Der er ingen Ære vist ham.«
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi Mordekai anamupatsa ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha chinthu chimene anachitachi?” Atumiki ake anamuyankha kuti, “Palibe chimene chinachitika kwa iye.”
4 Saa spurgte Kongen: Hvem er ude i Gaarden? Haman var netop kommet ind i den ydre Gaard til Kongens Palads for at bede Kongen om, at Mordokaj maatte blive hængt i den Galge, han havde rejst til ham.
Mfumu inati, “Kodi ndani ali mʼbwalomo?” Tsono Hamani anali atangolowa kumene mʼbwalo lakunja la nyumba yaufumu kuti akawuze mfumu zomukhomera Mordekai pa mtanda umene anamukonzera.
5 Kongens Folk svarede ham: »Det er Haman, der staar ude i Gaarden.« Da sagde Kongen: »Lad ham komme ind!«
Atumiki ake anamuyankha kuti, “Hamani ndiye wayima mu bwalo.” “Mulowetseni,” Mfumu inalamulira.
6 Da Haman var kommet ind; sagde Kongen til ham: »Hvad gør man ved den Mand, Kongen ønsker at hædre?« Haman tænkte ved sig selv: »Hvem andre end mig skulde Kongen ønske at hædre?«
Hamani atalowa, mfumu inamufunsa kuti, “Kodi timuchitire ulemu otani munthu amene mfumu ikondweretsedwa naye?” Tsono Hamani anaganiza mu mtima kuti, “Kodi palinso ndani amene mfumu ingamulemekeze kuposa ine?”
7 Derfor svarede Haman Kongen: »Hvis Kongen ønsker at hædre en Mand,
Choncho Hamani anayankha mfumuyo kuti, “Munthu amene mfumu ifuna kumuchitira ulemu, imuchitire izi:
8 skal man lade hente en kongelig Klædning, som Kongen selv har baaret, og en Hest, som Kongen selv har redet, og paa hvis Hoved der er sat en kongelig Krone,
Anthu abwere ndi chovala cha ufumu ndi kavalo amene mfumu imakwerapo wokhala ndi chizindikiro chaufumu pamutu pake.
9 og man skal overgive Klædningen og Hesten til en af Kongens ypperste Fyrster og give den Mand, Kongen ønsker at hædre, Klædningen paa og føre ham paa Hesten over Byens Torv og raabe foran ham: Saaledes gør man ved den Mand, Kongen ønsker at hædre!«
Ndipo mupereke chovala cha ufumucho ndi kavalo kwa mmodzi wa akalonga a mfumu a ulemu kwambiri. Ameneyu amuveke chovalacho munthu amene mfumu yakondweretsedwa naye. Akavekedwa chovalachi amuyendetse mʼmisewu yonse ya mzinda atakwera pa kavalo wa mfumu. Kalongayu azifuwula patsogolo pa munthuyu kuti ‘Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!’”
10 Da sagde Kongen til Haman: »Skynd dig at hente Klædningen og Hesten, som du sagde, og gør saaledes ved Jøden Mordokaj, som sidder i den kongelige Port! Undlad intet af, hvad du sagde!«
Mfumu inalamulira Hamani kuti, “Pita msanga, katenge chovala cha ufumu ndi kavalo ndipo uchite monga wanenera kwa Mordekai Myuda, amene amakhala pa chipata cha mfumu. Usasiyeko china chilichonse chimene wanena.”
11 Saa hentede Haman Klædningen og Hesten, gav Mordokaj Klædningen paa og førte ham paa Hesten over Byens Torv og raabte foran ham: »Saaledes gør man ved den Mand, Kongen ønsker at hædre!«
Choncho Hamani anatenga chovala ndi kavalo. Anamuveka Mordekai chovalacho ndipo anamuyendetsa mʼmisewu yonse ya mu mzinda atakwera pa kavalo, akufuwula kuti, “Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!”
12 Derefter gik Mordokaj tilbage til Kongens Port. Men Haman skyndte sig hjem, nedslaaet og med tilhyllet Hoved.
Pambuyo pake Mordekai anabwerera ku chipata cha mfumu. Koma Hamani anapita msanga ku nyumba kwake, akulira, atafundira mutu wake.
13 Og Haman fortalte sin Hustru Zeresj og alle sine Venner alt, hvad der var hændet ham. Da sagde hans Venner og hans Hustru Zeresj til ham: Hvis Mordokaj, over for hvem du nu for første Gang er kommet til kort, er af jødisk Æt, saa kan du intet udrette imod ham, men det bliver dit Fald til sidst!
Hamani anawuza Zeresi mkazi wake ndi abwenzi ake onse zonse zinamuchitikira. Anthu ake anzeru ndi mkazi wake Zeresi anamuwuza kuti, “Popeza kuti Mordekai ndi Myuda amene mwayamba kale kugonja pamaso pake, ndiye kuti palibe chimene mungachitepo. Mudzagwa ndithu pamaso pake.”
14 Medens de endnu talte med ham, indtraf de kongelige Hofmænd for hurtigt at hente Haman til det Gæstebud, Ester havde gjort rede.
Pamene anthuwa amayankhula nayebe, adindo a mfumu ofulidwa anabwera kudzamutenga Hamani mofulumira kupita naye ku phwando limene Estere anakonza.